Mika 6 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 6:1-16

Mlandu wa Yehova ndi Israeli

1Tamverani zimene Yehova akunena:

“Nyamukani, fotokozani mlandu wanu pamaso pa mapiri;

zitunda zimve zimene inu muti muyankhule.

2Imvani mlandu wa Yehova, inu mapiri;

tamverani, maziko amuyaya a dziko lapansi.

Pakuti Yehova ali ndi mlandu ndi anthu ake;

Iye akutsutsa Aisraeli.

3“Anthu anga, kodi ndakuchitirani chiyani?

Kodi ndakutopetsani bwanji? Ndiyankheni.

4Ine ndinakutulutsani ku dziko la Igupto

ndi kukuwombolani ku nyumba ya ukapolo.

Ndinatuma Mose kuti akutsogolereni,

pamodzi ndi Aaroni ndi Miriamu.

5Anthu anga, kumbukirani

zimene Balaki mfumu ya ku Mowabu inafuna kukuchitirani

ndiponso zimene Balaamu mwana wa Beori anayankha.

Kumbukirani zomwe zinachitika pa ulendo wochoka ku Sitimu kupita ku Giligala,

kuti mudziwe machitidwe olungama a Yehova.”

6Kodi ndidzatenga chiyani kupita nacho pamaso pa Yehova

ndi kukagwada pamaso pa Mulungu wakumwamba?

Kodi ndidzabwera pamaso pake ndi nsembe yopsereza,

ndi ana angʼombe a chaka chimodzi?

7Kodi Yehova adzakondwera ndi nkhosa zazimuna 1,000,

kapena ndi mitsinje yosalekeza ya mafuta?

Kodi ndipereke nsembe mwana wanga woyamba kubadwa chifukwa cha zolakwa zanga?

Chipatso cha thupi langa chifukwa cha tchimo la moyo wanga?

8Munthu iwe, Yehova wakuonetsa kale chimene chili chabwino.

Tsono kodi Yehova akuyembekezera chiyani kwa iwe?

Uzichita zolungama ndi kukonda chifundo

ndiponso kuyenda modzichepetsa pamaso pa Mulungu wako.

Kulakwa kwa Israeli ndi Chilango chake

9Tamverani! Yehova akuyitana anthu okhala mu mzinda

ndi nzeru kuopa dzina lanu.

“Mverani mfumu ndi Iye amene anayikhazikitsa.

10Inu anthu oyipa, kodi Ine nʼkuyiwala

chuma chanu chimene munachipeza mwachinyengo,

ndiponso muyeso wanu woperewera umene ndi wotembereredwa?

11Kodi ndimutenge ngati wosalakwa munthu amene ali ndi sikelo yachinyengo,

ndiponso miyeso yabodza mʼthumba lake?

12Anthu ake olemera amachita zachiwawa;

anthu ake ndi abodza

ndipo pakamwa pawo pamayankhula zachinyengo.

13Choncho, ndayamba kukuwonongani,

kukusakazani chifukwa cha machimo anu.

14Mudzadya, koma simudzakhuta;

mudzakhalabe ndi njala.

Mudzasunga zinthu, koma sizidzasungika,

chifukwa zimene mudzasunga zidzawonongedwa ndi lupanga.

15Mudzadzala, koma simudzakolola.

Mudzayenga mafuta a olivi, koma simudzawagwiritsa ntchito.

Mudzaponda mphesa, koma simudzamwa vinyo wake.

16Inu mwatsatira malangizo a Omuri

ndiponso machitidwe onse a banja la Ahabu,

ndi khalidwe lawo lonse.

Choncho Ine ndidzakuperekani kuti muwonongedwe

ndiponso anthu anu kuti azunguzike mitu;

mudzanyozedwa ndi anthu a mitundu ina.”

New Serbian Translation

Књига пророка Михеја 6:1-16

Господња парница против Израиља

1Чујте сада шта говори Господ:

„Устани, са горама се парничи.

Глас твој нека чују брда.

2О, брда и чврсти темељи земљини,

чујте Господњи случај!

Јер, Господ се суди са својим народом

и са Израиљем се спори.

3Шта сам ти урадио, народе мој?

Чиме сам ти дојадио, одговори ми?

4Па ја сам те извео из египатске земље,

из куће ропства сам те откупио

и пред тобом послао Мојсија,

Арона и Марију.

5Сети се, молим те, народе мој,

шта је наумио моавски цар Валак

и шта му је говорио Валам, син Веоров,

шта се збило од Ситима до Галгала,

да бисте схватили Господњу праведност.“

6Како ћу Господу да приступим,

савијен ничице пред узвишеним Богом?

Да му приступим са свеспалницама

и теладима од годину дана?

7Хоће ли Господ бити задовољан са хиљадама овнова,

са десетином хиљада потока уља?

Да ли да првенца дам за своје преступе,

плод утробе своје за грех душе моје?

8Објавио ти је Господ, о, човече, шта је добро

и шта тражи од тебе:

само да чиниш правду, волиш милосрђе

и покорно ходаш са својим Богом.

Кривица и казна Израиља

9Глас Господњи виче граду

и ко је мудар бојаће се имена твога.

„Слушајте жезло моћи и онога ко га је овластио!6,9 Овај део стиха може и овако да се преведе: Слушај, племе (Јудино)! Ко је онај што га је установио (град)?

10Има ли у кући непоштеног још увек непоштеног блага

и проклете непоштене мере?

11Зар ћу да будем чист са непоштеним теразијама

и са торбом нетачних тегова?

12Јер су њихови богаташи пуни насиља,

његови становници говоре превару,

лажљив им је језик у устима.

13И још ћу те разболети ударајући те,

због греха ћу те пустошити.

14Јешћеш, а сит нећеш бити.

Бићеш празан у нутрини својој.

Склањаћеш, а нећеш осигурати.

А ја ћу мач послати на оно што си осигурао.

15Сејаћеш, али нећеш жети,

газићеш маслине и грожђе,

али се уљем нећеш мазати и вино нећеш пити.

16Држиш Амријеве уредбе

и сва дела Ахавовог дома.

Идеш по њиховим саветима

и зато сам те предао разарању,

а твој живаљ ће поднети ругло

и погрду мог народа.“