Miyambo 6 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 6:1-35

Za Moyo wa Uchitsiru

1Mwana wanga, ngati wamuperekera mnansi wako chikole,

ngati walonjeza kumulipirira mlendo,

2ngati wagwidwa ndi zimene iwe unanena,

wakodwa ndi mawu a mʼkamwa mwako.

3Tsono popeza iwe mwana wanga

wadziponya mʼmanja mwa mnansi wako, chita izi kuti udzipulumutse:

pita msanga ukamupemphe mnansi wako;

kuti akumasule!

4Usagone tulo,

usawodzere.

5Dzipulumutse monga imachitira mphoyo mʼdzanja la mlenje,

ndi monga imachitira mbalame mu msampha wa munthu wosaka.

6Pita kwa nyerere, mlesi iwe;

kaonetsetse njira zake kuti uphunzirepo kanthu!

7Zilibe mfumu,

zilibe woyangʼanira kapena wolamulira,

8komabe zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe

ndipo zimatuta chakudyacho nthawi yokolola.

9Kodi uzingogonabe pamenepo mpaka liti mlesi iwe?

Kodi tulo tako tidzatha liti?

10Ukati ndingogona pangʼono, ndingowodzera pangʼono

ndingopinda manjawa pangʼono kuti ndipumule,

11umphawi udzakugwira ngati mbala

ndipo usiwa udzafika ngati munthu wachifwamba.

12Munthu wachabechabe, munthu woyipa,

amangoyendayenda ndi kumayankhula zoyipa,

13amatsinzinira maso ake,

namakwakwaza mapazi ake

ndi kulozaloza ndi zala zake,

14amalingalira zoyipa ndi mtima wake wachinyengo

ndipo nthawi zonse amangokhalira kuyambitsa mikangano pakati pa anthu.

15Nʼchifukwa chake tsoka lidzamugwera modzidzimutsa;

adzawonongeka msangamsanga popanda chomupulumutsa.

16Pali zinthu zisanu ndi chimodzi zimene Yehova amadana nazo,

zinthu zisanu ndi ziwiri zimene zimamunyansa:

17maso onyada,

pakamwa pabodza,

manja akupha munthu wosalakwa,

18mtima wokonzekera kuchita zoyipa,

mapazi othamangira msanga ku zoyipa,

19mboni yonama yoyankhula mabodza

komanso munthu amene amayambitsa mikangano pakati pa abale.

Chenjezo pa za Chigololo

20Mwana wanga, usunge malamulo a abambo ako;

ndipo usataye zimene anakuphunzitsa amayi ako.

21Zimenezi uzimatirire pa mtima pako masiku onse,

uzimangirire mʼkhosi mwako.

22Ukamayenda, zidzakulozera njira;

ukugona, zidzakulondera;

ukudzuka, zidzakuyankhula.

23Paja malamulo awa ali ngati nyale,

malangizowa ali ngati kuwunika,

ndipo chidzudzulo cha mwambo ndiwo

moyo weniweni,

24kukupulumutsa kwa mkazi wadama,

zimenezi zidzakutchinjiriza kwa mkazi wadama, ndi kukuthandiza kuti usamvere mawu oshashalika a mkazi wachiwerewere.

25Mu mtima wako usakhumbire kukongola kwake,

asakukope ndi zikope zake,

26paja mkazi wadama amakusandutsa kukhala ngati nyenyeswa za buledi

ndipo mkazi wa mwini wake amasokonezeratu moyo wako wonse.

27Kodi munthu angathe kutenga moto

zovala zake osapsa?

28Kodi munthu angathe kuyenda pa makala amoto

mapazi ake osapserera?

29Ndizo zimachitikira munthu amene amagonana ndi mkazi wa munthu wina.

Aliyense wokhudza mkazi wotere adzalangidwa.

30Paja anthu sayinyoza mbala ikaba

chifukwa chakuti ili ndi njala.

31Komabe ngati mbalayo igwidwa iyenera kulipira kasanu nʼkawiri,

ngakhale kulandidwa katundu wa mʼnyumba mwake.

32Munthu wochita chigololo ndi wopanda nzeru.

Wochita zimenezi amangodziwononga yekha.

33Adzalandira mabala ndi mʼnyozo,

ndipo manyazi ake sadzamuchokera.

34Paja nsanje imachititsa mwini mkaziyo kukalipa,

ndipo sadzachita chifundo pobwezera.

35Iye savomera dipo lililonse;

sangapepeseke ngakhale umupatse mphatso zochuluka motani.

