Mlaliki 10 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mlaliki 10:1-20

1Monga ntchentche zakufa zimayika fungo loyipa mʼmafuta onunkhira,

choncho kupusa pangʼono kumawononganso nzeru ndi ulemu.

2Mtima wa munthu wanzeru umamutsogolera bwino,

koma mtima wa munthu wopusa umamusocheretsa.

3Chitsiru ngakhale chikamayenda mu msewu,

zochita zake ndi zopanda nzeru

ndipo chimaonetsa aliyense kuti icho ndi chitsirudi.

4Ngati wolamulira akukwiyira,

usachoke pa ntchito yako;

kufatsa kumakonza zolakwa zazikulu.

5Pali choyipa chimene ndinachiona pansi pano,

kulakwitsa kumene kumachokera kwa wolamulira:

6Zitsiru amazipatsa ntchito zambiri zapamwamba,

pamene anthu olemera amawapatsa ntchito zotsika.

7Ndaona akapolo atakwera pa akavalo,

pamene akalonga akuyenda pansi ngati akapolo.

8Amene amakumba dzenje adzagwamo yekha;

amene amabowola khoma adzalumidwa ndi njoka.

9Amene amaphwanya miyala adzapwetekedwa ndi miyalayo;

amene amawaza nkhuni adzapwetekedwa nazo.

10Ngati nkhwangwa ili yobuntha

yosanoledwa,

pamafunika mphamvu zambiri potema,

koma luso limabweretsa chipambano.

11Nʼkopanda phindu kudziwa kuseweretsa njoka

ngati njokayo yakuluma kale.

12Mawu a pakamwa pa munthu wanzeru ndi okondweretsa,

koma chitsiru chidzawonongedwa ndi milomo yake yomwe.

13Chitsiru chimayamba ndi mawu opusa;

potsiriza pake zoyankhula zake ndi zamisala

14ndipo chitsiru chimachulukitsa mawu.

Palibe amene amadziwa zimene zikubwera mʼtsogolo,

ndani angamuwuze zomwe zidzachitika iye akadzafa?

15Chitsiru chimatopa msanga ndi ntchito yochepa;

ndipo sichikhala ndi mphamvu zobwererera ku mudzi.

16Tsoka kwa iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ikali mwana,

ndipo atsogoleri ako amakhala pa madyerero mmamawa.

17Wodala iwe, iwe dziko ngati mfumu yako ndi mwana wolemekezeka

ndipo atsogoleri ako amadya pa nthawi yake,

kuti apeze mphamvu osati kuti aledzere.

18Ngati munthu ndi waulesi, denga lake limaloshoka;

ngati manja ake ndi alobodo nyumba yake imadontha.

19Phwando ndi lokondweretsa anthu,

ndipo vinyo ndi wosangalatsa moyo,

koma ndalama ndi yankho la chilichonse.

20Usanyoze mfumu ngakhale mu mtima mwako,

kapena kutukwana munthu wachuma mʼchipinda chako,

pakuti mbalame yamlengalenga itha kutenga mawu ako

nʼkukafotokoza zomwe wanena.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Eclesiastés 10:1-20

Dichos de sabiduría

1Las moscas muertas apestan

y echan a perder el perfume.

Así mismo pesa más una pequeña necedad

que la sabiduría y la honra juntas.

2El corazón del sabio busca el bien,

pero el del necio busca el mal.

3Y aun en el camino por el que va, el necio revela su falta de inteligencia y a todos va diciendo lo necio que es.

4Si el ánimo del gobernante se exalta contra ti, no abandones tu puesto. La paciencia es el remedio para los grandes errores.

5Hay un mal que he visto en esta vida, semejante al error que cometen los gobernantes: 6al necio se le dan muchos puestos elevados, pero a los capaces se les dan los puestos más bajos. 7He visto esclavos montar a caballo, y príncipes andar a pie como esclavos.

8El que cava la fosa,

en ella se cae.

Al que abre brecha en el muro,

la serpiente lo muerde.

9El que pica piedra,

con las piedras se hiere.

El que corta leña,

con los leños se lastima.

10Si el hacha pierde su filo,

y no se vuelve a afilar,

hay que golpear con más fuerza.

El éxito radica en la acción

sabia y bien ejecutada.

11Si la serpiente muerde antes de ser encantada,

no hay ganancia para el encantador.

12Las palabras del sabio son placenteras,

pero los labios del necio son su ruina;

13sus primeras palabras son necedades,

y las últimas son terribles sandeces.

14¡Pero no le faltan las palabras!

Nadie sabe lo que ha de suceder,

y lo que será aun después,

¿quién podría decirlo?

15El trabajo del necio tanto lo fatiga

que ni el camino a la ciudad conoce.

16¡Ay del país cuyo rey es un inmaduro,

y cuyos príncipes banquetean desde temprano!

17¡Dichoso el país cuyo rey es un noble,

y cuyos príncipes comen cuando es debido,

para reponerse y no para embriagarse!

18Por causa del ocio se viene abajo el techo,

y por la pereza se desploma la casa.

19Para alegrarse, el pan;

para gozar, el vino;

para disfrutarlo, el dinero.

20No maldigas al rey ni con el pensamiento,

ni en privado maldigas al rico,

pues las aves del cielo pueden correr la voz.

Tienen alas y pueden divulgarlo.