Numeri 14 – CCL & NIRV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 14:1-45

Anthu Awukira

1Usiku umenewo gulu lonse la Aisraeli linalira mofuwula kwambiri. 2Ndipo Aisraeli onse anayankhula motsutsana ndi Mose ndi Aaroni. Gulu lonse linanena kwa iwo kuti, “Kunali bwino tikanafera ku Igupto kapena mʼchipululu muno! 3Nʼchifukwa chiyani Yehova akutilowetsa mʼdziko limenelo? Kodi kuti tikaphedwe ndi lupanga? Kuti akazi ndi ana athu akatengedwe ngati katundu wolanda ku nkhondo? Kodi sikungakhale bwino kuti tibwerere ku Igupto?” 4Ndipo anawuzana wina ndi mnzake kuti, “Tiyeni tisankhe mtsogoleri ndipo tibwerere ku Igupto.”

5Koma Mose ndi Aaroni anadzigwetsa pansi chafufumimba pamaso pa Aisraeli onse omwe anasonkhana pamenepo. 6Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune, omwe anali amodzi mwa amene anakazonda nawo dziko, anangʼamba zovala zawo 7ndipo anati kwa gulu lonse la Aisraeli, “Dziko limene tinakayendamo ndi kuliona ndi labwino kwambiri zedi. 8Ngati Yehova akukondwera nafe, adzatitsogolera kulowa mʼdziko limenelo. Dziko loyenda mkaka ndi uchi adzalipereka kwa ife, 9koma musawukire Yehova. Komanso musaope anthu a mʼdzikomo, pakuti tidzawagonjetsa. Chitetezo chawachokera, koma ife Yehova ali nafe. Musawaope.”

10Koma gulu lonse linayankhula zofuna kuwagenda miyala. Pamenepo ulemerero wa Yehova unaonekera kwa Aisraeli onse ku tenti ya msonkhano. 11Yehova anawuza Mose kuti, “Anthu awa adzandinyoza mpaka liti? Sadzandikhulupirira mpaka liti, ngakhale ndachita zizindikiro zozizwitsa zonsezi pakati pawo? 12Ndidzawakantha ndi mliri ndi kuwawononga. Koma ndidzakusandutsa iwe mtundu waukulu ndi wamphamvu kuposa iwo.”

13Mose anati kwa Yehova, “Aigupto adzamva zimenezi! Mwa mphamvu yanu munawatulutsa anthu amenewa pakati pawo. 14Ndipo iwowo adzawuza anthu okhala mʼdziko lino zimenezi. Anthuwa amva kale kuti Inu Yehova mumakhala pakati pa anthu amenewa ndi kuti Inuyo Yehova mwawaonekera maso ndi maso. Mtambo wanu umakhala pamwamba pawo ndiponso mumayenda nawo mu mtambo woyima, masana ndi moto woyima, usiku. 15Tsono mukawapha anthu onsewa nthawi imodzi, mayiko amene anamva za Inu adzati, 16‘Yehova walephera kuwalowetsa anthuwo mʼdziko lomwe anawalonjeza molumbira, ndipo wawapha mʼchipululu.’

17“Chonde Ambuye wonetsani mphamvu yanu monga munalonjezera kuti, 18‘Yehova sakwiya msanga, ndipo ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika, wokhululukira tchimo ndi kuwukira. Koma Iye sadzaleka kulanga ochimwa. Iyeyo amalanga ana chifukwa cha tchimo la makolo awo kufikira mʼbado wachitatu ndi wachinayi.’ 19Chifukwa cha kukula kwa chikondi chanu chosasinthika, akhululukireni anthuwa tchimo lawo monga mwakhala mukuwakhululukira kuchokera pa nthawi imene anachoka ku Igupto mpaka tsopano.”

20Yehova anayankha kuti, “Ndawakhululukira monga wapemphera. 21Komabe, ndikunenetsa kuti pali Ine, ndiponso pamene dziko lapansi ladzaza ndi ulemerero wa Yehova, 22palibe ndi mmodzi yemwe mwa anthu amene anaona ulemerero wanga ndi zizindikiro zozizwitsa zimene ndinazichita ku Igupto ndi mʼchipululu muno, koma osandimvera ndi kundiyesa kokwanira kakhumi, 23palibe ndi mmodzi yemwe wa anthu amenewa amene adzaone dziko limene ndinalonjeza ndi lumbiro kwa makolo awo. Aliyense amene anandinyoza sadzaliona dzikolo. 24Koma mtumiki wanga Kalebe, pakuti ali ndi mtima wosiyana ndi ena ndiponso amanditsatira ndi mtima wonse, ndidzamulowetsa mʼdziko limene anapitamolo ndipo zidzukulu zake zidzalandira dzikolo ngati cholowa chawo. 25Ndipo popeza kuti Aamaleki ndi Akanaani akukhala ku chigwa, mawa mubwerere ndipo mupite ku chipululu podzera ku Nyanja Yofiira.”

