Miyambo 7 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 7:1-27

Za Mkazi Wachigololo

1Mwana wanga, mvera mawu anga;

usunge bwino malamulo angawa.

2Utsate malamulo anga ndipo udzakhala ndi moyo;

samala malangizo angawa monga uchitira ndi maso ako.

3Uchite ngati wawamangirira pa zala zako,

ndiponso ngati kuti wawalemba pa mtima pako.

4Nzeru uyiwuze kuti, “Iwe ndiwe mlongo wanga,”

ndipo khalidwe lomvetsa bwino zinthu ulitchule kuti, “Bwenzi langa lapamtima.”

5Zidzakuteteza kwa mkazi wachigololo

ndiponso zidzakuthandiza kusamvera mawu oshashalika a mkazi wachilendo.

6Tsiku lina pa zenera la nyumba yanga

ndinasuzumira pa zenera.

7Ndinaona pakati pa anthu opusa,

pakati pa anyamata,

mnyamata wina wopanda nzeru.

8Iye ankayenda njira yodutsa pafupi ndi nyumba ya mkaziyo,

kuyenda molunjika nyumba ya mkaziyo.

9Inali nthawi yachisisira madzulo,

nthawi ya usiku, kuli mdima.

10Ndipo mkaziyo anadzakumana naye,

atavala ngati munthu wachiwerewere wa mtima wonyenga.

11(Mkaziyo ndi wolongolola ndiponso nkhutukumve,

iye ndi wosakhazikika pa khomo.

12Mwina umupeza pa msewu, mwina umupeza pa msika,

ndipo amadikirira munthu pa mphambano iliyonse).

13Tsono amagwira mnyamatayo ndi kupsompsona

ndi nkhope yake yopanda manyazi amamuwuza kuti,

14“Ndinayenera kupereka nsembe zachiyanjano.

Lero ndakwaniritsa malumbiro anga.

15Choncho ndinabwera kudzakumana nawe;

ndinkakufunafuna ndipo ndakupeza!

16Pa bedi panga ndayalapo

nsalu zosalala zokongola zochokera ku Igupto.

17Pa bedi panga ndawazapo zonunkhira

za mure, mafuta onunkhira a aloe ndi sinamoni.

18Bwera, tiye tikhale malo amodzi kukondwerera chikondi mpaka mmawa;

tiye tisangalatsane mwachikondi!

19Mwamuna wanga kulibe ku nyumbako;

wapita ulendo wautali:

20Anatenga thumba la ndalama

ndipo adzabwera ku nyumba mwezi ukakhwima.”

21Ndi mawu ake onyengerera amamukakamiza mnyamatayo;

amukopa ndi mawu ake oshashalika.

22Nthawi yomweyo chitsiru chimamutsatira mkaziyo

ngati ngʼombe yopita kukaphedwa,

monga momwe mbawala ikodwera mu msampha,

23mpaka muvi utalasa chiwindi chake,

chimakhala ngati mbalame yothamangira mʼkhwekhwe,

osadziwa kuti moyo wake uwonongeka.

24Tsono ana inu, ndimvereni;

mvetsetsani zimene ndikunena.

25Musatengeke mtima ndi njira za mkazi ameneyu;

musasochere potsata njira zake.

26Paja iye anagwetsa anthu ambiri;

wapha gulu lalikulu la anthu.

27Nyumba yake ndi njira yopita ku manda,

yotsikira ku malo a anthu akufa.

Hoffnung für Alle

Sprüche 7:1-27

Die treulose Frau

1Mein Sohn, beachte, was ich dir sage, halte unter allen Umständen daran fest! 2Wenn du dich danach richtest, so wird dein Leben gelingen. Hüte meine Worte wie deinen Augapfel, 3denke jederzeit über sie nach und schreibe sie dir ins Herz! 4Lass die Weisheit eine Schwester für dich sein, mach dir die Einsicht zur besten Freundin! 5Das wird dich schützen vor der Frau eines anderen Mannes, vor der Verführerin, die dir mit schmeichelnden Worten den Kopf verdrehen will.

6Einmal stand ich am Fenster und schaute durch das Gitter hinaus auf die Straße. 7Dort sah ich eine Gruppe noch unerfahrener junger Männer vorbeikommen. Besonders einer von ihnen fiel mir durch sein kopfloses Verhalten auf. 8Er lief die Straße hinunter, an deren Ecke eine bestimmte Frau wohnte, und näherte sich ihrem Haus.

9Inzwischen war die Nacht hereingebrochen, und es war dunkel geworden. 10Da kam sie ihm entgegen, herausgeputzt und zurechtgemacht wie eine Hure. Sie verfolgte keine guten Absichten – so viel stand fest! 11Leidenschaftlich und hemmungslos, wie sie war, hielt sie es zu Hause nie lange aus. 12Man sah sie jeden Tag draußen auf den Straßen und Plätzen, an jeder Straßenecke stand sie und schaute sich nach einem neuen Opfer um.

13Jetzt ging sie auf den jungen Mann zu, umarmte und küsste ihn. Mit herausforderndem Blick sagte sie: 14»Heute habe ich ein Gelübde eingelöst und Gott ein Friedensopfer dargebracht. Davon ist noch Fleisch übrig, 15also bin ich hinausgegangen, um dich zu suchen. Endlich habe ich dich gefunden! 16Ich habe mein Bett mit schönen bunten Decken aus Ägypten gepolstert 17und mit herrlichem Parfüm besprengt7,17 Wörtlich: und mit Myrrhe, Aloe und Zimt besprengt.. 18Komm doch mit! Wir wollen uns die ganze Nacht hindurch lieben und uns bis zum Morgen vergnügen! 19Mein Mann ist nicht da, er macht gerade eine lange Reise. 20Er hat viel Geld mitgenommen und kommt frühestens in zwei Wochen wieder zurück7,20 Wörtlich: und kommt erst bei Vollmond wieder zurück.

21Ihre Einladung klang verlockend, und so überredete sie den jungen Mann. 22Er folgte ihr ins Haus wie ein Ochse, der zum Schlachten geführt wird – nichts ahnend wie ein Hirsch, der in die Schlinge des Jägers gerät:7,22 So in Anlehnung an die griechische Übersetzung. Der hebräische Text ist nicht sicher zu deuten. 23Plötzlich schnappt die Falle zu, und ein Pfeil durchbohrt ihm das Herz! Ohne dass er etwas von der tödlichen Gefahr merkte, hatte sie ihn gefangen wie einen Vogel im Netz.

24Darum hört auf meine Warnung, ihr jungen Männer, und befolgt sie! 25Lasst euch von solch einer Frau nicht verführen, sondern geht ihr aus dem Weg! 26Denn sie hat schon viele Männer zu Fall gebracht, die Zahl ihrer Opfer ist groß. 27Ihr Haus steht am Rand des Abgrunds; wer zu ihr geht, den reißt sie mit in den Tod.