Mika 4 – CCL & LCB

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 4:1-13

Phiri la Yehova

1Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse.

Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.

2Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

3Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

4Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa

ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu,

ndipo palibe amene adzawachititse mantha,

pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.

5Mitundu yonse ya anthu

itha kutsatira milungu yawo;

ife tidzayenda mʼnjira za Yehova

Mulungu wathu mpaka muyaya.

Cholinga cha Yehova

6“Tsiku limenelo, Yehova akuti,

“ndidzasonkhanitsa olumala;

ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa

ndiponso amene ndinawalanga.

7Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala.

Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.

Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova

kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.

8Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga,

iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni,

ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe;

ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”

9Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula,

kodi ulibe mfumu?

Kodi phungu wako wawonongedwa,

kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?

10Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,

ngati mayi pa nthawi yake yobereka,

pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda

ndi kugona kunja kwa mzindawo.

Udzapita ku Babuloni;

kumeneko udzapulumutsidwa,

kumeneko Yehova adzakuwombola

mʼmanja mwa adani ako.

11Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu

yasonkhana kulimbana nawe.

Iwo akuti, “Tiyeni timudetse,

maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”

12Koma iwo sakudziwa

maganizo a Yehova;

iwo sakuzindikira cholinga chake,

Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.

13“Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo;

ndidzakupatsa ziboda zamkuwa

ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.”

Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova,

chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.

Luganda Contemporary Bible

Mikka 4:1-13

Obufuzi bwa Mukama eri Amawanga Gonna

14:1 a Zek 8:3 b Ez 17:22 c Zab 22:27; 86:9; Yer 3:17Mu nnaku ez’oluvannyuma

olusozi lw’ennyumba ya Mukama luligulumizibwa

okusinga ensozi zonna;

lulisitulibwa waggulu okusukkuluma ku busozi,

era abantu balisimba ennyiriri nga balaga gye luli.

24:2 a Yer 31:6 b Zek 2:11; 14:16 c Zab 25:8-9; Is 54:13Amawanga mangi galiragayo ne googera nti,

“Mujje twambuke ku lusozi lwa Mukama,

mu nnyumba ya Katonda wa Yakobo.

Alituyigiriza by’ayagala

tulyoke tutambulire mu makubo ge.”

Alisinziira mu Sayuuni okuwa abantu etteeka lye,

n’ekigambo kya Mukama kiriva mu Yerusaalemi.

34:3 a Is 11:4 b Yo 3:10 c Is 2:4Aliramula amawanga

atereeze ensonga wakati w’amawanga gakirimaanyi ag’ewala.

Baliddira ebitala byabwe ne babiweesaamu enkumbi,

n’amafumu gaabwe ne bagaweesaamu ebiwabyo.

Eggwanga teririyimusa kitala ku ggwanga linnaalyo,

so tebalyetegeka kulwana ntalo nate.

44:4 a 1Bk 4:25 b Lv 26:6 c Is 1:20; Zek 3:10Buli muntu aliba mu ddembe wansi w’omuzabbibu gwe

ne mu mutiini gwe.

Tewalibaawo abatiisa

kubanga akamwa ka Mukama Ayinzabyonna ke kakyogedde.

54:5 a 2Bk 17:29 b Yos 24:14-15; Is 26:8; Zek 10:12Newaakubadde nga amawanga gonna

galigoberera bakatonda baago,

naye ffe tunaatambuliranga mu linnya lya Mukama

Katonda waffe emirembe n’emirembe.

Isirayiri ewona Obusibe

64:6 a Zab 147:2 b Ez 34:13, 16; 37:21; Zef 3:19“Ku lunaku olwo,” bw’ayogera Mukama,

“Ndikuŋŋaanya abalema,

n’abo abaawaŋŋangusibwa

n’abo abali mu nnaku.

74:7 a Mi 2:12 b Dan 7:14; Luk 1:33; Kub 11:15Abalema ndibafuula abalonde,

n’abo be nagoba, mbafuule eggwanga ery’amaanyi.

Mukama alibafugira mu Lusozi Sayuuni

okuva ku lunaku olwo okutuusa emirembe gyonna.

84:8 Is 1:26Ggwe omunaala oguyimirirwamu okulabirira endiga,

ggwe ekigo eky’amaanyi ekya Muwala wa Sayuuni,

ekitiibwa kyo eky’edda kirikuddira,

n’obwakabaka ne bukomawo eri Muwala wa Sayuuni.”

94:9 a Yer 8:19 b Yer 30:6Naye kaakano kiki ekibakaabya ennyo bwe mutyo?

Temulina kabaka abakulembera?

Omuwi w’amagezi wammwe yafa,

ennaku eryoke ebakwate ng’omukazi alumwa okuzaala?

104:10 a 2Bk 20:18; Is 43:14 b Is 48:20Lumwa, weenyoole ggwe Omuwala wa Sayuuni

ng’omukazi alumwa okuzaala.

Kubanga kaakano oteekwa okuva mu kibuga

ogende obeere ku ttale.

Mulitwalibwa mu buwaŋŋanguse mu Babulooni,

era eyo gye ndibalokolera.

Ndibanunulira eyo

okuva mu mukono gw’omulabe.

114:11 Kgb 2:16; Ob 12Kyokka kaakano amawanga mangi

gakuŋŋaanye okubalwanyisa.

Boogera nti, Ayonoonebwe,

n’amaaso gaffe geelolere Sayuuni.

124:12 Is 55:8; Bar 11:33-34Naye tebamanyi

birowoozo bya Mukama;

tebategeera kuteesa kwe;

oyo akuŋŋaanya abalabe be ng’ebinywa by’eŋŋaano bwe bikuŋŋaanyizibwa mu gguuliro.

134:13 Dan 2:44“Golokoka otandike okusa ggwe Omuwala wa Sayuuni,

kubanga ejjembe lyo ndirifuula ekyuma;

ndikuwa ebigere eby’ekyuma eky’ekikomo

era olibetenta amawanga mangi.”

Amagoba gaabwe n’ebintu byabwe bye bafunye mu makubo amakyamu olibiwaayo eri Mukama,

n’obugagga bwabwe n’obuwaayo eri Mukama w’ensi zonna.