Miyambo 30 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 30:1-33

Mawu a Aguri

1Nawa mawu a Aguri mwana wa Yake wa ku Masa:

Munthuyo anati kwa Itieli, “Inu Mulungu, ine ndatopa.

Inu Mulungu, ine ndatopa. Ndalefukiratu.

2“Ine ndine munthu wopusa kuposa anthu onse;

ndilibe nzeru zomvetsa zinthu zonga za munthu.

3Sindinaphunzire nzeru,

ndipo Woyerayo sindimudziwa.

4Kodi ndani anakwera kumwamba ndi kutsikako?

Ndani anafumbatapo mphepo mʼmanja mwake?

Ndani anamanga madzi mʼchovala chake?

Ndani anakhazikitsa mathero onse a dziko lapansi?

Dzina lake ndani? Ndiwuze ngati ukudziwa!

Ndipo mwana wake dzina lake ndani?

5“Mawu ali wonse a Mulungu ndi opanda cholakwika;

Iye ndi chishango kwa amene amathawira kwa Iye.

6Usawonjezepo kanthu pa mawu ake,

kuopa kuti Iye angadzakudzudzule ndi kukupeza kuti ndiwe wabodza.”

7“Inu Yehova, ndikukupemphani zinthu ziwiri

musandimane zimenezo ndisanafe:

8Choyamba, mundichotsere kutali nane mabodza ndi chinyengo.

Chachiwiri, ndisakhale mʼmphawi kapena munthu wachuma.

Koma muzindidyetsa chakudya chondikwanira tsiku ndi tsiku

9kuopa kuti ndikakhuta kwambiri ndingayambe kukukanani,

nʼkumanena kuti, ‘Yehova ndiye yaninso?’

Kuopanso kuti ndikakhala wosauka ndingayambe kuba,

potero nʼkuyipitsa dzina la Mulungu wanga.”

10“Usamusinjirire wantchito kwa mbuye wake

kuopa kuti angakutemberere ndipo iweyo nʼkupezeka wolakwa.”

11“Alipo ena amene amatemberera abambo awo,

ndipo sadalitsa amayi awo.

12Pali ena amene amadziyesa okha oyera mtima

komatu sanachotse zoyipa zawo.

13Pali ena ndi odzitukumula kwambiri,

amene amakweza zikope modzitukumula.

14Pali ena amene mano awo ali ngati malupanga

ndipo zibwano zawo zili ngati mipeni

moti amadya amphawi ndi kuwachotsa pa dziko lapansi.

Amachotsanso anthu osauka pakati pa anzawo.”

15“Msundu uli ndi ana aakazi awiri

iwo amalira kuti, ‘Tipatseni! Tipatseni!’ ”

“Pali zinthu zitatu zimene sizikhuta,

zinthu zinayi zimene sizinena kuti, ‘Takhuta!’

16Manda, mkazi wosabala,

nthaka yosakhuta madzi

ndiponso moto womangoyakirayakira!”

17Aliyense amene amanyoza abambo ake,

ndi kunyozera kumvera amayi ake,

makwangwala a ku chigwa adzamukolowola maso

ndipo mphungu zidzadya mnofu wake.

18Pali zinthu zitatu zimene zimandidabwitsa,

zinthu zinayi zimene ine sindizimvetsetsa.

19Ndipo ndi izi: mmene chiwulukira chiwombankhanga mlengalenga;

mmene iyendera njoka pa thanthwe;

mmene chiyendera chombo pa nyanja;

ndiponso mmene mwamuna achitira akakhala ndi namwali.

20Umu ndi mʼmene mkazi amachitira atachita chigololo:

Atatha kudya ndi kupukuta pakamwa pake

iye amanena kuti “Sindinachite kalikonse kolakwa.”

21Pali zinthu zitatu zimene zimanjenjemeretsa dziko lapansi,

pali zinthu zinayi zimene dziko lapansi silingathe kuzipirira:

22Kapolo amene wasanduka mfumu,

chitsiru chimene chakhuta,

23mkazi wonyozeka akakwatiwa

ndiponso wantchito wamkazi akalanda mwamuna wa mbuye wake.

