Miyambo 22 – CCL & TNCV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 22:1-29

1Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri;

kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.

2Wolemera ndi wosauka ndi ofanana;

onsewa anawalenga ndi Yehova.

3Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala,

koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.

4Mphotho ya munthu wodzichepetsa

ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.

5Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha,

koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.

6Mwana muzimuphunzitsa njira yake,

ndipo akadzakalamba sadzachokamo.

7Wolemera amalamulira wosauka,

ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.

8Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto,

ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.

9Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika,

pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.

10Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha;

mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.

11Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino,

adzakhala bwenzi la mfumu.

12Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu,

koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.

13Munthu waulesi amati,

“Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”

14Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama;

amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.

15Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana,

koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.

16Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake,

ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.

Malangizo a Anthu Anzeru

17Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru;

uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.

18Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako

ndi wokonzeka kuziyankhula.

19Ndakuphunzitsa zimenezi lero

koma makamaka uziopa Yehova.

20Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu

okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,

21malangizo okudziwitsa zolungama

ndi zoona

ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?

22Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka,

ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,

23pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo

ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.

24Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima

ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya

25kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake

ndi kukodwa mu msampha.

26Usakhale munthu wopereka chikole

kapena kukhala mboni pa ngongole;

27ngati ulephera kupeza njira yolipirira

adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.

28Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale

amene anayikidwa ndi makolo ako.

29Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake?

Iye adzatumikira mafumu;

sadzatumikira anthu wamba.

Thai New Contemporary Bible

สุภาษิต 22:1-29

1ชื่อเสียงดีน่าปรารถนายิ่งกว่าทรัพย์สมบัติมหาศาล

เป็นที่ยกย่องก็ดีกว่าได้เงินหรือทอง

2คนรวยคนจนก็เหมือนกันอย่างหนึ่ง

คือองค์พระผู้เป็นเจ้าทรงสร้างพวกเขาทั้งหมด

3คนมีวิจารณญาณเห็นภัยอันตรายและหลบเข้าที่กำบัง

ส่วนคนโง่เดินลุยต่อไปและต้องทุกข์ทนกับผลที่ตามมา

4ความถ่อมสุภาพคือการยำเกรงองค์พระผู้เป็นเจ้า

รางวัลของมันคือ ความมั่งคั่ง เกียรติ และชีวิต

5เส้นทางของคนชั่วมีกับดักและตาข่าย

ส่วนผู้ที่ปกป้องชีวิตของตนก็หลีกห่างจากทางนั้น

6จงอบรมเด็กในทางที่เขาควรจะไป22:6 หรือจงให้เด็กเริ่มต้นไปในทางที่ควร

และเมื่อเขาโตขึ้น เขาจะไม่หันเหไปจากทางนั้น

7คนรวยปกครองคนจน

ลูกหนี้ก็เป็นทาสของเจ้าหนี้

8ผู้หว่านความอยุติธรรมก็เก็บเกี่ยวความทุกข์ร้อน

อำนาจอันน่าสะพรึงกลัวของเขาจะถูกทำลายลง

9ความสุขมีแก่คนใจกว้าง

เพราะเขาแบ่งปันอาหารแก่ผู้ยากไร้

10จงขับไล่คนชอบเยาะเย้ยออกไป การต่อสู้ชิงดีจะได้จบสิ้น

การสบประมาทและการทะเลาะวิวาทจะได้ยุติ

11ผู้ที่รักจิตใจอันบริสุทธิ์และมีวาจาอ่อนโยน

จะได้เป็นมิตรกับกษัตริย์

12พระเนตรขององค์พระผู้เป็นเจ้าทรงปกป้องความรู้

แต่ทรงลบล้างถ้อยคำของคนไม่ซื่อสัตย์

13คนเกียจคร้านพูดว่า “มีสิงโตอยู่ข้างนอก!”

“ฉันจะถูกมันฆ่ากลางถนน!”

14ปากของหญิงแพศยาเหมือนหลุมลึก

ผู้ที่องค์พระผู้เป็นเจ้าทรงสาปแช่งจะตกลงไปในนั้น

15ความเขลาฝังแน่นอยู่ในใจของเด็ก

แต่ไม้เรียวที่ตีสั่งสอนจะช่วยไล่มันออกไป

16ผู้ที่ขูดรีดคนยากจนเพื่อเพิ่มความมั่งคั่งให้ตนเอง

และผู้ที่ให้ของกำนัลแก่คนร่ำรวย ทั้งสองจะมาถึงความขัดสน

คำสอน

คำสอนที่

17จงเอียงหูฟังคำสอนของปราชญ์

และจงใส่ใจในความรู้ของเรา

18เพราะน่าชื่นใจ เมื่อเจ้ารักษาถ้อยคำเหล่านั้นไว้ในใจ

และเมื่อทุกถ้อยคำนั้นติดปากของเจ้า

19เพื่อเจ้าจะไว้วางใจในองค์พระผู้เป็นเจ้า

เราสอนเจ้าในวันนี้ ใช่ แม้กระทั่งเจ้า

20เราได้เขียนคำสอนสามสิบประการไว้ให้เจ้าไม่ใช่หรือ?

เป็นคำแนะนำและความรู้

21สอนเจ้าให้เป็นคนซื่อสัตย์และพูดจาน่าเชื่อถือ

เพื่อเจ้าจะกลับไปรายงานผู้ที่เจ้ารับใช้ได้อย่างถูกต้อง

คำสอนที่

22อย่าขูดรีดคนจน เพราะเขาจนอยู่แล้ว

และอย่าบีบคั้นคนขัดสนในศาล

23เพราะองค์พระผู้เป็นเจ้าจะทรงว่าความให้เขา

และจะเล่นงานผู้ที่เล่นงานเขา

คำสอนที่

24อย่าผูกมิตรกับคนใจร้อน

อย่าคบหากับคนที่ฉุนเฉียวง่าย

25มิฉะนั้นเจ้าจะเอาอย่างเขา

แล้วพาตัวเองไปติดกับ

คำสอนที่

26อย่าริอ่านจับมือวางมัดจำ

หรือเป็นผู้ค้ำประกันในการกู้หนี้ยืมสิน

27หากเจ้าไม่มีจะจ่ายให้

แม้ที่นอนก็ยังจะถูกกระชากไปจากหลังของเจ้า

คำสอนที่

28อย่าเคลื่อนย้ายหลักเขตเก่าแก่

ซึ่งบรรพบุรุษของเจ้าได้ปักไว้

คำสอนที่

29เจ้าเห็นคนที่เชี่ยวชาญในงานของตนไหม?

เขาจะได้รับใช้กษัตริย์

เขาจะไม่ต้องทำงานให้กับคนสามัญ