Mika 5 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 5:1-15

Wolamulira Wochokera ku Betelehemu

1Iwe mzinda wa anthu ankhondo, sonkhanitsa anthu ako ankhondo,

pakuti anthu atizungulira kuti alimbane nafe.

Adzakantha ndi ndodo pa chibwano

cha wolamulira wa Israeli.

2“Koma iwe Betelehemu Efurata,

ngakhale uli wonyozeka pakati pa mafuko a Yuda,

mwa iwe mudzatuluka

munthu amene adzalamulira Israeli,

amene chiyambi chake nʼchakalekale,

nʼchamasiku amakedzana.”

3Nʼchifukwa chake Israeli adzasiyidwa

mpaka pa nthawi imene mayi amene ali woyembekezera adzachire.

Ndipo abale ake onse otsalira adzabwerera

kudzakhala pamodzi ndi Aisraeli.

4Iye adzalimbika, ndipo adzaweta nkhosa zake

mwa mphamvu ya Yehova,

mu ulemerero wa dzina la Yehova Mulungu wake.

Ndipo iwo adzakhala mu mtendere,

pakuti ukulu wake udzakhala ponseponse pa dziko lapansi.

5Ndipo Iye adzakhala mtendere wawo.

Chipulumutso ndi Chiwonongeko

Asiriya akadzalowa mʼdziko lathu

ndi kuyamba kuthira nkhondo malo athu otetezedwa,

tidzawadzutsira abusa asanu ndi awiri,

ngakhalenso atsogoleri asanu ndi atatu.

6Iwo adzagonjetsa dziko la Asiriya ndi lupanga,

dziko la Nimurodi adzalilamulira mwankhondo.

Adzatipulumutsa kwa Asiriya

akadzafika mʼmalire a mʼdziko lathu

kudzatithira nkhondo.

7Otsalira a Yakobo adzakhala

pakati pa mitundu yambiri ya anthu

ngati mame ochokera kwa Yehova,

ngati mvumbi pa udzu,

omwe sulamulidwa ndi munthu

kapena kudikira lamulo la anthu.

8Otsala a Yakobo adzakhala pakati pa mitundu ya anthu,

mʼgulu la anthu a mitundu yambiri,

ngati mkango pakati pa nyama za mʼnkhalango.

Ngati mwana wa mkango pakati pa gulu la nkhosa,

amene pozidutsa amazidya ndi kuzikhadzula,

ndipo palibe angathe kuzilanditsa.

9Mudzagonjetsa adani anu,

ndipo adani anu onse adzawonongeka.

10Yehova akuti,

“Tsiku limenelo ndidzawononga akavalo anu onse

ndi kuphwasula magaleta anu.

11Ndidzawononga mizinda ya mʼdziko mwanu

ndi kugwetsa malinga anu onse.

12Ndidzawononga ufiti wanu

ndipo sikudzakhalanso anthu owombeza mawula.

13Ndidzawononga mafano anu osema

pamodzi ndi miyala yanu yopatulika imene ili pakati panu;

simudzagwadiranso zinthu zopanga

ndi manja anu.

14Ndidzazula mitengo ya mafano a Asera imene ili pakati panu,

ndipo ndidzawononga mizinda yanu.

15Ndidzayilanga mwaukali ndi mokwiya

mitundu imene sinandimvere Ine.”

Luganda Contemporary Bible

Mikka 5:1-15

Omufuzi ava mu Besirekemu

15:1 Kgb 3:30Kuŋŋaanya amaggye go, ggwe ekibuga ekirina amaggye,

kubanga tulumbiddwa.

Omukulembeze wa Isirayiri

balimukuba omuggo ku luba.

25:2 a Yk 7:42 b Lub 48:7 c Zab 102:25 d Mat 2:6*“Naye ggwe Besirekemu Efulasa,

newaakubadde ng’oli mutono mu bika bya Yuda,

mu ggwe mwe muliva alibeera

omufuzi wange mu Isirayiri.

Oyo yaliwo okuva edda n’edda,

ng’ensi tennabaawo.”

3Mukama kyaliva awaayo Isirayiri eri abalabe baayo

okutuusa omukyala alumwa okuzaala lwalizaala omwana,

era baganda be abaasigalawo ne balyoka bakomawo

eri bannaabwe mu Isirayiri.

45:4 a Is 40:11; 49:9; Ez 34:11-15, 23; Mi 7:14 b Is 52:13; Luk 1:32Aliyimirira n’anyweera n’aliisa ekisibo kye

mu maanyi ga Mukama,

mu kitiibwa ky’erinnya lya Mukama Katonda we.

Era abantu be tebalibaako abateganya, kubanga aliba mukulu

okutuusa ku nkomerero y’ensi.

55:5 a Is 9:6; Luk 2:14; Bak 1:19-20 b Is 8:7 c Is 10:24-27Omukulu oyo aliba mirembe gyabwe.

Omwasuli bw’alirumba ensi yaffe

n’abuna ebigo byaffe,

tulimuyimbulira abasumba musanvu,

n’abakulembeze munaana.

65:6 a Lub 10:8 b Zef 2:13 c Nak 2:11-13Abo be balifuga ensi ya Asuli n’ekitala

era ensi ya Nimuloodi nayo bagyonoone.

Naye alitulokola eri Omwasuli

bw’alitulumba mu nsi yaffe

era bw’aliyingira mu nsalo zaffe.

75:7 a Mi 2:12 b Is 44:4Abantu ba Isirayiri abalisigalawo balibeera

wakati mu mawanga agabeetoolodde,

babe ng’omusulo oguva eri Mukama,

ng’obukubakuba obutonnyeredde ku muddo

obutalindirira muntu

oba abaana b’abantu.

85:8 a Lub 49:9 b Mi 4:13; Zek 10:5 c Zab 50:22; Kos 5:14Ng’empologoma bw’ebeera n’ensolo endala ez’omu nsiko,

abantu abaasigalawo aba Yakobo balibeera mu mawanga mangi agabeetoolodde;

ate era ng’empologoma ento mu bisibo by’endiga,

bw’egenda n’eyitamu n’etaagulataagula

ne wataba n’omu aziwonya.

95:9 Zab 10:12Omukono gwo guliwangula abalabe bo,

ne bonna abakuyigganya balizikirizibwa.

105:10 Kos 14:3; Zek 9:10“Ku lunaku olwo,” bw’ayogera Mukama,

“Ndizikiriza embalaasi zo

ne nsanyaawo n’amagaali go.

115:11 a Is 6:11 b Kos 10:14; Am 5:9Ndizikiriza ebibuga eby’omu nsi yo

era mmenyemenye n’ebigo byo byonna.

125:12 Ma 18:10-12; Is 2:6; 8:19Obulogo bwo ndibumalawo

era toliddayo kukolima nate.

135:13 Ez 6:9; Zek 13:2N’ebibumbe bye musinza ndibizikiriza.

Ne nziggyawo n’amayinja ge mwawonga;

temuliddayo nate kuvuunamira bakatonda

be mwekoledde n’emikono gyammwe.

145:14 Kuv 34:13Era ndisigula Baasera okuva mu mmwe,

ebibuga byammwe n’embizikiriza.

155:15 Is 65:12Era ndyesasuza ku mawanga agataŋŋondedde

n’obusungu n’ekiruyi.”