Mlaliki 2 – CCL & BPH

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 2:1-26

Zosangalatsa Nʼzopandapake

1Ine ndinaganiza mu mtima mwanga, “Tsopano ndiyese zosangalatsa kuti ndipeze zomwe ndi zabwino.” Koma izi zinaonekanso kuti ndi zopandapake. 2“Kuseka,” ndinati, “imeneyo ndi misala. Ndipo kodi chisangalalo chimabweretsa phindu lanji?” 3Ndinayesa kudzisangalatsa ndi vinyo, koma umenewu unali uchitsiru, pamenepo nʼkuti maganizo anga akutsogozedwa ndi nzeru. Ine ndinkati mwina kapena njira yotero nʼkukhala yopambana, imene anthu amatsata pofuna kusangalala pa masiku owerengeka a moyo wawo.

4Ndinagwira ntchito zikuluzikulu: Ndinadzimangira nyumba ndi kuwoka mipesa. 5Ndinalima madimba ndi minda yamitengo; ndipo ndinadzalamo mitengo ya zipatso za mitundu yonse. 6Ndinakumba mayiwe osungiramo madzi woti ndizithirira minda ya mitengo yodzalidwa ija. 7Ndinagula akapolo aamuna ndi akapolo aakazi, ndiponso ndinali ndi akapolo ena omwe anabadwira mʼnyumba mwanga. Ndinalinso ndi ngʼombe ndi nkhosa zambiri kupambana aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. 8Ndinadzikundikira siliva ndi golide, ndiponso chuma chochokera kwa mafumu ndi madera awo. Ndinali ndi amuna ndi akazi oyimba ndiponso azikazi; zinthu zokondweretsa mtima wa munthu. 9Ndinali munthu wotchuka kupambana wina aliyense mu Yerusalemu amene analipo ndisanabadwe. Mu zonsezi nzeru zanga zinali nane.

10Sindinadzimane chilichonse chimene maso anga anachifuna;

mtima wanga sindinawumane zokondweretsa.

Mtima wanga unakondwera ndi ntchito yanga yonse,

ndipo iyi ndiyo inali mphotho ya ntchito zanga zonse zolemetsa.

11Koma pamene ndinayamba kuyangʼanayangʼana zonse zimene ndinachita ndi manja anga,

ndi zimene ndinazivutikira kuti ndizipeze,

zonsezi zinali zopandapake; kungodzivuta chabe,

palibe chomwe ndinapindula pansi pano.

Nzeru ndi Uchitsiru Nʼzopandapake

12Kenaka maganizo anga anayamba kulingalira zakuti nzeru nʼchiyani,

komanso kuti misala ndi uchitsiru nʼchiyani.

Kodi munthu wodzalowa ufumu tsopanoyo angachite chiyani

choposa chimene chinachitidwa kale?

13Ndinaona kuti nzeru ndi yopambana uchitsiru,

monga momwe kuwala kumapambanira mdima.

14Munthu wanzeru amayenda maso ali patsogolo,

pamene chitsiru chimayenda mʼchimbulimbuli;

koma ndinazindikira kuti chomwe

chimawachitikira onsewo ndi chimodzi.

15Pamenepo ndinalingalira mu mtima mwanga,

“Zochitikira chitsiru zidzandichitikiranso ine.

Nanga tsono phindu langa nʼchiyani pakukhala wanzeru?”

Ndinati mu mtima mwanga,

“Ichinso ndi chopandapake.”

16Pakuti munthu wanzeru, pamodzinso ndi chitsiru sadzakumbukiridwa nthawi yayitali;

mʼmasiku amʼtsogolo awiriwo adzayiwalika.

Mmene chimafera chitsiru ndi mmenenso amafera wanzeru!

Kugwira Ntchito Nʼkopandapake

17Kotero ndinadana nawo moyo chifukwa ntchito zimene zimagwiridwa pansi pano ndi zosautsa kwa ine. Ntchito zonsezo ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe. 18Ine ndinadana nazo ntchito zonse zimene ndinazigwira pansi pano, chifukwa ndinayenera kudzazisiyira wina amene adzalowa mʼmalo mwanga. 19Ndipo ndani amadziwa kuti munthu ameneyo adzakhala wanzeru kapena chitsiru? Komabe munthuyo adzakhala wolamulira zonse zimene ndinazichita pansi pano mwa nzeru zanga. Izinso ndi zopandapake. 20Motero ndinayamba kutaya mtima chifukwa cha ntchito zonse zimene ndinazivutikira pansi pano. 21Pakuti munthu atha kugwira ntchito yake mwanzeru, chidziwitso ndi luntha, ndipo kenaka nʼkusiyira wina amene sanakhetserepo thukuta. Izinso ndi zopandapake ndiponso tsoka lalikulu. 22Kodi munthu amapindulanji pa ntchito zonse zolemetsa ndi zodetsa nkhawa zimene amazichita pansi pano? 23Masiku ake onse amakhala achisoni, ntchito yake imakhala yovuta; ngakhale usiku womwe, mtima wake supumula. Izinso ndi zopandapake.