24Pali zinthu zinayi zingʼonozingʼono pa dziko lapansi,

komatu ndi zochenjera kwambiri:

25Nyerere zili ngati anthu opanda mphamvu,

komatu zimasungiratu chakudya chake nthawi ya chilimwe;

26mbira zili ngati anthu opanda mphamvu

komatu zimakonza pokhalapo pawo mʼmiyala;

27dzombe lilibe mfumu,

komatu lonse limakhala mʼmagulumagulu poyenda.

28Buluzi ungathe kumugwira mʼmanja

komatu amapezeka mʼnyumba za mafumu.

29“Pali zinthu zitatu zimene zimayenda chinyachinya,

pali zinthu zinayi zimene zimayenda monyadira:

30Mkango umene uli wamphamvu kuposa nyama zonse,

ndipo suthawa kanthu kalikonse.

31Tambala woyenda chinyachinya, mbuzi yayimuna,

ndiponso mfumu yoyenda pakati pa anthu ake.

32“Ngati wakhala ukupusa ndi kumadzikweza wekha,

kapena ngati wakhala ukukonzekera zoyipa,

ndiye khala kaye chete, uganizire bwino!

33Paja pakutha mkaka mafuta amapangidwa,

ndipo ukapsinya mphuno, magazi amatuluka,

ndipo mikangano imakhalapo ukalimbikira kukwiya.”

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 30:1-33

亞古珥的箴言

1以下是雅基的兒子亞古珥的箴言。

這人說:上帝啊,我很疲倦;

上帝啊,我很疲倦,精疲力盡。30·1 希伯來文或譯「這人對以鐵說,對以鐵和烏甲說:」

2我比眾人都愚蠢,

不具備人的悟性。

3我從未學到智慧,

也不認識至聖者。

4誰升上高天又降下來?

誰將風聚在掌中?

誰將眾水裹在衣服裡?

誰定了地的邊界?

祂叫什麼名字?

祂兒子叫什麼名字?

你知道嗎?

5上帝的話句句千真萬確,

祂作投靠祂之人的盾牌。

6你不可對祂的話有所添加,

免得祂責備你,

揭穿你的虛謊。

7上帝啊,我向你求兩件事,

求你在我未死以前賜給我。

8求你使虛偽和謊言遠離我,

求你讓我不貧窮也不富足,

賜給我需用的飲食,

9免得我因為飽足就不認你,

說:「耶和華是誰呢?」

又恐怕我因窮困而偷竊,

以致辱沒我上帝的名。

10別向主人譭謗他的僕人,

免得你受咒詛、擔當罪責。

11有一種30·11 」希伯來文是「世代」,11-14節也相同。人咒詛父親,

不為母親祝福。

12有一種人自以為純潔,

卻沒有洗掉自己的污穢。

13有一種人趾高氣揚,

目空一切。

14有一種人牙如劍,

齒如刀,

要吞吃世間的困苦人和貧窮人。

15水蛭有兩個女兒,

她們不停地叫:「給我!給我!」

三樣東西從不知足,

永不言「夠」的共有四樣:

16陰間、不孕的婦人、

乾旱的土地和火焰。

17嘲笑父親、藐視母親教誨的,

眼睛必被谷中的烏鴉啄出,

被禿鷹吃掉。

18我測不透的妙事有三樣,

我不明白的事共有四樣:

19鷹在空中飛翔之道,

蛇在石上爬行之道,

船在海中航行之道,

男女相愛之道。

20淫婦的道是這樣:

她吃完就擦擦嘴,

說,「我沒有做壞事。」

21使大地震動的事有三樣,

大地無法承受的事共有四樣:

22奴僕做王,

愚人吃飽,

23醜惡女子出嫁,

婢女取代主母。

24地上有四種動物,

身體雖小卻極其聰明:

25螞蟻力量雖小,

卻在夏天儲備糧食;

26石獾雖不強壯,

卻在岩石中築巢穴;

27蝗蟲雖無君王,

卻整齊地列隊前進;

28壁虎雖易捕捉,

卻居住在王宮大內。

29步履威武的有三樣,

走路雄壯的共有四樣:

30威震百獸、從不畏縮的獅子,

31昂首闊步的雄雞,

公山羊和率領軍隊的君王。

32你若行事愚昧、

妄自尊大或圖謀不軌,

就當用手掩口。

33激起憤怒會引起爭端,

正如攪牛奶會攪出奶油,

擰鼻子會擰出血。