Hoffnung für Alle

Sprüche 6:1-35

Vier Gefahren

1Mein Sohn, hast du dich mit Handschlag dazu verpflichtet, für die Schulden eines Fremden aufzukommen? 2Bist du an ein Versprechen gebunden, das du gegeben hast? Sind deine eigenen Worte dir zur Schlinge geworden? 3Dann gibt es nur einen Rat: Versuch so schnell wie möglich, davon freizukommen! Der Gläubiger hat dich in seiner Gewalt – also geh zu ihm und bestürme ihn so lange, bis er dich freigibt. 4Schieb es nicht auf, gönn dir keine Ruhe! 5Versuch mit allen Mitteln, dich herauszuwinden wie ein Tier aus der Falle des Jägers!

6Beobachte die Ameisen, du Faulpelz! Nimm dir ein Beispiel an ihnen, damit du endlich klug wirst: 7Kein Vorgesetzter treibt sie an; 8trotzdem arbeiten sie den ganzen Sommer über fleißig und legen in der Erntezeit ihre Vorräte an. 9Wie lange willst du noch im Bett bleiben, du Faulpelz? Wann stehst du endlich auf? 10»Lass mich noch ein bisschen schlafen«, sagst du, »ich will nur noch ein Weilchen die Augen zumachen und kurz verschnaufen!« 11Doch während du dich ausruhst, ist die Armut plötzlich da, und die Not überfällt dich wie ein Räuber.

12Einen nichtswürdigen und gemeinen Menschen erkennt man an seinem Verhalten: Er verbreitet Lügen, 13zwinkert seinen Komplizen vielsagend zu und macht alle möglichen Gesten, mit denen er andere hinters Licht führen will. 14Sein Wesen ist falsch und heimtückisch, er hat ständig Böses im Sinn und legt es immer auf einen Streit an. 15Darum wird das Unglück unerwartet über ihn hereinbrechen; er findet plötzlich ein schreckliches Ende – ohne jede Hoffnung auf Rettung!

16Sechs Dinge sind dem Herrn verhasst, und auch das siebte verabscheut er:6,16 Es handelt sich um einen sogenannten »Zahlenspruch«: Verschiedene Beispiele werden zusammengestellt und an ein bestimmtes Zahlenschema gebunden.

17Augen, die überheblich blicken;

eine Zunge, die Lügen verbreitet;

Hände, die unschuldige Menschen töten;

18ein Herz, das finstere Pläne schmiedet;

Füße, die schnell laufen, um Böses zu tun;

19ein Zeuge, der falsche Aussagen macht;

ein Mensch, der Freunde gegeneinander aufhetzt.

20Mein Sohn, gehorche deinem Vater und deiner Mutter und schlage ihre Weisungen nicht in den Wind! 21Erinnere dich zu jeder Zeit an ihre Worte und bewahre sie in deinem Herzen! 22Tag und Nacht sollen sie dich begleiten, dich beschützen, wenn du schläfst, und dich beraten, sobald du morgens aufwachst. 23Denn die Erziehung deiner Eltern ist wie ein Licht, das dir den richtigen Weg weist; ihre Ermahnungen eröffnen dir den Zugang zu einem erfüllten Leben. 24Sie warnen dich vor der Frau eines anderen, vor der Ehebrecherin, die dich mit betörenden Worten lockt. 25Lass dich nicht von ihren Reizen einfangen, begehre sie nicht, wenn sie dir schöne Augen macht. 26Für eine Hure bezahlst du nur so viel wie für ein Brot, aber wenn du mit einer verheirateten Frau die Ehe brichst, bezahlst du es teuer mit deinem Leben.

27Kann man etwa Feuer in der Manteltasche tragen, ohne den Mantel in Brand zu stecken? 28Kann man etwa barfuß über glühende Kohlen gehen, ohne sich die Füße zu verbrennen? 29Genauso schlimm sind die Folgen, wenn man mit der Frau eines anderen schläft: Keiner, der es tut, bleibt ungestraft. 30Wer Brot stiehlt, weil er Hunger hat, wird nicht verachtet. 31Wenn er ertappt wird, muss er es siebenfach ersetzen, aber das kostet ihn höchstens seinen ganzen Besitz. 32Wer dagegen die Ehe bricht, hat den Verstand verloren und richtet sich selbst zugrunde. 33Er handelt sich Schläge ein und erntet dazu noch Schimpf und Schande, die er nie wieder loswird. 34Ein eifersüchtiger Ehemann schnaubt vor Wut, und in seiner Rachsucht kennt er kein Erbarmen. 35Keine Entschädigung, die du ihm anbietest, kein noch so großes Geschenk wird ihn besänftigen.