Zefaniya 1 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Zefaniya 1:1-18

1Yehova anayankhula ndi Zefaniya mwana wa Kusi, mwana wa Gedaliya, mwana wa Amariya, mwana wa Hezekiya pa nthawi ya Yosiya, mwana wa Amoni, mfumu ya Yuda.

Yehova Adzaweruza Dziko Lapansi

2“Ndidzawononga kotheratu zinthu zonse

pa dziko lapansi,”

akutero Yehova.

3“Ndidzawononga anthu pamodzi ndi nyama zomwe;

ndidzawononga mbalame zamlengalenga

ndi nsomba za mʼnyanja.

Ndidzawononga anthu oyipa,

ndipo ndidzafafaniza mtundu wa anthu pa dziko lonse lapansi,”

akutero Yehova.

Chenjezo kwa Yuda

4Ndidzatambasula dzanja langa pa Yuda

ndi onse okhala mu Yerusalemu.

Ndidzawononga pamalo pano otsalira opembedza Baala,

mayina a anthu osapembedza pamodzi ndi ansembe a mafano:

5amene amagwada pa madenga a nyumba zawo

kupembedza zolengedwa zamumlengalenga,

amene amagwada ndi kulumbira mʼdzina la Yehova,

komanso mʼdzina la Moleki,

6amene abwerera mʼmbuyo osatsata Yehova,

osafunafuna kapena kupempha nzeru kwa Yehova.

7Khalani chete pamaso pa Ambuye Yehova,

chifukwa tsiku la Yehova layandikira.

Yehova wakonzekera kupereka nsembe;

wapatula iwo amene wawayitana.

8Pa tsiku la nsembe ya Yehova

ndidzalanga akalonga

ndi ana aamuna a mfumu

ndi onse amene amavala

zovala zachilendo.

9Pa tsiku limenelo ndidzalanga

onse amene safuna kuponda pa chiwundo,

amene amadzaza nyumba ya ambuye awo

ndi chiwawa ndi chinyengo.

10“Pa tsiku limenelo,” akutero Yehova,

“Kufuwula kwakukulu kudzamveka pa Chipata cha Nsomba,

kulira kwa chisoni kuchokera mʼChigawo Chatsopano,

ndi phokoso la kugumuka kochokera ku mapiri.

11Lirani mwachisoni, inu amene mumakhala kumene kuli msika;

a malonda anu onse adzapululidwa,

ndiponso onse amene ali ndi siliva adzawonongedwa.

12Pa nthawi imeneyo ndidzafufuzafufuza mu Yerusalemu ndi nyale

ndi kulanga onse amene sakulabadira,

amene ali ngati vinyo wosakhutchumulidwa,

amene amaganiza kuti, ‘Yehova sadzachita chilichonse,

chabwino kaya choyipa.’

13Chuma chawo chidzafunkhidwa,

nyumba zawo zidzagwetsedwa.

Adzamanga nyumba,

koma osakhalamo;

adzadzala minda ya mpesa

koma sadzamwako vinyo wake.”

Tsiku Lalikulu la Yehova

14Tsiku lalikulu la Yehova layandikira,

layandikira ndipo lifika msanga.

Tamverani! Kulira kwa pa tsiku la Yehova kudzakhala kowawa,

ngakhale munthu wolimba mtima adzalira kwambiri.

15Tsiku limenelo lidzakhala la ukali,

tsiku losautsa ndi lomvetsa chisoni,

tsiku la mavuto ndi la chiwonongeko,

tsiku la mdima ndi lachisoni,

tsiku la mitambo ndi la mdima wandiweyani.

16Tsiku loliza lipenga ndi la mfuwu wankhondo,

tsiku la kugwa kwa mizinda yotetezedwa

ndi nsanja za pa ngodya.

17Ndidzabweretsa msautso pa anthu

ndipo adzayenda ngati anthu osaona,

chifukwa achimwira Yehova,

magazi awo adzamwazika ngati fumbi

ndi mnofu wawo ngati ndowe.

