Numeri 13 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 13:1-33

Kukazonda Kanaani

1Yehova anawuza Mose kuti, 2“Tuma anthu kuti akazonde dziko la Kanaani limene ndikupereka kwa Aisraeli. Kuchokera pa fuko lililonse utume munthu mmodzi amene ndi mtsogoleri wawo.”

3Monga mwa mawu a Yehova, Mose anawatuma kuchokera ku chipululu cha Parani. Onsewo anali atsogoleri a Aisraeli. 4Mayina awo ndi awa:

kuchokera ku fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri;

5kuchokera ku fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori;

6kuchokera ku fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune;

7kuchokera ku fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe;

8kuchokera ku fuko la Efereimu, Hoseya mwana wa Nuni;

9kuchokera ku fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu;

10kuchokera ku fuko la Zebuloni, Gadieli mwana wa Sodi;

11kuchokera ku fuko la Manase (fuko la Yosefe), Gadi mwana wa Susi;

12kuchokera ku fuko la Dani, Amieli mwana wa Gemali;

13kuchokera ku fuko la Aseri, Seturi mwana wa Mikayeli;

14kuchokera ku fuko la Nafutali, Naabi mwana wa Vofisi;

15kuchokera ku fuko la Gadi, Geuweli mwana wa Maki.

16Amenewa ndiwo mayina a anthu amene Mose anawatuma kukazonda dzikolo. (Hoseya mwana wa Nuni, Mose anamupatsa dzina loti Yoswa).

17Mose atawatuma kuti akazonde Kanaani anati, “Mupite kudzera ku Negevi, mukapitirire mpaka ku dziko la mapiri. 18Mukaone dzikolo kuti ndi lotani ndi anthu okhala mʼmenemo ngati ndi amphamvu kapena ofowoka, ochepa kapena ambiri. 19Nanga dziko limene akukhalako ndi lotani? Ndi labwino kapena loyipa? Mizinda imene akukhalamo ndi yotani? Kodi ilibe malinga kapena ndi ya malinga? 20Nthaka yake ndi yotani? Yachonde kapena yopanda chonde? Kodi dzikolo lili ndi mitengo kapena lilibe mitengo? Mukayesetse kubweretsako zipatso za mʼdzikomo.” (Inali nthawi yamphesa zoyamba kupsa).

21Choncho anapita kukazonda dzikolo kuchokera ku chipululu cha Zini mpaka ku Rehobu, mopenyana ndi Lebo Hamati. 22Anapita kudzera ku Negevi ndi kukafika ku Hebroni, kumene Ahimani, Sesai ndi Talimai, ana a Anaki ankakhala. (Anamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri asanamange Zowani ku Igupto). 23Atafika ku chigwa cha Esikolo, anadulako nthambi ya mpesa ya phava limodzi la mphesa ndipo anthu awiri ananyamulizana, natenganso makangadza ndi nkhuyu. 24Malo amenewo anawatcha chigwa cha Esikolo chifukwa cha phava la mphesa limene Aisraeli anadula kumeneko. 25Patapita masiku makumi anayi, anthu aja anabwerako kokazonda dziko lija.

Kufotokoza Zomwe Anakaona

26Ndipo atabwerako anapita kwa Mose ndi Aaroni ndi kwa Aisraeli onse ku Kadesi mʼchipululu cha Parani. Kumeneko anafotokozera anthu onse nawaonetsanso zipatso za mʼdzikolo. 27Anthuwo anafotokozera Mose kuti, “Tinapita ku dziko komwe munatituma. Dzikolo ndi loyenda mkaka ndi uchi ndipo zipatso zake ndi izi. 28Koma anthu amene amakhala mʼdzikomo ndi amphamvu, mizinda yawo ndi ya malinga aakulu kwambiri. Tinaonanso Aanaki kumeneko. 29Aamaleki amakhala ku Negevi, Ahiti, Ayebusi ndi Aamori amakhala mʼdziko la mapiri ndipo Akanaani amakhala pafupi ndi nyanja, mʼmbali mwa Yorodani.”

30Koma Kalebe anawakhalitsa chete anthuwo pamaso pa Mose, ndipo anati, “Tiyeni tipite ndithu ndi kutenga dzikolo, pakuti tingathe kulitenga.”