26Yehova anawuza Mose ndi Aaroni kuti, 27“Kodi anthu oyipawa adzangʼungʼudza ndi kutsutsana nane mpaka liti? Ndamva madandawulo a Aisraeli ongʼungʼudzawa. 28Tsono awuze kuti, ‘Ndikulumbira pali Ine,’ akutero Yehova, ‘Ndidzakuchitirani zinthu zonse zimene ndamva inu mukunena: 29Mitembo yanu idzakhala ili ngundangunda mʼchipululu muno; mtembo wa munthu aliyense pakati panu amene ali ndi zaka makumi awiri kapena kupitirirapo, amene anawerengedwa pa chiwerengero chija ndipo anangʼungʼudza motsutsana nane. 30Palibe ndi mmodzi yemwe mwa inu amene adzalowe mʼdziko lomwe ndinalumbira mokweza manja kuti likhale lanu, kupatula Kalebe mwana wa Yefune ndi Yoswa mwana wa Nuni. 31Koma ana anu amene mukunena kuti adzatengedwa ngati katundu wolanda ku nkhondo, Ine ndidzawalowetsa kuti akasangalale mʼdziko limene munalikana. 32Koma inu mitembo yanu idzakhala ngundangunda mʼchipululu muno. 33Ana anu adzakhala abusa mʼchipululu muno zaka makumi anayi, kuvutika chifukwa cha kusakhulupirika kwanu, mpaka munthu womaliza mwa inu atafa mʼchipululu muno. 34Mudzavutika chifukwa cha machimo anu kwa zaka makumi anayi Chaka chimodzi chikuyimira tsiku limodzi la masiku makumi anayi amene munakazonda dziko lija ndipo mudzadziwa kuyipa kwake kwa kukangana ndi Ine.’ 35Ine Yehova, ndanena, ndidzachitadi zimenezi kwa anthu onse oyipawa, amene agwirizana kunditsutsa. Adzathera mʼchipululu momwe muno, adzafera muno basi.”

36Ndipo anthu amene Mose anawatuma kukazonda dziko aja anachoka pamaso pake nachititsa gulu lonse la anthu kuwukira Moseyo chifukwa chofalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo. 37Anthu amene ankafalitsa mbiri yoyipa ya dzikolo anakanthidwa ndi mliri ndipo anafa pamaso pa Yehova. 38Mwa anthu amene anakaona dzikolo, Yoswa mwana wa Nuni ndi Kalebe mwana wa Yefune ndi okhawo amene anapulumuka.

39Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri. 40Mmamawa tsiku linalo anapita mbali ya ku dziko la mapiri. Iwo anati, “Tachimwa, tipita ku dziko limene Yehova anatilonjeza.”

41Koma Mose anati, “Chifukwa chiyani simukumvera lamulo la Yehova? Zimenezi sizitheka! 42Musapite chifukwa Yehova sali pakati panu. Mudzagonjetsedwa ndi adani anu 43chifukwa kumeneko mukakumana ndi Aamaleki ndi Akanaani. Popeza mwaleka kutsata Yehova, Iyeyo sadzakhala nanu ndipo mudzaphedwa ndi lupanga.”

44Komabe mwa maganizo awo anapita molunjika dziko la mapiri ngakhale kuti Mose sanachoke ndi Bokosi la Chipangano la Yehova pa msasa. 45Koma Aamaleki ndi Akanaani amene ankakhala ku dziko lamapirilo anatsika ndi kumenyana nawo ndipo anawakantha mʼnjira yonse mpaka ku Horima.

New International Reader’s Version

Numbers 14:1-45

The People Refuse to Obey the Lord

1That night all the members of the community raised their voices. They wept out loud. 2The Israelites spoke against Moses and Aaron. The whole community said to them, “We wish we had died in Egypt or even in this desert. 3Why is the Lord bringing us to this land? We’re going to be killed by swords. Our enemies will capture our wives and children. Wouldn’t it be better for us to go back to Egypt?” 4They said to one another, “We should choose another leader. We should go back to Egypt.”

5Then Moses and Aaron fell with their faces to the ground. They did it in front of the whole community of Israel gathered there. 6Joshua, the son of Nun, tore his clothes. So did Caleb, the son of Jephunneh. Joshua and Caleb were two of the men who had checked out the land. 7They spoke to the whole community of Israel. They said, “We passed through the land and checked it out. It’s very good. 8If the Lord is pleased with us, he’ll lead us into that land. It’s a land that has plenty of milk and honey. He’ll give it to us. 9But don’t refuse to obey him. And don’t be afraid of the people of the land. We will swallow them up. The Lord is with us. So nothing can save them. Don’t be afraid of them.”

