Nahumu 1 – CCL & CCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nahumu 1:1-15

1Uthenga wonena za Ninive. Buku la masomphenya a Nahumu wa ku Elikosi.

Mkwiyo wa Yehova pa Ninive

2Yehova ndi Mulungu wansanje

ndiponso wobwezera;

Yehova amabwezera ndipo ndi waukali.

Yehova amabwezera adani ake

ndipo ukali wake umakhala nthawi zonse pa adani akewo.

3Yehova sakwiya msanga koma ndi wa mphamvu yayikulu;

ndipo sadzalola kuti munthu

wolakwa asalangidwe.

Iye amayenda mʼkamvuluvulu ndi mʼnamondwe,

ndipo mitambo ndi fumbi la ku mapazi ake.

4Amalamulira nyanja ndipo imawuma;

amawumitsa mitsinje yonse.

Zomera za ku Basani ndi Karimeli zimawuma

ndipo maluwa a ku Lebanoni amafota.

5Mapiri amagwedera pamaso pake

ndipo zitunda zimasungunuka.

Dziko lapansi limanjenjemera pamaso pake,

dziko lonse ndi zonse zokhala mʼmenemo.

6Ndani angathe kuyima pamaso pake Iye akalusa?

Ndani angapirire mkwiyo wake woopsa?

Ukali wake ukuyaka ngati moto;

matanthwe akunyeka pamaso pake.

7Yehova ndi wabwino,

ndiye kothawirako nthawi ya masautso.

Amasamalira amene amamudalira,

8koma ndi madzi achigumula choopsa

Iye adzawononga adani ake (Ninive);

adzapirikitsira adani ake ku malo a mdima.

9Chiwembu chilichonse chimene akukonzekera kumuchitira Yehova

adzachiwononga kotheratu;

msautso sudzabweranso kachiwiri.

10Iwo adzakodwa mu ziyangoyango za minga

ndipo adzaledzera ndi vinyo wawo;

adzatenthedwa ngati ziputu zowuma.

11Kwa iwe, Ninive, kunachokera munthu wa cholinga choyipa,

wofuna kuchitira Yehova chiwembu,

amene amapereka uphungu woyipa.

12Yehova akuti,

“Ngakhale Asiriyawo ali ndi abwenzi,

kaya iwowo ndi ambiri,

koma adzawonongedwa ndi kutheratu.

Ngakhale ndinakuzunza iwe Yuda,

sindidzakuzunzanso.

13Tsopano ndidzathyola goli lake pa khosi lako

ndipo ndidzadula maunyolo ako.”

14Yehova walamulira za iwe, Ninive kuti,

“Sudzakhala ndi zidzukulu

zimene zidzadziwike ndi dzina lako.

Ndidzawononga zifanizo zosema ndi mafano owumba

amene ali mʼnyumba ya milungu yako.

Ine ndidzakukumbira manda

chifukwa ndiwe woyipitsitsa.”

15Taonani, pa phiripo,

mapazi a munthu amene akubweretsa nkhani yabwino,

amene akulengeza za mtendere!

Inu anthu a ku Yuda, chitani madyerero anu

ndipo kwaniritsani malumbiro anu.

Anthu oyipa sadzakuthiraninso nkhondo;

iwo adzawonongedwa kotheratu.

Chinese Contemporary Bible (Simplified)

那鸿书 1:1-15

1以下是关于尼尼微的预言,是伊勒歌斯那鸿的启示书。

耶和华向尼尼微发怒

2耶和华是痛恨不贞、施行报应的上帝。

耶和华施行报应,充满烈怒。

耶和华报应祂的仇敌,向他们发烈怒。

3耶和华不轻易发怒,有伟大的能力。

耶和华断不以有罪的为无罪。

祂行走在旋风和暴风中,

云彩是祂脚下的尘土。

4祂斥责大海,使大海干涸;

祂使一切河流枯竭。

巴珊迦密的草木凋零,

黎巴嫩的鲜花衰残。

5在祂面前,群山震动,丘陵消融。

在祂面前,大地隆起,

世界和世上的一切都战栗。

6祂发怒,谁能站立?

祂发烈怒,谁能承受?

祂的愤怒如火焰喷涌而出,

磐石在祂面前崩裂。

7耶和华是良善的,

是人患难时的避难所;

祂看顾那些信靠祂的人。

8祂必用滔滔洪水灭绝祂的敌人,

把他们驱逐到黑暗中。

9尼尼微人啊,

你们为何图谋抵挡耶和华?

祂要彻底毁灭你们,

无需击打两次。

10你们像纠结的荆棘,

又像酩酊大醉的人,

要如干秸被火烧尽。

11你们当中有一个人,

一个邪恶的阴谋者,

图谋抵挡耶和华。

12耶和华说:

“尽管尼尼微势力强大、人口众多,

但必被铲除,化为乌有。

我的子民啊,我使你们受了苦,

但必不再使你们受苦。

13现在我要打碎他们套在你们颈项上的轭,

松开你们身上的锁链。”

14尼尼微啊,

耶和华已发出有关你的命令:

“你的名不会传于后世。

我要摧毁你神庙中雕刻和铸造的偶像。

我要为你掘好坟墓,

因为你毫无用处。”

15看啊,

传喜讯、报平安的人穿山越岭而来。

犹大啊,

庆祝你的节期,

还你许的愿吧!

邪恶之人将不再侵扰你,

他们都将被彻底毁灭。