Numeri 12 – CCL & KJV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Numeri 12:1-16

Miriamu ndi Aaroni Atsutsana ndi Mose

1Miriamu ndi Aaroni anayamba kuyankhula motsutsana ndi Mose chifukwa cha mkazi wa ku Kusi, popeza Moseyo anakwatira Mkusi. 2Iwowo anafunsa kuti, “Kodi Yehova anayankhula kudzera mwa Mose yekha? Kodi sanayankhule kudzeranso mwa ife?” Ndipo Yehova anamva zimenezi.

3(Koma Mose anali munthu wodzichepetsa kwambiri kuposa munthu aliyense pa dziko lapansi).

4Nthawi yomweyo Yehova anati kwa Mose, Aaroni ndi Miriamu, “Bwerani ku tenti ya msonkhano nonse atatu.” Ndipo atatuwo anapitadi kumeneko. 5Tsono Yehova anatsika mu mtambo, nayima pa khomo la chihema. Kenaka anayitana Aaroni ndi Miriamu. Ndipo onse awiri atapita patsogolo, 6Mulungu anati, “Mverani mawu anga:

“Pakakhala mneneri wa Yehova pakati panu,

ndimadzionetsera kwa iyeyo mʼmasomphenya,

ndimayankhula naye mʼmaloto.

7Koma sinditero ndi Mose mtumiki wanga;

Iyeyu ndi wokhulupirika mʼnyumba yanga yonse.

8Ndimayankhula naye maso ndi maso,

momveka bwino osati mophiphiritsa;

ndipo amaona maonekedwe a Yehova.

Nʼchifukwa chiyani simunaope

kuyankhula motsutsana ndi Mose mtumiki wanga?”

9Ndipo Yehova anawakwiyira, nachoka.

10Pamene mtambo unachoka pamwamba pa Chihema, taonani, Miriamu anagwidwa ndi khate. Aaroni atachewuka anaona Miriamu ali ndi khate; 11ndipo Aaroni anawuza Mose kuti, “Pepani mbuye wanga, musatilange chifukwa cha tchimo limene tachita mopusa. 12Musalole kuti Miriamu akhale ngati mwana wobadwa wakufa kuchoka mʼmimba mwa amayi ake, thupi lake litawonongeka.”

13Tsono Mose anafuwulira Yehova kuti, “Chonde Inu Mulungu, muchiritseni!”

14Yehova anayankha Mose kuti, “Abambo ake akanamulavulira malovu mʼmaso, kodi sakanakhala wonyozeka masiku asanu ndi awiri? Mutsekereni kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri, kenaka mumulowetsenso.” 15Choncho anamutsekera Miriamu kunja kwa msasa masiku asanu ndi awiri ndipo anthu sanayende ulendo wawo mpaka Miriamu atamulowetsanso.

16Pambuyo pake anthu ananyamuka ku Heziroti ndi kukamanga mʼchipululu cha Parani.

King James Version

Numbers 12:1-16

1And Miriam and Aaron spake against Moses because of the Ethiopian woman whom he had married: for he had married an Ethiopian woman.12.1 Ethiopian: or, Cushite12.1 married: Heb. taken 2And they said, Hath the LORD indeed spoken only by Moses? hath he not spoken also by us? And the LORD heard it. 3(Now the man Moses was very meek, above all the men which were upon the face of the earth.)

4And the LORD spake suddenly unto Moses, and unto Aaron, and unto Miriam, Come out ye three unto the tabernacle of the congregation. And they three came out. 5And the LORD came down in the pillar of the cloud, and stood in the door of the tabernacle, and called Aaron and Miriam: and they both came forth. 6And he said, Hear now my words: If there be a prophet among you, I the LORD will make myself known unto him in a vision, and will speak unto him in a dream. 7My servant Moses is not so, who is faithful in all mine house. 8With him will I speak mouth to mouth, even apparently, and not in dark speeches; and the similitude of the LORD shall he behold: wherefore then were ye not afraid to speak against my servant Moses? 9And the anger of the LORD was kindled against them; and he departed.

10And the cloud departed from off the tabernacle; and, behold, Miriam became leprous, white as snow: and Aaron looked upon Miriam, and, behold, she was leprous. 11And Aaron said unto Moses, Alas, my lord, I beseech thee, lay not the sin upon us, wherein we have done foolishly, and wherein we have sinned. 12Let her not be as one dead, of whom the flesh is half consumed when he cometh out of his mother’s womb. 13And Moses cried unto the LORD, saying, Heal her now, O God, I beseech thee.

14¶ And the LORD said unto Moses, If her father had but spit in her face, should she not be ashamed seven days? let her be shut out from the camp seven days, and after that let her be received in again. 15And Miriam was shut out from the camp seven days: and the people journeyed not till Miriam was brought in again. 16And afterward the people removed from Hazeroth, and pitched in the wilderness of Paran.