Miyambo 28 – CCL & CCBT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 28:1-28

1Munthu woyipa amathawa ngakhale palibe wina womuthamangitsa,

koma wolungama ndi wolimba mtima ngati mkango.

2Pamene mʼdziko muli kuwukirana, dzikolo limakhala ndi olamulira ambiri,

koma anthu omvetsa ndi odziwa zinthu bwino ndiwo angakhazikitse bata mʼdzikolo nthawi yayitali.

3Munthu wosauka amene amapondereza osauka anzake

ali ngati mvula yamkuntho imene imawononga mbewu mʼmunda.

4Amene amakana malamulo amatamanda anthu oyipa,

koma amene amasunga malamulo amatsutsana nawo.

5Anthu oyipa samvetsa za chiweruzo cholungama,

koma amene amafuna kuchita zimene Yehova afuna amachimvetsetsa bwino.

6Munthu wosauka wa makhalidwe abwino

aposa munthu wolemera wa makhalidwe okhotakhota.

7Amene amasunga malamulo ndi mwana wozindikira zinthu,

koma amene amayenda ndi anthu adyera amachititsa manyazi abambo ake.

8Amene amachulukitsa chuma chake polandira chiwongoladzanja chochuluka

amakundikira chumacho anthu ena, amene adzachitira chifundo anthu osauka.

9Wokana kumvera malamulo

ngakhale pemphero lake lomwe limamunyansa Yehova.

10Amene amatsogolera anthu olungama kuti ayende mʼnjira yoyipa

adzagwera mu msampha wake womwe,

koma anthu opanda cholakwa adzalandira cholowa chabwino.

11Munthu wolemera amadziyesa kuti ndi wanzeru,

koma munthu wosauka amene ali ndi nzeru zodziwa zinthu amamutulukira.

12Pamene olungama apambana pamakhala chikondwerero chachikulu;

koma pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro, anthu amabisala.

13Wobisa machimo ake sadzaona mwayi,

koma aliyense amene awulula ndi kuleka machimowo, adzalandira chifundo.

14Ndi wodala munthu amene amaopa Yehova nthawi zonse,

koma amene aumitsa mtima wake adzagwa mʼmavuto.

15Ngati mkango wobuma kapena chimbalangondo cholusa

ndi mmenenso amakhalira munthu woyipa akamalamulira anthu osauka.

16Wolamulira amene samvetsa zinthu ndiye amakhala wankhanza

koma amene amadana ndi phindu lopeza mwachinyengo adzakhala ndi moyo wautali.

17Munthu amene wapalamula mlandu wopha munthu

adzakhala wothawathawa mpaka imfa yake;

wina aliyense asamuthandize.

18Amene amayenda mokhulupirika adzapulumutsidwa

koma amene njira zake ndi zokhotakhota adzagwa mʼdzenje.

19Amene amalima mʼmunda mwake adzakhala ndi chakudya chochuluka,

koma amene amangosewera adzakhala mʼmphawi.

20Munthu wokhulupirika adzadalitsika kwambiri,

koma wofuna kulemera mofulumira adzalangidwa.

21Kukondera si kwabwino,

ena amachita zolakwazo chifukwa cha kachidutswa ka buledi.

22Munthu wowumira amafunitsitsa kulemera

koma sazindikira kuti umphawi udzamugwera.

23Amene amadzudzula mnzake potsiriza pake

mnzakeyo adzamukonda kwambiri, kupambana amene amanena mawu oshashalika.

24Amene amabera abambo ake kapena amayi ake

namanena kuti “kumeneko sikulakwa,”

ndi mnzake wa munthu amene amasakaza.

25Munthu wadyera amayambitsa mikangano,

koma amene amadalira Yehova adzalemera.

26Amene amadzidalira yekha ndi chitsiru,

koma amene amatsata nzeru za ena adzapulumuka.

27Amene amapereka kwa osauka sadzasowa kanthu,

koma amene amatsinzina maso ake adzatembereredwa kwambiri.

28Pamene anthu oyipa apatsidwa ulamuliro anthu amabisala,

koma anthu oyipa akawonongeka olungama amapeza bwino.

Chinese Contemporary Bible (Traditional)

箴言 28:1-28

1惡人未被追趕也逃竄,

義人坦然無懼如雄獅。

2國中有罪,君王常換;

國有哲士,長治久安。

3窮人28·3 窮人」有些抄本作「暴君」。欺壓貧民,

如暴雨沖毀糧食。

4背棄律法的稱讚惡人,

遵守律法的抗拒惡人。

5邪惡之人不明白公義,

尋求耶和華的全然明白。

6行為正直的窮人,

勝過行事邪僻的富人。

7遵守律法的是智慧之子,

與貪食者為伍令父蒙羞。

8人放高利貸牟利,

等於為扶貧者積財。

9人若不聽從律法,

他的禱告也可憎。

10引誘正直人走邪道,

必掉進自己設的陷阱;

但純全無過的人必承受福分。

11富人自以為有智慧,

卻被明智的窮人看透。

12義人得勝,遍地歡騰;

惡人當道,人人躲藏。

13自掩其罪,必不亨通;

痛改前非,必蒙憐憫。

14敬畏上帝必蒙福,

頑固不化必遭禍。

15暴虐的君王轄制窮人,

如咆哮的獅、覓食的熊。

16昏庸的君王殘暴不仁,

恨不義之財的享長壽。

17背負血債者必終生逃亡,

誰也不要幫他。

18純全無過的必蒙拯救,

行為邪僻的轉眼滅亡。

19勤奮耕耘,豐衣足食;

追求虛榮,窮困潦倒。

20忠信的人必大蒙祝福,

急於發財的難免受罰。

21徇私偏袒實不可取,

人卻為一餅而枉法。

22貪婪的人急於發財,

卻不知貧窮即將臨到。

23責備人的至終比諂媚者更受愛戴。

24竊取父母之財而不知罪者與匪類無異。

25貪得無厭的人挑起紛爭,

信靠耶和華的富足昌盛。

26愚人心中自以為是,

憑智慧行事的平安穩妥。

27賙濟窮人的一無所缺,

視而不見的多受咒詛。

28惡人當道,人人躲藏;

惡人滅亡,義人增多。