31Koma anthu aja amene anapita naye anati, “Sitingathe kulimbana ndi anthuwo popeza ndi amphamvu kuposa ifeyo.” 32Choncho anthuwo anafalitsa pakati pa Aisraeli mbiri yoyipa ya dziko lomwe anakalionalo. Iwo anati, “Dziko limene tinapita kukalizonda limawononga anthu okhala mʼmenemo. Ndipo anthu onse amene tinakawaona kumeneko ndi ataliatali. 33Kumeneko tinaona Anefili (ana a Aanaki ochokera kwa Nefili). Ifeyo timangodziona ngati ziwala mʼmaso mwawo, ndipo kwa iwo timaonekadi motero ndithu.”

King James Version

Numbers 13:1-33

1And the LORD spake unto Moses, saying, 2Send thou men, that they may search the land of Canaan, which I give unto the children of Israel: of every tribe of their fathers shall ye send a man, every one a ruler among them. 3And Moses by the commandment of the LORD sent them from the wilderness of Paran: all those men were heads of the children of Israel. 4And these were their names: of the tribe of Reuben, Shammua the son of Zaccur. 5Of the tribe of Simeon, Shaphat the son of Hori. 6Of the tribe of Judah, Caleb the son of Jephunneh. 7Of the tribe of Issachar, Igal the son of Joseph. 8Of the tribe of Ephraim, Oshea the son of Nun.13.8 Oshea: also called, Joshua 9Of the tribe of Benjamin, Palti the son of Raphu. 10Of the tribe of Zebulun, Gaddiel the son of Sodi. 11Of the tribe of Joseph, namely, of the tribe of Manasseh, Gaddi the son of Susi. 12Of the tribe of Dan, Ammiel the son of Gemalli. 13Of the tribe of Asher, Sethur the son of Michael. 14Of the tribe of Naphtali, Nahbi the son of Vophsi. 15Of the tribe of Gad, Geuel the son of Machi. 16These are the names of the men which Moses sent to spy out the land. And Moses called Oshea the son of Nun Jehoshua.13.16 Oshea: also called Joshua13.16 Jehoshua: or, Joshua

17¶ And Moses sent them to spy out the land of Canaan, and said unto them, Get you up this way southward, and go up into the mountain: 18And see the land, what it is; and the people that dwelleth therein, whether they be strong or weak, few or many; 19And what the land is that they dwell in, whether it be good or bad; and what cities they be that they dwell in, whether in tents, or in strong holds; 20And what the land is, whether it be fat or lean, whether there be wood therein, or not. And be ye of good courage, and bring of the fruit of the land. Now the time was the time of the firstripe grapes.

21¶ So they went up, and searched the land from the wilderness of Zin unto Rehob, as men come to Hamath. 22And they ascended by the south, and came unto Hebron; where Ahiman, Sheshai, and Talmai, the children of Anak, were. (Now Hebron was built seven years before Zoan in Egypt.) 23And they came unto the brook of Eshcol, and cut down from thence a branch with one cluster of grapes, and they bare it between two upon a staff; and they brought of the pomegranates, and of the figs.13.23 brook: or, valley 24The place was called the brook Eshcol, because of the cluster of grapes which the children of Israel cut down from thence.13.24 brook: or, valley13.24 Eshcol: that is, A cluster of grapes 25And they returned from searching of the land after forty days.

26¶ And they went and came to Moses, and to Aaron, and to all the congregation of the children of Israel, unto the wilderness of Paran, to Kadesh; and brought back word unto them, and unto all the congregation, and shewed them the fruit of the land. 27And they told him, and said, We came unto the land whither thou sentest us, and surely it floweth with milk and honey; and this is the fruit of it. 28Nevertheless the people be strong that dwell in the land, and the cities are walled, and very great: and moreover we saw the children of Anak there. 29The Amalekites dwell in the land of the south: and the Hittites, and the Jebusites, and the Amorites, dwell in the mountains: and the Canaanites dwell by the sea, and by the coast of Jordan. 30And Caleb stilled the people before Moses, and said, Let us go up at once, and possess it; for we are well able to overcome it. 31But the men that went up with him said, We be not able to go up against the people; for they are stronger than we. 32And they brought up an evil report of the land which they had searched unto the children of Israel, saying, The land, through which we have gone to search it, is a land that eateth up the inhabitants thereof; and all the people that we saw in it are men of a great stature.13.32 men…: Heb. men of statures 33And there we saw the giants, the sons of Anak, which come of the giants: and we were in our own sight as grasshoppers, and so we were in their sight.