Miyambo 11 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 11:1-31

1Muyeso wachinyengo Yehova umamunyansa,

koma amakondwera ndi muyeso woyenera.

2Kunyada kukalowa, pamafikanso manyazi,

koma pamene pali kudzichepetsa pameneponso pali nzeru.

3Ungwiro wa anthu olungama umawatsogolera,

koma anthu osakhulupirika amawonongeka ndi chinyengo chawo.

4Chuma sichithandiza pa tsiku lawukali wa Mulungu,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

5Chilungamo cha anthu angwiro chimawongolera moyo wawo,

koma ntchito zoyipa zimagwetsa mwini wake yemweyo.

6Chilungamo cha anthu oyera mtima chimawapulumutsa,

koma anthu onyenga adzagwidwa ndi zilakolako zawo zomwe.

7Pamene munthu woyipa wafa, chiyembekezo chake chimathanso.

Chiyembekezo cha munthu wosalungama chimawonongeka.

8Munthu wolungama amapulumutsidwa ku mavuto,

koma mʼmalo mwake amagwa mʼmavutomo ndi anthu oyipa.

9Munthu wosapembedza amawononga mnansi wake ndi pakamwa pake,

koma munthu wolungama amapulumuka chifukwa cha kudziwa zinthu.

10Anthu olungama zinthu zikamawayendera bwino, mzinda wonse umakondwera,

ndipo oyipa akamawonongeka anthu amafuwula mwachimwemwe.

11Mzinda umakwezeka chifukwa cha madalitso a anthu oyera mtima,

koma umawonongedwa chifukwa cha pakamwa pa anthu oyipa.

12Munthu wonyoza mnzake ndi wopanda nzeru,

koma munthu wanzeru zomvetsa zinthu amakhala chete.

13Amene amanka nachita ukazitape amawulula zinsinsi;

koma munthu wokhulupirika amasunga pakamwa pake.

14Pakasoweka uphungu mtundu wa anthu umagwa;

koma pakakhala aphungu ambiri pamakhalanso chipulumutso.

15Woperekera mlendo chikole adzapeza mavuto,

koma wodana ndi za chikole amakhala pa mtendere.

16Mkazi wodekha amalandira ulemu,

koma amuna ankhanza amangopata chuma.

17Munthu wachifundo amadzipindulira zabwino

koma munthu wankhanza amadzibweretsera mavuto.

18Munthu woyipa amalandira malipiro wopanda phindu,

koma wochita chilungamo amakolola mphotho yeniyeni.

19Munthu wochita za chilungamo amapeza moyo,

koma wothamangira zoyipa adzafa.

20Yehova amanyansidwa ndi anthu a mtima wokhotakhota

koma amakondwera ndi anthu a makhalidwe angwiro.

21Zoonadi, anthu oyipa adzalangidwa,

koma anthu olungama adzapulumuka.

22Monga imaonekera mphete yagolide ikakhala pa mphuno ya nkhumba,

ndi momwenso amaonekera mkazi wokongola wamʼkamwa.

23Zokhumba za anthu olungama zimathera pa zabwino zokhazokha,

koma chiyembekezo cha anthu oyipa chimathera mu ukali wa Mulungu.

24Munthu wina amapatsako anzake zinthu mwaufulu nʼkumangolemererabe;

wina amamana chomwe akanatha kupereka, koma kumanka nasawukabe.

25Munthu wopereka mowolowamanja adzalemera;

iye amene amathandiza ena iyenso adzathandizidwa.

26Anthu amatemberera womana anzake chakudya,

koma madalitso amakhala pamutu pa munthu amene amagulitsa chakudyacho.

27Iye amene amafunafuna zabwino mwakhama amapeza zabwinozo,

koma wofunafuna zoyipa zidzamupeza.

28Aliyense amene amadalira chuma chake adzafota,

koma wolungama adzaphukira ngati tsamba lobiriwira.

29Wovutitsa a mʼnyumba mwake adzalowa mʼmavuto,

ndipo chitsiru chidzakhala kapolo wa munthu wa nzeru.

30Chipatso cha ntchito zabwino ndi moyo,

ndipo kusatsata malamulo kumawonongetsa moyo.

31Ngati anthu olungama amalandira mphotho zawo pa dziko lapansi,

kuli bwanji anthu osapembedza ndi ochimwa!

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Proverbios 11:1-31

1El Señor aborrece las balanzas adulteradas,

pero aprueba las pesas exactas.

2Con el orgullo viene el oprobio;

con la humildad, la sabiduría.

3A los justos los guía su integridad;

a los falsos los destruye su hipocresía.

4En el día de la ira de nada sirve ser rico,

pero la justicia libra de la muerte.

5La justicia endereza el camino de los íntegros,

pero la maldad hace caer a los impíos.

6La justicia libra a los justos,

pero la codicia atrapa a los falsos.

7Muere el malvado, y con él su esperanza;

muere también su ilusión de poder.

8El justo se salva de la calamidad,

pero la desgracia le sobreviene al malvado.

9Con la boca el impío destruye a su prójimo,

pero los justos se libran por el conocimiento.

10Cuando el justo prospera, la ciudad se alegra;

cuando el malvado perece, hay gran regocijo.

11La bendición de los justos enaltece a la ciudad,

pero la boca de los malvados la destruye.

12El falto de juicio desprecia a su prójimo,

pero el entendido refrena su lengua.

13La gente chismosa revela los secretos;

quien es de fiar es discreto.

14Sin dirección, la nación fracasa;

el éxito depende de los muchos consejeros.

15El fiador de un extraño saldrá perjudicado;

negarse a dar fianza11:15 a dar fianza. Lit. a estrechar la mano. es vivir en paz.

16La mujer bondadosa se gana el respeto;

los hombres violentos solo ganan riquezas.

17El que es bondadoso se beneficia a sí mismo;

el que es cruel, a sí mismo se perjudica.

18El malvado obtiene ganancias ilusorias;

el que siembra justicia asegura su ganancia.

19El que es justo obtiene la vida;

el que persigue el mal se encamina a la muerte.

20El Señor aborrece a los de corazón perverso,

pero se complace en los que viven con rectitud.

21Una cosa es segura:11:21 Una cosa es segura. Lit. Mano a mano. Los malvados no quedarán impunes,

pero los justos saldrán bien librados.

22Como argolla de oro en hocico de cerdo

es la mujer bella pero indiscreta.

23Los deseos de los justos terminan bien;

la esperanza de los malvados termina mal.11:23 termina mal (LXX); es ira (TM).

24Unos dan a manos llenas, y reciben más de lo que dan;

otros ni sus deudas pagan, y acaban en la miseria.

25El que es generoso prospera;

el que reanima será reanimado.

26La gente maldice al que acapara el trigo,

pero colma de bendiciones al que gustoso lo vende.

27El que madruga para el bien, halla buena voluntad;

el que anda tras el mal, por el mal será alcanzado.

28El que confía en sus riquezas se marchita,

pero el justo se renueva como el follaje.

29El que perturba su casa no hereda más que el viento,

y el necio termina sirviendo al sabio.

30El fruto de la justicia11:30 de la justicia (LXX); del justo (TM). es árbol de vida,

pero el que arrebata vidas es violento.11:30 violento (LXX); sabio (TM).

31Si los justos reciben su pago aquí en la tierra,

¡cuánto más los impíos y los pecadores!