Mika 4 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mika 4:1-13

Phiri la Yehova

1Mʼmasiku otsiriza,

phiri la Nyumba ya Yehova adzalikhazikitsa

kukhala lalitali kuposa mapiri ena onse.

Lidzaonekera pamwamba pa mapiri ena onse,

ndipo anthu amitundu yonse adzathamangira kumeneko.

2Mayiko ambiri adzabwera ndikunena kuti,

“Tiyeni, tikwere ku phiri la Yehova,

ku nyumba ya Mulungu wa Yakobo.

Iye adzatiphunzitsa njira zake,

ndipo tidzayenda mʼnjira zakezo.”

Malangizo adzachokera ku Ziyoni,

mawu a Yehova adzachokera ku Yerusalemu.

3Iye adzaweruza pakati pa anthu amitundu yambiri

ndipo adzathetsa kusamvana pakati pa anthu amphamvu akutali ndi apafupi omwe.

Anthuwo adzasandutsa malupanga awo kukhala makasu

ndiponso mikondo yawo kukhala zomwetera.

Mtundu wina sudzatenganso lupanga kumenyana ndi mtundu wina,

kapena kuphunziranso za nkhondo.

4Munthu aliyense adzakhala pansi pa tsinde pa mtengo wake wa mpesa

ndi pa tsinde pa mtengo wake wamkuyu,

ndipo palibe amene adzawachititse mantha,

pakuti Yehova Wamphamvuzonse wayankhula.

5Mitundu yonse ya anthu

itha kutsatira milungu yawo;

ife tidzayenda mʼnjira za Yehova

Mulungu wathu mpaka muyaya.

Cholinga cha Yehova

6“Tsiku limenelo, Yehova akuti,

“ndidzasonkhanitsa olumala;

ndidzasonkhanitsa pamodzi anthu ochotsedwa

ndiponso amene ndinawalanga.

7Anthu olumalawo ndidzawasandutsa anthu anga otsala.

Anthu amene ndinawachotsa ndidzawasandutsa mtundu wamphamvu.

Yehova adzawalamulira mʼPhiri la Yehova

kuyambira tsiku limenelo mpaka muyaya.

8Kunena za iwe, nsanja ya ziweto zanga,

iwe linga la mwana wamkazi wa Ziyoni,

ulamuliro wako wakale udzabwezeretsedwa kwa iwe;

ufumu udzabwera pa mwana wamkazi wa Yerusalemu.”

9Chifukwa chiyani tsopano ukulira mofuwula,

kodi ulibe mfumu?

Kodi phungu wako wawonongedwa,

kotero kuti ululu wako uli ngati wa mayi amene akubereka?

10Gubuduka ndi ululu, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,

ngati mayi pa nthawi yake yobereka,

pakuti tsopano muyenera kuchoka mu mzinda

ndi kugona kunja kwa mzindawo.

Udzapita ku Babuloni;

kumeneko udzapulumutsidwa,

kumeneko Yehova adzakuwombola

mʼmanja mwa adani ako.

11Koma tsopano mitundu yambiri ya anthu

yasonkhana kulimbana nawe.

Iwo akuti, “Tiyeni timudetse,

maso athu aone chiwonongeko cha Ziyoni!”

12Koma iwo sakudziwa

maganizo a Yehova;

iwo sakuzindikira cholinga chake,

Iye amene amawatuta ngati mitolo ya tirigu ku malo opunthira tirigu.

13“Imirira, puntha, iwe mwana wamkazi wa Ziyoni,

pakuti ndidzakupatsa nyanga zachitsulo;

ndidzakupatsa ziboda zamkuwa

ndipo udzaphwanya mitundu yambiri ya anthu.”

Phindu lawo lolipeza molakwikalo udzalipereka kwa Yehova,

chuma chawo kwa Yehova wa dziko lonse lapansi.

New Russian Translation

Михей 4:1-13

Гора Господня

(Ис. 2:2-4)

1В последние дни

гора дома Господня станет

высочайшею среди гор;

вознесется она над холмами,

и устремятся к ней народы.

2Многие народы пойдут и скажут:

«Идем, поднимемся на Господню гору,

к дому Бога Иакова.

Он научит нас Своим путям,

и мы будем ходить по Его тропам».

Ведь из Сиона выйдет Закон,

и слово Господне – из Иерусалима.

3Он рассудит меж многими народами,

разрешит тяжбы сильных племен в далеких краях.

Перекуют они мечи на плуги

и копья – на серпы.

Не поднимет народ на народ меча,

и не будут больше учиться войне.

4Каждый будет сидеть под своей виноградной лозой

и под своим инжиром,

и некого им будет бояться,

потому что так сказал Господь Сил.

5Пусть все народы живут во имя своих богов,

а мы будем ходить во имя Господа,

нашего Бога, во веки и веки.

Божий замысел

6– В тот день, – возвещает Господь, –

Я созову хромых,

Я соберу изгнанников

с теми, кого заставил горевать.

7Я сделаю хромых уцелевшими,

а изгнанников – сильным народом.

Господь будет править ими с горы Сион,

с того дня и вовек.

8Что до тебя, башня стада, холм дочери Сиона,

к тебе возвратится прежняя власть;

царская власть придет к дочери Иерусалима.

9Что же ты теперь заходишься криком,

разве нет у тебя царя?

Разве погиб твой советник,

что муки схватили тебя, точно женщину при родах?

10Мечись и стони, дочь Сиона,

как женщина при родах,

ведь теперь ты покинешь город

и в поле разобьешь лагерь.

Ты уйдешь в Вавилон;

там ты будешь избавлена,

там Господь тебя выкупит

из рук твоих врагов.

11А сейчас много народов

против тебя собралось.

Говорят: «Пусть будет она осквернена!

Пусть наши глаза увидят несчастье Сиона!»

12Но они не знают Господних мыслей,

не понимают Его замысла,

что собрал Он их, как снопы на гумно.

13– Поднимайся и молоти, дочь Сиона;

Я сделаю рог твой железным,

бронзовыми – копыта4:13 Здесь Израиль представлен в образе молотящего вола; его рога и копыта – это символ силы и могущества: рога – чтобы пронзить врагов, копыта – чтобы «сокрушить» многие народы.,

и сокрушишь ты много народов.

Господу посвятишь4:13 Так в некоторых древних переводах; букв.: «Я посвящу». На языке оригинала стоит слово, которое говорит о полном посвящении предметов или людей Господу, часто осуществлявшемся через их уничтожение. их имущество,

их богатства – Владыке всей земли.