1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.
Mkwiyo wa Yehova pa Ninive
2Yehova ndi Mulungu wansanje
ndiponso wobwezera;
Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.
Yehova amabwezera adani ake
ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.
3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;
ndipo sadzalola kuti munthu
wolakwa asalangidwe.
Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,
ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.
4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;
amawumitsa mitsinje yonse.
Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma
ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.
5Mapiri amagwedera pamaso pake
ndipo zitunda zimasungunuka.
Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,
dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.
6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?
Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?
Ukali wake ukuyaka ngati moto;
matanthwe akunyeka pamaso pake.
7Yehova ndi wabwino,
ndiye kothawirako nthawi ya masautso.
Amasamalira amene amamudalira,
8koma ndi madzi achigumula choopsa
Iye adzawononga adani ake (Ninive);
adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.
9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova
adzachiwononga kotheratu;
msautso sudzabweranso kachiwiri.
10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga
ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;
adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.
11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,
wofuna kuchitira Yehova chiwembu,
amene amapereka uphungu woyipa.
12Yehova akuti,
“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,
kaya iwowo ndi ambiri,
koma adzawonongedwa ndi kutheratu.
Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,
sindidzakuzunzanso.
13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako
ndipo ndidzadula maunyolo ako.”
14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,
“Sudzakhala ndi zidzukulu
zimene zidzadziwike ndi dzina lako.
Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba
amene ali mʼnyumba ya milungu yako.
Ine ndidzakukumbira manda
chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”
15Taonani, pa phiripo,
mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,
amene akulengeza za mtendere!
Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu
ndipo kwaniritsani malumbiro anu.
Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;
iwo adzawonongedwa kotheratu.
1Profecía acerca de Nínive. Libro de la visión que tuvo Nahúm de Elcós.
Manifestación del Señor
2El Señor es un Dios celoso y vengador.
¡Señor de la venganza, Señor de la ira!
El Señor se venga de sus adversarios;
es implacable con sus enemigos.
3El Señor es lento para la ira,
imponente en su fuerza.
El Señor no deja a nadie sin castigo.
Camina en el huracán y en la tormenta;
las nubes son el polvo de sus pies.
4Increpa al mar y lo seca;
hace que todos los ríos se evaporen.
Los montes Basán y Carmelo pierden su lozanía;
el verdor del Líbano se marchita.
5Ante él tiemblan las montañas
y se desmoronan las colinas.
Ante él se agita la tierra,
el mundo y cuanto en él habita.
6¿Quién podrá enfrentarse a su indignación?
¿Quién resistirá el ardor de su ira?
Su furor se derrama como fuego;
ante él se resquebrajan las rocas.
Destrucción de Nínive
7Bueno es el Señor;
es refugio en el día de la angustia,
y protector de los que en él confían.
8Pero destruirá a Nínive1:8 a Nínive. Lit. el lugar de ella.
con una inundación arrasadora;
¡aun en las tinieblas perseguirá a sus enemigos!
9¿Qué tramáis contra el Señor?
¡Él desbaratará vuestros planes!
¡La calamidad no se repetirá!
10Serán consumidos como paja seca,
como espinos enmarañados,
como borrachos ahogados en vino.
11Tú, Nínive, engendraste
al que trama el mal contra el Señor,
al infame consejero.
Liberación del opresor
12Así dice el Señor:
«Aunque los asirios sean fuertes y numerosos,
serán arrancados y morirán.
Y a ti, Judá, aunque te he afligido,
no volveré a afligirte.
13Voy a quebrar el yugo que te oprime,
voy a romper tus ataduras».
14Pero acerca de ti, Nínive,
el Señor ha decretado:
«No tendrás más hijos que perpetúen tu nombre;
extirparé de la casa de tus dioses
las imágenes talladas y los ídolos fundidos.
Te voy a preparar una tumba,
porque eres una infame».
Anuncio de la victoria sobre Nínive
15¡Mirad! Ya se acerca por los montes
el que anuncia las buenas nuevas de victoria,
el que proclama la paz.
¡Celebra tus peregrinaciones, Judá!
¡Paga tus votos!
Porque no volverán a invadirte los malvados,
pues han sido destruidos por completo.