Numeri 14 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 14:1-45

Anthu Awukira

1Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri. 2Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno! 3Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?” 4Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”

5Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo. 6Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo 7ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi. 8Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife, 9koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”

10Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano. 11Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo? 12Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”

13Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo. 14Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku. 15Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati, 16‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’

17“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti, 18‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’ 19Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”

20Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera. 21Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova, 22palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi, 23palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo. 24Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo. 25Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”

26Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti, 27“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa. 28Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena: 29Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane. 30Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni. 31Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana. 32Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno. 33Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno. 34Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’ 35Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”

36Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo. 37Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova. 38Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.

39Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri. 40Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”

41Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka! 42Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu 43chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”

44Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa. 45Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.

New Russian Translation

Числа 14:1-45

Мятеж израильтян

1В ту ночь народ поднял крик и громко плакал. 2Израильтяне роптали на Моисея и Аарона. Люди говорили им:

– О если бы мы умерли в Египте! Или здесь, в пустыне! 3Зачем Господь ведет нас в эту землю? Мы падем в ней от меча, а наши жены и дети попадут в плен. Не лучше ли нам вернуться в Египет? 4Они говорили друг другу:

– Нам нужно выбрать вождя и вернуться в Египет.

5Тогда Моисей и Аарон пали ниц перед собравшимся обществом израильтян. 6Иисус, сын Навин, и Халев, сын Иефонниин, которые были среди тех, кто разведывал землю, разорвали на себе одежду 7и сказали собранию израильтян:

– Земля, через которую мы прошли и которую разведали, необыкновенно хороша. 8Если Господь благосклонен к нам, Он поведет нас в эту землю, где течет молоко и мед, и отдаст ее нам. 9Не восставайте против Господа. Не бойтесь жителей той земли, потому что мы легко одолеем их. Они лишились защиты, а с нами Господь. Не бойтесь их.

10Но народ говорил о том, чтобы побить их камнями. Тогда слава Господа явилась израильтянам у шатра собрания.

Молитва Моисея за народ

11Господь сказал Моисею:

– До каких пор этот народ будет презирать Меня? До каких пор они будут отказываться поверить в Меня, несмотря на все знамения, которые Я совершил среди них? 12Я поражу их мором и истреблю, а от тебя произведу народ больше и сильнее их.

13Моисей сказал Господу:

– Но об этом услышат египтяне, из среды которых Ты вывел Своей силой этот народ, 14и они расскажут всем обитателям этой земли. Они уже слышали, что Ты, Господи, с этим народом и что Ты, Господи, даешь видеть Себя лицом к лицу, что Твое облако стоит над ними, и что Ты идешь перед ними в облачном столбе днем и в огненном ночью. 15Если Ты истребишь весь этот народ, как одного человека, то народы, которые слышали о Тебе, скажут: 16«Господь не смог привести этот народ в землю, которую с клятвой обещал ему. Поэтому Он погубил его в пустыне». 17Пусть откроется теперь сила Владыки, как Ты и говорил: 18«Господь медлен на гнев, богат милостью и прощает грех и отступничество. Но Он не оправдывает виновных, карая детей за грехи отцов до третьего и четвертого поколения». 19По великой Своей любви прости грех этого народа, как прощал ему со времен Египта до сегодняшнего дня.

20Господь ответил:

– Я простил его по твоей просьбе. 21Но, верно, как и то, что Я живу и что слава Господа наполняет всю землю, 22никто из тех, кто видел Мою славу и знамения, которые Я совершил в Египте и в пустыне, но не послушался Меня и испытывал Меня десять раз, 23никто из них не увидит землю, которую Я с клятвой обещал их отцам. Никто из тех, кто презирал Меня, ее не увидит. 24Но у Моего слуги Халева иной дух, и он повинуется Мне от всего сердца. За это Я приведу его в землю, куда он ходил, и его потомки будут ею владеть. 25Раз в долинах живут амаликитяне и хананеи, поверните завтра и ступайте в пустыню к Красному морю.

Наказание за мятеж

26Господь сказал Моисею и Аарону:

27– Сколько еще этот грешный народ будет роптать на Меня? Я слышу все, что говорят израильтяне, когда ропщут на Меня. 28Скажи им: «Верно, как и то, что Я живу, – возвещает Господь, – что вы говорили, то Я и сделаю. 29Ваши трупы будут брошены в этой пустыне, и никто из вас двадцати лет и старше, кто был исчислен при переписи и роптал на Меня, 30не войдет в землю, которую Я, воздев руку, клялся сделать вашим домом, за исключением Халева, сына Иефонниина, и Иисуса, сына Навина. 31Ваших детей, о которых вы говорили, что они попадут в плен, Я приведу, и они узнают землю, которую вы отвергли. 32Что до вас, то ваши трупы будут брошены в этой пустыне. 33Ваши дети будут там пастухами сорок лет, страдая за вашу неверность, пока последний из вас не падет мертвым в пустыне. 34Сорок лет – по году за каждый из сорока дней, в которые вы разведывали землю, – вы будете страдать за свой грех и узнаете, что значит враждовать со Мной». 35Это сказал Я, Господь. Я непременно сделаю так с этим грешным народом, который восстал против Меня. В этой пустыне они сгинут; они все умрут здесь.

36Те, кого Моисей посылал разведать землю, и кто, вернувшись, возмутил народ против него, ругая ту землю, 37эти люди, опорочившие землю, умерли перед Господом от мора. 38Из тех, кто ходил разведать землю, в живых остались только Иисус, сын Навин, и Халев, сын Иефонниин.

39Когда Моисей пересказал это израильтянам, они горько заплакали. 40Встав рано утром, они стали подниматься к вершинам нагорий.

– Мы готовы, – говорили они. – Мы пойдем в тот край, что обещал Господь; мы согрешили.

41Но Моисей сказал:

– Почему вы нарушаете повеление Господа? Успеха вам не будет. 42Не ходите, потому что Господа не будет с вами. Ваши враги разобьют вас, 43ведь там вас встретят амаликитяне и хананеи. Вы отвернулись от Господа, и Его не будет с вами; вы падете от меча.

44Но они дерзнули подняться к вершинам нагорий, хотя ни ковчег Господнего завета, ни Моисей не покидали лагерь14:44 Это означало, что Бог не пошел с ними, и что Он не станет оказывать им помощь в бою. Обычно присутствие Господа в виде облака или огненного столба сопровождало израильский народ, когда они трогались в путь (см. 9:15-23).. 45И амаликитяне с хананеями, жившие в тех нагорьях, спустились, разбили их и гнались за ними всю дорогу до Хормы.