18Ngakhale siliva wawo kapena golide wawo

sadzatha kuwapulumutsa

pa tsiku la ukali wa Yehova.

Dziko lonse lapansi lidzanyeka

mʼmoto wa nsanje yake

chifukwa adzakantha modzidzimutsa

onse okhala pa dziko lapansi.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Sofonías 1:1-18

1Esta es la palabra del Señor, que vino a Sofonías hijo de Cusí, hijo de Guedalías, hijo de Amarías, hijo de Ezequías, durante el reinado de Josías hijo de Amón, rey de Judá:

Advertencia sobre la destrucción venidera

2«Arrasaré por completo

cuanto hay sobre la faz de la tierra

—afirma el Señor—.

3Arrasaré con hombres y animales,

con las aves del cielo,

con los peces del mar,

con ídolos e impíos por igual.1:3 con ídolos e impíos por igual. Texto de difícil traducción.

»Exterminaré al hombre

de sobre la faz de la tierra

—afirma el Señor—.

Juicio contra Judá

4»Extenderé mi mano contra Judá

y contra todos los habitantes de Jerusalén.

Exterminaré de este lugar todo rastro de Baal,

y hasta el nombre de sus sacerdotes;1:4 de sus sacerdotes (LXX); de los sacerdotes paganos con los sacerdotes (TM).

5a los que en las azoteas se postran en adoración

ante las estrellas del cielo,

a los que, postrados en adoración,

juran lealtad al Señor,

y al mismo tiempo a Moloc,1:5 Moloc. Lit. Malcán; es decir, Milcón.

6a los que se apartan del Señor,

y no lo buscan ni lo consultan.

7¡Silencio ante el Señor omnipotente,

porque cercano está el día del Señor;

ha preparado el Señor un sacrificio

y ha purificado a sus invitados!

8En el día del sacrificio del Señor

castigaré a los funcionarios y oficiales del rey,

y a cuantos se visten según modas extrañas.

9En aquel día castigaré

a cuantos evitan pisar el umbral,1:9 evitan pisar el umbral. Alusión a una práctica supersticiosa; véase 1S 5:5.

a los que llenan de violencia y engaño

la casa de sus dioses.1:9 la casa de sus dioses. Alt. el palacio de su señor.

10»Aquel día se oirán gritos de auxilio,

desde la puerta del Pescado,

gemidos desde el Barrio Nuevo,

y gran quebranto desde las colinas

—afirma el Señor—.

11»¡Gemid, habitantes del Barrio del Mercado!1:11 Mercado. Alt. Mortero.

Aniquilados serán todos los mercaderes,

exterminados cuantos comercian con plata.

12En aquel tiempo registraré Jerusalén con lámparas

para castigar a los que reposan tranquilos

como vino en su sedimento,

a los que piensan: “El Señor no va a hacer nada,

ni para bien ni para mal”.

13En botín se convertirán sus riquezas,

sus casas, en desolación:

“Edificarán casas,

pero no las habitarán;

plantarán viñas,

pero del vino no beberán”.

El gran día del Señor

14»Ya se acerca el gran día del Señor;

a toda prisa se acerca.

El estruendo del día del Señor será amargo,

y aun el más valiente gritará.

15Día de ira será aquel día,

día de acoso y angustia,

día de devastación y ruina,

día de tinieblas y penumbra,

día de niebla y densos nubarrones,

16día de trompeta y grito de batalla

contra las ciudades fortificadas,

contra los altos bastiones.

17De tal manera acosaré a los hombres

que andarán como ciegos,

porque pecaron contra el Señor.

Su sangre será derramada como polvo

y sus entrañas, como estiércol.

18No los podrán librar

ni su plata ni su oro

en el día de la ira del Señor.

En el fuego de su celo

será toda la tierra consumida;

en un instante reducirá a la nada

a todos los habitantes de la tierra».