Miyambo 8 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 8:1-36

Nzeru Ikuyitana

1Kodi nzeru sikuyitana?

Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?

2Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira,

imayima pa mphambano ya misewu.

3Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda,

pa makomo olowera imafuwula kuti,

4Inu anthu, ndikuyitana inu;

ndikuyitanatu anthu onse.

5Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera;

inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.

6Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri;

ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.

7Pakamwa panga pamayankhula zoona

ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.

8Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama;

mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.

9Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona;

kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.

10Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva,

nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.

11Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali,

ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.

12Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera.

Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.

13Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa.

Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama,

kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.

14Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino;

ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.

15Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira.

Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.

16Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula.

Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.

17Ndimakonda amene amandikonda,

ndipo amene amandifunafuna amandipeza.

18Ine ndili ndi chuma ndi ulemu,

chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.

19Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala;

zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.

20Ndimachita zinthu zolungama.

Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.

21Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda

ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.

22“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba.

Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.

23Ndinapangidwa kalekalelo,

pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.

24Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi,

zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.

25Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo,

mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,

26lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake;

lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.

27Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga,

pamene ankalemba malire a nyanja yozama,

28pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga

ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,

29pamene anayikira nyanja malire

kuti madzi asadutse malirewo,

ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.

30Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri;

ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku,

kusangalala nthawi zonse pamaso pake.

31Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse

ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”

32“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni;

odala anthu amene amasunga njira zanga.

33Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru;

musanyozere mawu anga.

34Wodala munthu amene amandimvera,

amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku,

kudikirira pa chitseko changa.

35Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo

ndipo Yehova amamukomera mtima.

36Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha;

onse amene amandida amakonda imfa.”

New Serbian Translation

Приче Соломонове 8:1-36

Мудрост позива

1Зар то мудрост не позива,

не диже ли разборитост глас свој?

2Ено је на узвишицама, покрај пута,

на раскршћима се поставила;

3на капијама, на улазима у град,

на улазним вратима она виче:

4„Људи, вас дозивам

и глас дижем целом човечанству!

5Разборитости се научите, лаковерни људи,

уразумите срце, неразумни.

6Слушајте, јер ја објављујем драгоцене ствари,

честите ће бити изреке усана мојих.

7Баш истину казиваћу

јер је злоба мрска уснама мојим.

8Праведне су све речи мојих уста

и нема у њима изопачености и непоштења.

9Све су оне јасне разборитом

и исправне онима што знање стичу.

10Прихватите поуку моју, а не сребро,

изаберите знање пре него суво злато.

11Јер је мудрост од драгуља боља

и сва јој уживања ни принети нису.

12Ја, мудрост, с разборитошћу живим,

проналазим знање и домишљатост.

13Богобојазност значи мрзети зло,

јер ја мрзим бахати понос,

пут злобе и уста покварена.

14У мени је савет, поуздана мудрост.

У мени је умност, ја имам снагу.

15Цареви владају уз моју помоћ

и владари деле правду.

16Главари, кнезови и све праведне судије

владају уз моју помоћ.

17Ја волим све који воле мене,

налазе ме сви који ме помно траже.

18Част, иметак, трајно благостање

и праведност су са мном.

19Од злата, од сувога злата је род мој бољи,

и добит моја боља од пробраног сребра.

20Ја ходам путем праведности

и посред стаза правде,

21да онима који ме воле дам наследство

и њихове ризнице напуним.

22Мене је имао Господ на почетку његовог пута,

још пре дела својих древних.

23Постављена сам од давнина,

од искона, пре постања земље.

24Рођена сам кад бездана још није било,

када није било ни извора обилних вода.

25Пре планина постављених

и пре брда рођена сам,

26док још земљу он створио није,

ни поља, ни прво тло света.

27Када је створио небеса, ја сам била тамо,

када је оцртавао хоризонт над лицем бездана;

28када је горе учвршћивао облаке

и када су набујали извори бездана;

29када је мору поставио његове обале,

како вода не би прелазила његову заповест,

и када је означио темеље земљине.

30Била сам уз њега као градитељка,

била сам му радост свакодневна,

веселила се пред њим стално;

31веселила се по свету, по његовој земљи

и радовала се са потомцима људи.

32Зато ме, децо, послушајте.

О, како су благословени они који се држе мојих путева!

33Послушајте поуку моју,

радите мудро и не одбацујте је.

34Како је благословен човек који ме слуша,

који свакодневно бдије на мојим вратима

и пази на доврацима врата мојих!

35Јер ко мене нађе, нашао је живот

и добио наклоност Господњу.

36Али ко мене не нађе, себи самом шкоди,

а сви који ме мрзе воле смрт.“