Miyambo 30 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 30:1-33

Mawu a Aguri

1Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.

Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

2“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;

ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.

3Sindinaphunzire nzeru,

ndipo Woyerayo sindimudziwa.

4Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?

Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?

Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?

Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?

Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!

Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

5“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;

Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.

6Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,

kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

7“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri

musandimane zimenezo ndisanafe:

8Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.

Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.

Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku

9kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,

nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’

Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,

potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake

kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

11“Alipo ena amene amatemberera abambo awo,

ndipo sadalitsa amayi awo.

12Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima

komatu sanachotse zoyipa zawo.

13Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,

amene amakweza zikope modzitukumula.

14Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga

ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni

moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.

Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”

15“Msundu uli ndi ana aakazi awiri

iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”

“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,

zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’

16Manda, mkazi wosabala,

nthaka yosakhuta madzi

ndiponso moto womangoyakirayakira!”

17Aliyense amene amanyoza abambo ake,

ndi kunyozera kumvera amayi ake,

makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso

ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.

18Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,

zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.

19Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;

mmene iyendera njoka pa thanthwe;

mmene chiyendera chombo pa nyanja;

ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.

20Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:

Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake

iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”

21Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,

pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:

22Kapolo amene wasanduka mfumu,

chitsiru chimene chakhuta,

23mkazi wonyozeka akakwatiwa

ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.

24Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,

komatu ndi zochenjera kwambiri:

25Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,

komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;

26mbira zili ngati anthu opanda mphamvu

komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;

27dzombe lilibe mfumu,

komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.

28Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja

komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.

29“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,

pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:

30Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,

ndipo suthawa kanthu kalikonse.

31Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,

ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

32“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,

kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,

ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!

33Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,

ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,

ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

Thai New Contemporary Bible

สุภาษิต 30:1-33

คำสอนของอากูร์

1นี่คือคำสอนของอากูร์บุตรยาเคห์ เป็นถ้อยคำที่ได้รับการดลใจ30:1 หรือคำสอนของอากูร์บุตรยาเคห์แห่งมัสสา

เขากล่าวกับอิธีเอลว่า

“ข้าแต่พระเจ้า ข้าพระองค์อ่อนล้า

แต่ข้าพระองค์มีชัยได้30:1 ในภาษาฮีบรูอาจมีความหมายอีกอย่างหนึ่งว่าเขากล่าวกับอิธีเอล / กับอิธีเอลและกับอูคาลว่า หรือ“ข้าแต่พระเจ้า ข้าพระองค์อ่อนล้า / ข้าแต่พระเจ้า ข้าพระองค์อ่อนล้าและระโหยโรยแรง

2ข้าพเจ้าโง่เขลาเกินกว่าจะเป็นมนุษย์

ที่จริง ข้าพเจ้าไม่มีความเข้าใจอย่างมนุษย์ทั่วไป

3ข้าพเจ้าไม่ได้เรียนรู้สติปัญญา

และไม่รู้จักองค์บริสุทธิ์

4ใครเล่าได้ขึ้นสู่สวรรค์และลงมา?

ใครเล่าได้กำกระแสลมไว้ในอุ้งมือ?

ใครเล่าได้ห่อหุ้มห้วงน้ำไว้ในเสื้อคลุม?

ใครเล่าได้สถาปนาทั่วทุกมุมโลก?

ผู้นั้นมีนามว่าอะไร? และบุตรของผู้นั้นมีนามว่าอะไร?

แน่นอน เจ้ารู้!

5“พระดำรัสทุกคำของพระเจ้าไม่มีข้อผิดพลาด

พระองค์ทรงเป็นโล่สำหรับบรรดาผู้ที่ลี้ภัยในพระองค์30:5 ดู2ซมอ.22:31-32 และสดด.18:30-31

6อย่าเพิ่มเติมพระวจนะของพระองค์

มิฉะนั้นพระองค์จะทรงตำหนิเจ้า และเจ้าจะถูกจับได้ว่าโกหก

7“ข้าพระองค์ทูลขอสองสิ่งจากพระองค์

ขออย่าทรงปฏิเสธก่อนที่ข้าพระองค์จะตายไป

8คือขอให้สิ่งเท็จเทียมและคำโกหกห่างไกลจากข้าพระองค์

ขออย่าให้ข้าพระองค์ยากจนหรือร่ำรวย

แต่ขอโปรดประทานอาหารประจำวันแก่ข้าพระองค์

9มิฉะนั้นข้าพระองค์อาจอิ่มหนำสำราญแล้วปฏิเสธพระเจ้า

และพูดว่า ‘องค์พระผู้เป็นเจ้าเป็นใครกัน?’

