Habakuku 1 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Habakuku 1:1-17

1Uthenga umene mneneri Habakuku analandira mʼmasomphenya.

Dandawulo la Habakuku

2Kodi inu Yehova, ndidzakhala ndikukupemphani thandizo kwa nthawi yayitali motani,

koma wosayankha?

Kapena kufuwulira kwa inu kuti, “Chiwawa kuno!”

koma wosatipulumutsa?

3Chifukwa chiyani mukundionetsa zinthu zoyipa?

Chifukwa chiyani mukundionetsa mavutowa?

Ndikuona chiwonongeko ndi chiwawa;

pali ndewu ndi kukangana kwambiri.

4Kotero malamulo anu atha mphamvu,

ndipo chilungamo sichikugwira ntchito.

Anthu oyipa aposa olungama,

kotero apotoza chilungamo.

Yankho la Yehova

5“Yangʼanani pakati pa mitundu ya anthu, ndipo penyetsetsani,

ndipo muthedwe nazo nzeru.

Pakuti ndidzachitadi zinthu pa nthawi yanu

zimene inu simudzazikhulupirira,

ngakhale wina atakufotokozerani.

6Pakuti taonani, Ine ndikuwutsa Ababuloni,

anthu ankhanza ndiponso amphamvu,

amene amapita pa dziko lonse lapansi

kukalanda malo amene si awo.

7Iwowa ndi anthu ochititsa mantha, ndipo ndi owopsa;

amadzipangira okha malamulo

ndi kudzipezera okha ulemu.

8Akavalo awo ndi aliwiro kwambiri kupambana akambuku

ndi owopsa kupambana mimbulu yolusa nthawi ya madzulo.

Okwerapo awo akuthamanga molunjika;

a pa akavalo awo ndi ochokera kutali,

akuwuluka ngati chiwombankhanga chofuna kugwira nyama;

9onse akubwera atakonzekera zachiwawa.

Gulu la ankhondo likubwera ngati mphepo ya mʼchipululu

ndi kugwira akapolo ochuluka ngati mchenga.

10Akunyoza mafumu

ndiponso kuchitira chipongwe olamulira.

Akupeputsa mizinda yonse yotetezedwa;

akumanga mitumbira ndi kulanda mizindayo.

11Kenaka amasesa mofulumira ngati mphepo nʼkumangopitirirabe,

anthu ochimwa, amene mphamvu zawo ndiye mulungu wawo.”

Dandawulo Lachiwiri la Habakuku

12Inu Yehova, kodi sindinu wachikhalire?

Mulungu wanga, Woyera wanga, ife sitidzafa.

Inu Yehova, munawasankha anthuwo kuti abweretse chiweruzo;

Inu Thanthwe, munawayika iwowo kuti atilange.

13Maso anu ndi oyera kwambiri safuna kuona choyipa;

Inu simulekerera cholakwa.

Chifukwa chiyani nanga mukulekerera anthu ochita zachinyengowa?

Chifukwa chiyani muli chete pamene anthu oyipa

akuwononga anthu olungama kupambana iwowo?

14Mwasandutsa anthu kukhala ngati nsomba zamʼnyanja,

ngati zolengedwa zamʼnyanja zimene zilibe wolamulira.

15Mdani wawo woyipa amakoka anthu onse ndi mbedza,

amawakola mu ukonde wake,

amawasonkhanitsa mu khoka lake;

kotero iyeyo amakondwa ndi kusangalala.

16Choncho iye amaperekera nsembe ukonde wake

ndiponso kufukizira lubani khoka lake,

popeza ukonde wakewo ndiye umamubweretsera moyo wapamwamba

ndipo amadya chakudya chabwino kwambiri.

17Kodi iye azipitirabe kugwiritsa ntchito makoka akewo,

kuwononga mitundu ya anthu mopanda chifundo?

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Habacuc 1:1-17

1Esta es la profecía que el profeta Habacuc recibió en visión.

La primera queja de Habacuc

2¿Hasta cuándo, Señor, he de pedirte ayuda

sin que tú me escuches?

¿Hasta cuándo he de quejarme de la violencia

sin que tú nos salves?

3¿Por qué me haces presenciar calamidades?

¿Por qué debo contemplar el sufrimiento?

Veo ante mis ojos destrucción y violencia;

surgen riñas y abundan las contiendas.

4Por lo tanto, se entorpece la ley

y no se da curso a la justicia.

El impío acosa al justo,

y las sentencias que se dictan son injustas.

La respuesta del Señor

5«¡Mirad a las naciones!

¡Contempladlas y quedaos asombrados!

Voy a hacer en estos días cosas tan sorprendentes

que no las creeréis aunque alguien os las explique.

6Estoy incitando a los caldeos,

ese pueblo despiadado e impetuoso,

que recorre toda la tierra

para apoderarse de territorios ajenos.

7Son un pueblo temible y espantoso,

que impone su propia justicia y grandeza.

8Sus caballos son más veloces que leopardos,

más feroces que lobos nocturnos.

Su caballería se lanza a todo galope;

sus jinetes vienen de muy lejos.

¡Caen como buitres sobre su presa!

9Vienen en son de violencia;

avanzan sus hordas1:9 hordas. Palabra de difícil traducción. como el viento del desierto,

hacen prisioneros como quien recoge arena.

10Ridiculizan a los reyes,

se burlan de los gobernantes;

se ríen de toda ciudad amurallada,

pues construyen terraplenes y la toman.

11Son un viento que a su paso arrasa todo;

su pecado es hacer de su fuerza un dios».

La segunda queja de Habacuc

12¡Tú, Señor, existes desde la eternidad!

¡Tú, mi santo Dios, eres inmortal!1:12 eres inmortal (lit. no morirás; según una tradición rabínica); no moriremos (TM).

Tú, Señor, los has puesto para hacer justicia;

tú, mi Roca, los has puesto para ejecutar tu castigo.

13Son tan puros tus ojos que no puedes ver el mal;

no te es posible contemplar el sufrimiento.

¿Por qué entonces toleras a los traidores?

¿Por qué guardas silencio

mientras los impíos se tragan a los justos?

14Has hecho a los hombres como peces del mar,

como reptiles que no tienen jefe.

15Babilonia los saca a todos con anzuelo,

los arrastra con sus redes,

los recoge entre sus mallas,

y así se alegra y regocija.

16Por lo tanto, ofrece sacrificios a sus redes

y quema incienso a sus mallas,

pues gracias a sus redes su porción es sabrosa

y su comida es suculenta.

17¿Continuará vaciando sus redes

y matando sin piedad a las naciones?