24Kwa munthu palibe chabwino china kuposa kudya, kumwa ndi kukondwerera ntchito zake. Izinso ndaona kuti ndi zochokera kwa Mulungu, 25pakuti popanda Iye, ndani angadye ndi kupeza chisangalalo? 26Munthu amene amakondweretsa Mulungu, Mulunguyo amamusandutsa wanzeru, wozindikira ndi wachisangalalo, koma wochimwa, Mulungu amamupatsa ntchito yosonkhanitsa ndi kusunga chuma kuti adzachipereke kwa amene Mulunguyo amakondwera naye. Izinso ndi zopandapake, nʼkungodzivuta chabe.

Bibelen på hverdagsdansk

Prædikerens Bog 2:1-26

Findes livets mening i rigdom og forlystelser?

1Jeg sagde til mig selv: „Lad mig prøve livets goder. Nu vil jeg have det sjovt og nyde livet.” Men også det var meningsløst. 2Det er tåbeligt at le hele tiden. Hvad opnår man ved at more sig dag ud og dag ind? 3Jeg forsøgte at komme i godt humør ved at drikke vin og slå mig løs, imens jeg tænkte over, hvordan man bedst kan bruge sit korte liv her på jorden.

4Jeg lagde store planer og førte dem ud i livet: Jeg byggede huse og plantede vingårde, 5anlagde haver og parker med alle mulige frugttræer, 6gravede damme med vand til mine plantager. 7Jeg købte mandlige og kvindelige slaver ud over dem, der blev født i min husstand. Jeg ejede flere kvægflokke og fåreflokke end nogen anden i Jerusalem før mig. 8Jeg samlede guld og sølv og købte sjældne kostbarheder fra andre konger og lande. Jeg havde sangere og sangerinder og hengav mig til sanselig nydelse med et stort harem. 9Således overgik jeg alle tidligere konger i Jerusalem både i visdom og store bedrifter.

10Alt, hvad jeg fik øje på, købte jeg. Jeg nægtede ikke mig selv nogen fornøjelse, men glædede mig over alt, hvad jeg fik udrettet. Det var lønnen for mit store slid. 11Men da jeg tænkte nærmere over det, jeg havde opnået, syntes det mig alligevel helt omsonst. I virkeligheden havde jeg ikke gjort noget af værdi.

Er livets mening at få visdom?

12Derfor gav jeg mig til at sammenligne visdom med tåbelighed. Hvad ellers skulle jeg finde på? 13Jeg indså, at visdom er at foretrække frem for tåbelighed, ligesom lys er at foretrække frem for mørke. 14Den vise tænker over hvilke konsekvenser, hans handlinger får for fremtiden, mens tåben famler rundt i mørke. Men jeg indså også, at den samme skæbne rammer os alle. 15Så tænkte jeg: „Når både tåben og jeg lider samme skæbne, hvad gavner så al min visdom? Så er selv det at søge visdom jo meningsløst!” 16Både den vise og tåben skal dø, og ingen af dem huskes for evigt, for med tiden bliver alting glemt. 17Da blev jeg led ved livet, for uanset hvad vi foretager os, er det alt sammen meningsløst.

Ligger livets mening i at få succes?

18Jeg blev frustreret over mit slid og slæb, for alt det, jeg har bygget op, må jeg jo overlade til min efterfølger. 19Og hvem ved, om det bliver en vismand eller en tåbe? Alligevel er jeg tvunget til at overlade resultatet af alle mine anstrengelser i hans hænder. Hvor meningsløst!

20Det ærgrede mig at tænke på alt det arbejde, jeg havde udført. 21Man har slidt og slæbt for at realisere sine planer med visdom, kundskab og dygtighed kun for at overlade sit livsværk til en anden, som ikke har rørt en finger. Det er jo meningsløst og direkte uretfærdigt! 22Hvad får man ud af alle de anstrengelser og bekymringer, man gør sig her i livet? 23Kun lidelser og skuffelser. Selv om natten finder tankerne ingen hvile. Hvor meningsløst!

Livet som en gave

24Det bedste, man kan gøre, er derfor at spise og drikke og glæde sig over sit arbejde. Jeg indså, at denne glæde egentlig er en gave fra Gud. 25For hvem kan spise eller glæde sig uden at være taknemmelig til Gud? 26Han giver jo visdom, kundskab og glæde til dem, der ønsker at gøre hans vilje. Men syndere giver han det slidsomme arbejde at samle rigdom for derefter at give det til dem, der gør hans vilje. Altså er synderes slid meningsløst.