หรือข้าพระองค์อาจยากจนแล้วลักขโมย

ก็ลบหลู่พระนามพระเจ้าของข้าพระองค์

10“อย่ากล่าวร้ายคนรับใช้ให้นายเขาฟัง

เกรงว่าผู้นั้นจะแช่งด่าเจ้า และเจ้าต้องชดใช้

11“มีบางคนแช่งด่าพ่อ

และไม่อวยพรแม่ของตน

12บางคนคิดว่าตัวเองบริสุทธิ์

ทั้งที่ยังไม่ได้รับการชำระมลทิน

13บางคนยโสโอหังยิ่งนัก

บางคนปรายตาดูถูกผู้อื่น

14บางคนฟันของเขาคือดาบ

บางคนกรามของเขาคือมีด

เขมือบผู้ยากไร้ไปจากแผ่นดิน

เขมือบคนขัดสนจากมวลมนุษยชาติ

15“ปลิงมีปากสองปาก

มันร้องว่า ‘เอาอีก! เอาอีก!’

“มีสามสิ่งที่ไม่เคยอิ่มหนำ

ที่จริง มีสี่สิ่งที่ไม่เคยพูดว่า ‘พอแล้ว!’

16คือแดนผู้ตายครรภ์ของหญิงหมัน

แผ่นดินที่ไม่เคยอิ่มน้ำ

และไฟที่ไม่เคยพูดว่า ‘พอแล้ว!’

17“ตาที่เย้ยหยันพ่อ

ที่ดูหมิ่นไม่เชื่อฟังแม่ผู้ชรา

จะถูกกาแห่งหุบเขาจิกออกมา

จะถูกแร้งรุมกิน

18“มีสามสิ่งที่ทำให้ข้าพเจ้าประหลาดใจ

ที่จริง มีสี่สิ่งที่ข้าพเจ้าไม่เข้าใจ

19คือการเคลื่อนไหวของนกอินทรีในท้องฟ้า

การเลื้อยของงูบนก้อนหิน

การแล่นของเรือในท้องทะเล

และความสัมพันธ์ของชายหนุ่มกับหญิงสาว

20นี่คือการปรนเปรอตนเองของหญิงสำส่อน

นางกินแล้วเช็ดปาก

และพูดว่า ‘ฉันไม่ได้ทำอะไรผิด’

21“มีสามสิ่งที่ทำให้แผ่นดินโลกสั่นสะเทือน

ที่จริง มีสี่สิ่งซึ่งโลกทนไม่ได้

22คือคนรับใช้ที่กลายเป็นกษัตริย์

คนโฉดเขลาที่มีอาหารเหลือเฟือ

23หญิงที่ไม่มีใครรักได้แต่งงาน

สาวใช้ที่ครองตำแหน่งแทนนายหญิง

24“มีสี่สิ่งในโลกซึ่งเล็กกระจิริด

แต่ฉลาดเหลือล้ำ ได้แก่

25มด กำลังน้อยนิด

แต่ก็ยังรู้จักสะสมอาหารในฤดูร้อน

26ตัวตุ่นผา แรงน้อย

แต่ก็ยังทำรังในซอกหิน

27ตั๊กแตน ไม่มีราชา

แต่ก็ยังรวมตัวกันไปเป็นขบวน

28จิ้งจก เอามือจับก็ได้

แต่ก็ยังพบมันในพระราชวัง

29“มีสามสิ่งที่มีท่วงท่าสง่างาม

ที่จริง มีสี่สิ่งซึ่งเคลื่อนไหวอย่างองอาจ

30คือราชสีห์ ผู้เป็นเจ้าป่า

มันไม่ถอยหนีสิ่งใด

31พ่อไก่ที่เดินป้อ แพะตัวผู้

และกษัตริย์ที่ไม่มีใครต่อต้าน

32“หากเจ้าได้ทำตัวโง่เขลาด้วยการยกย่องตัวเอง

หรือหากเจ้าได้วางแผนชั่ว

จงเอามืออุดปากของเจ้าเสีย!

33เพราะเมื่อกวนนมก็ได้เนย

หรือเมื่อกระแทกจมูกก็ได้เลือดกำเดาฉันใด

เมื่อกวนโมโหก็ได้การวิวาทฉันนั้น”