Miyambo 10 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Miyambo 10:1-32

Miyambo ya Solomoni

1Miyambo ya Solomoni:

Mwana wanzeru amakondweretsa abambo ake,

koma mwana wopusa amamvetsa amayi ake chisoni.

2Chuma chochipeza mwachinyengo sichipindulitsa,

koma chilungamo chimapulumutsa ku imfa.

3Yehova salola kuti munthu wolungama azikhala ndi njala;

koma amalepheretsa zokhumba za anthu oyipa.

4Wochita zinthu mwaulesi amasauka,

koma wogwira ntchito mwakhama amalemera.

5Amene amakolola nthawi yachilimwe ndi mwana wanzeru,

koma amene amangogona nthawi yokolola ndi mwana wochititsa manyazi.

6Madalitso amakhala pa mutu wa munthu wolungama,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamaphimba chiwawa.

7Munthu wolungama anzake adzamukumbukira ngati mdalitso,

koma dzina la munthu woyipa lidzayiwalika.

8Munthu wa mtima wanzeru amasamala malamulo,

koma chitsiru chomangolongolola chidzawonongeka.

9Munthu woyenda mwangwiro amayenda mosatekeseka;

koma amene amayenda njira yokhotakhota adzadziwika.

10Aliyense wotsinzinira maso mwachinyengo amabweretsa mavuto,

koma wodzudzula chitsiru molimba mtima amabweretsa mtendere.

11Pakamwa pa munthu wolungama ndi kasupe wamoyo,

koma pakamwa pa munthu woyipa pamabisa chiwawa.

12Udani umawutsa mikangano,

koma chikondi chimaphimba zolakwa zonse.

13Nzeru imapezeka pa milomo ya munthu wozindikira zinthu,

koma pa msana pa munthu wopanda nzeru sipachoka chikwapu.

14Anzeru amasunga chidziwitso

koma pakamwa pa chitsiru pamatulutsa zowononga.

15Chuma cha munthu wolemera

ndiye chitetezo chake; koma umphawi ndiye chiwonongeko cha osauka.

16Moyo ndiye malipiro a munthu wolungama,

koma phindu la anthu oyipa ndi uchimo ndi imfa.

17Wosamalira malangizo amayenda mʼnjira ya moyo,

koma wonyoza chidzudzulo amasochera.

18Amene amabisa chidani chake ndi munthu wonama,

ndipo amene amafalitsa miseche ndi chitsiru.

19Mawu akachuluka zolakwa sizisowa,

koma amene amasunga pakamwa pake ndi wanzeru.

20Mawu a munthu wolungama ali ngati siliva wabwino kwambiri,

koma mtima wa munthu woyipa ndi wopanda phindu.

21Milomo ya anthu olungama imalimbikitsa ambiri;

koma chitsiru chimafa chifukwa chosowa nzeru.

22Mdalitso wa Yehova ndiwo umabweretsa chuma,

ntchito za munthu siziwonjezerapo kanthu.

23Kwa chitsiru kuchita zinthu zoyipa ndiye chinthu chomusangalatsa,

koma kwa munthu womvetsa bwino zinthu nzeru ndiyo imamusangalatsa.

24Chimene munthu woyipa amachiopa chidzamuchitikira;

chimene munthu wolungama amachilakalaka adzachipeza.

25Pamene namondwe wawomba, anthu oyipa amachotsedwa,

koma anthu olungama amakhazikika mpaka muyaya.

26Momwe amakhalira vinyo wosasa mʼkamwa ndi momwe umakhalira utsi mʼmaso,

ndi momwenso amakhalira munthu waulesi kwa amene amutuma.

27Kuopa Yehova kumatalikitsa moyo;

koma zaka za anthu oyipa zidzafupikitsidwa.

28Chiyembekezo cha olungama chimapatsa chimwemwe,

koma chiyembekezo cha anthu ochimwa chidzafera mʼmazira.

29Njira za Yehova ndi linga loteteza anthu ochita zabwino,

koma wochita zoyipa adzawonongeka.

30Munthu wolungama sadzachotsedwa, pamalo pake

koma oyipa sadzakhazikika pa dziko.

31Pakamwa pa munthu wolungama pamatulutsa za nzeru,

koma lilime lokhota lidzadulidwa.

32Milomo ya anthu olungama imadziwa zoyenera kuyankhula,

koma pakamwa pa anthu ochimwa pamatulutsa zokhota zokhazokha.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Proverbios 10:1-32

Proverbios de Salomón

1Proverbios de Salomón:

El hijo sabio es la alegría de su padre;

el hijo necio es el pesar de su madre.

2Las riquezas mal adquiridas no sirven de nada,

pero la justicia libra de la muerte.

3El Señor no deja sin comer al justo,

pero frustra la avidez de los malvados.

4Las manos ociosas conducen a la pobreza;

las manos hábiles atraen riquezas.

5El hijo prevenido se abastece en el verano,

pero el sinvergüenza duerme en tiempo de cosecha.

6El justo se ve coronado de bendiciones,

pero la boca del malvado encubre violencia.

7La memoria de los justos es una bendición,

pero la fama de los malvados será pasto de los gusanos.

8El de sabio corazón acata las órdenes,

pero el necio y rezongón va camino al desastre.

9Quien se conduce con integridad anda seguro;

quien anda en malos pasos será descubierto.

10Quien guiña el ojo con malicia provoca pesar;

el necio y rezongón va camino al desastre.

11Fuente de vida es la boca del justo,

pero la boca del malvado encubre violencia.

12El odio es motivo de disensiones,

pero el amor cubre todas las faltas.

13En los labios del prudente hay sabiduría;

en la espalda del falto de juicio, solo garrotazos.

14El que es sabio atesora el conocimiento,

pero la boca del necio es un peligro inminente.

15La riqueza del rico es su baluarte;

la pobreza del pobre es su ruina.

16El salario del justo es la vida;

la ganancia del malvado es el pecado.

17El que atiende a la corrección va camino a la vida;

el que la rechaza se pierde.

18El de labios mentirosos disimula su odio,

y el que propaga calumnias es un necio.

19El que mucho habla mucho yerra;

el que es sabio refrena su lengua.

20Plata refinada es la lengua del justo;

el corazón del malvado no vale nada.

21Los labios del justo orientan a muchos;

los necios mueren por falta de juicio.

22La bendición del Señor trae riquezas,

y nada se gana con preocuparse.

23El necio se divierte con su mala conducta,

pero el sabio se recrea con la sabiduría.

24Lo que el malvado teme, eso le ocurre;

lo que el justo desea, eso recibe.

25Pasa la tormenta y desaparece el malvado,

pero el justo permanece firme para siempre.

26Como vinagre a los dientes y humo a los ojos

es el perezoso para quienes lo emplean.

27El temor del Señor prolonga la vida,

pero los años del malvado se acortan.

28El futuro de los justos es halagüeño;

la esperanza de los malvados se desvanece.

29El camino del Señor es refugio de los justos

y ruina de los malhechores.

30Los justos no tropezarán jamás;

los malvados no habitarán la tierra.

31La boca del justo profiere sabiduría,

pero la lengua perversa será cercenada.

32Los labios del justo destilan10:32 destilan (LXX); saben (TM). bondad;

de la boca del malvado brota perversidad.