10But all the people talked about killing Joshua and Caleb by throwing stones at them. Then the glory of the Lord appeared at the tent of meeting. All the Israelites saw it. 11The Lord said to Moses, “How long will these people not respect me? How long will they refuse to believe in me? They refuse even though I have done many signs among them. 12So I will strike them down with a plague. I will destroy them. But I will make you into a greater and stronger nation than they are.”

13Moses said to the Lord, “Then the Egyptians will hear about it. You used your power to bring these people up from among them. 14And the Egyptians will tell the people who live in Canaan about it. Lord, they have already heard a lot about you. They’ve heard that you are with these people. They’ve heard that you have been seen face to face. They’ve been told that your cloud stays over them. They’ve heard that you go in front of them in a pillar of cloud by day. They’ve been told that you go in front of them in a pillar of fire at night. 15Suppose you put all these people to death and leave none alive. Then the nations who have heard these things about you will talk. They’ll say, 16‘The Lord promised to give these people the land of Canaan. But he wasn’t able to bring them into it. So he killed them in the desert.’

17“Now, Lord, show your strength. You have said, 18‘I am the Lord. I am slow to get angry. I am full of love. I forgive those who sin. I forgive those who refuse to obey. But I do not let guilty people go without punishing them. I cause the sin of the parents to affect their children, grandchildren and great-grandchildren.’ 19Lord, your love is great. So forgive the sin of these people. Forgive them just as you have done from the time they left Egypt until now.”

20The Lord replied, “I have forgiven them, just as you asked. 21You can be sure that I live. You can be just as sure that my glory fills the whole earth. 22And here is what you can be just as sure of. Not one of these people will see the land I promised to give them. They have seen my glory. They have seen the signs I did in Egypt. And they have seen what I did in the desert. But they did not obey me. And they have tested me ten times. 23So not even one of them will ever see the land I promised to give to their people of long ago. The person who has not respected me will never see it. 24But my servant Caleb has a different spirit. He follows me with his whole heart. So I will bring him into the land he went to. And his children after him will receive land there. 25The Amalekites and the Canaanites are living in the valleys. So turn back tomorrow. Start out toward the desert. Go along the way that leads to the Red Sea.”

26The Lord said to Moses and Aaron, 27“How long will this evil community speak against me? I have heard these Israelites talk about how unhappy they are. 28So tell them, ‘Here is what I am announcing. I am the Lord. You can be sure that I live. And here is what you can be just as sure of. I will do to you the very thing that I heard you say. 29You will die in this desert. Every one of you 20 years old or more will die. Every one of you who was counted in the list of the people will die. Every one of you who has spoken out against me will be wiped out. 30I lifted up my hand and promised to make this land your home. But now not all of you will enter the land. Caleb, the son of Jephunneh, will enter it. So will Joshua, the son of Nun. They are the only ones who will enter the land. 31You have said that your enemies would capture your children. But I will bring your children in to enjoy the land you have turned your backs on. 32As for you, you will die in the desert. 33Your children will be shepherds here for 40 years. They will suffer because you were not faithful. They will suffer until the last of your bodies lies here in the desert. 34For 40 years you will suffer for your sins. That is one year for each of the 40 days you checked out the land. You will know what it is like to have me against you.’ 35I, the Lord, have spoken. I will surely do these things to this entire evil community of Israel. They have joined together against me. They will meet their end in this desert. They will die here.”

36So the Lord struck down the men Moses had sent to check out the land. They had returned and had spread a bad report about the land. And that had made the whole community speak out against Moses. 37Those men were to blame for spreading the bad report. So the Lord struck them down. They died of a plague. 38Only two of the men who went to check out the land remained alive. One of them was Joshua, the son of Nun. The other was Caleb, the son of Jephunneh.

39Moses reported to all the Israelites what the Lord had said. And they became very sad. 40Early the next morning they set out for the highest point in the hill country. “We have sinned,” they said. “Now we are ready to go up to the land the Lord promised to give us.”

41But Moses said, “Why aren’t you obeying the Lord’s command? You won’t succeed. 42So don’t go up. The Lord isn’t with you. Your enemies will win the battle over you. 43The Amalekites and the Canaanites will meet you on the field of battle. You have turned away from the Lord. So he won’t be with you. And you will be killed by swords.”

44But they wouldn’t listen. They still went up toward the highest point in the hill country. They went up even though Moses didn’t move from the camp. They went even though the ark of the Lord’s covenant didn’t move from the camp. 45Then the Amalekites and the Canaanites who lived in that hill country came down. They attacked the Israelites. They won the battle over them. They chased the Israelites all the way to Hormah.