Yona 1 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yona 1:1-17

Yona Athawa Yehova

1Yehova anayankhula ndi Yona mwana wa Amitai kuti, 2“Nyamuka, pita ku mzinda waukulu wa Ninive ndipo ukalalikire motsutsana nawo, chifukwa zoyipa zawo zafika pamaso panga.”

3Koma Yona anathawa Yehova ndi kulowera ku Tarisisi. Anapita ku Yopa, kumene anapeza sitima yapamadzi yopita ku Tarisisi. Atagula chiphaso, anakwera sitimayo kupita ku Tarisisi kuthawa Yehova.

4Koma Yehova anatumiza chimphepo champhamvu pa nyanja, ndipo panauka namondwe wamphamvu amene anafuna kuphwanya sitimayo.

5Onse oyendetsa sitimayo anachita mantha ndipo aliyense anayamba kupemphera kwa mulungu wake. Ndipo anaponya katundu mʼnyanja kuti sitimayo ipepuke. Koma Yona pa nthawiyi nʼkuti atatsikira mʼkatikati mwa sitimayo kumene anagona tulo tofa nato. 6Mkulu wa oyendetsa sitimayo anapita kwa iye ndipo anati, “Kodi iwe, nʼchifukwa chiyani ukugona? Dzuka pemphera kwa mulungu wako! Mwina adzatithandiza, ndipo sitidzawonongeka.”

7Ndipo oyendetsa sitimayo anayamba kuwuzana kuti, “Bwerani, tichite maere kuti tipeze amene wabweretsa tsoka limeneli.” Iwo anachita maerewo ndipo anagwera Yona.

8Tsono anamufunsa kuti, “Tatiwuze, tsoka limeneli latigwera chifukwa chiyani? Umagwira ntchito yanji? Ukuchokera kuti? Kwanu nʼkuti? Ndiwe mtundu wanji wa anthu?”

9Iye anayankha kuti, “Ndine Mhebri, ndipo ndimapembedza Yehova, Mulungu Wakumwamba, amene analenga nyanja ndi mtunda.”

10Izi zinawachititsa mantha kwambiri ndipo anafunsa kuti, “Kodi wachita chiyani?” (Iwo ankadziwa kuti iyeyo amathawa Yehova, chifukwa nʼkuti atawawuza kale).

11Namondwe ananka nakulirakulirabe pa nyanjapo. Tsono anamufunsa iye kuti, “Kodi tikuchite chiyani kuti nyanjayi ikhale bata?”

12Iye anayankha kuti, “Nyamuleni ndi kundiponya mʼnyanjamu ndipo nyanjayi ikhala bata. Ndikudziwa kuti wolakwa ndine nʼchifukwa chake chimphepo champhamvuchi chabwera pa inu.”

13Komabe oyendetsa sitimayo anayesetsa kupalasa kwambiri kuti abwerere ku mtunda koma analephera ndithu poti nyanja inawinduka kwambiri kuposa poyamba paja 14Pamenepo iwo anafuwulira kwa Yehova nati, “Inu Yehova, musalole kuti ife tife chifukwa cha moyo wa munthu uyu. Musatizenge mlandu wa kupha munthu wosalakwa, pakuti ife tachita monga mwakufuna kwanu, Inu Yehova.” 15Ndipo anatenga Yona namuponya mʼnyanja, ndipo nyanja yowindukayo inakhala bata. 16Anthuwo ataona zimenezi anachita mantha akulu ndi Yehova, ndipo anapereka nsembe kwa Yehova nalumbira kuti adzatumikira Yehovayo.

17Koma Yehova anatuma nsomba yayikulu kuti imeze Yona. Motero Yona anakhala mʼmimba mwa nsombayo masiku atatu, usana ndi usiku.

New Russian Translation

Иона 1:1-16

Иона бежит от Господа

1К Ионе, сыну Амиттая, было слово Господне:

2– Собирайся, ступай в великий город Ниневию и проповедуй там, потому что его злодеяния дошли до Меня.

3Но Иона собрался бежать от Господа в Таршиш1:3 Таршиш – возможно это финикийская колония в Испании (по представлениям древних евреев чуть ли не край земли). Другими словами, Иона бежал в противоположную сторону от Ниневии.. Он отправился в Яффу, нашел уходящий в Таршиш корабль и, заплатив за проезд, сел на него, чтобы уплыть с ними от Господа.

4Но Господь навел на море страшный ветер, и поднялся такой сильный шторм, что корабль был готов разбиться. 5Все моряки перепугались, и каждый принялся взывать к своему богу. Они побросали в море всю кладь, какая была на корабле, чтобы облегчить его.

А Иона спустился в трюм, лег там и уснул крепким сном. 6Капитан пришел к нему и сказал:

– Что ты спишь? Вставай, воззови к своему Богу! Может быть, Он позаботится о нас, и мы не погибнем.

7Моряки говорили друг другу:

– Давайте кинем жребий и узнаем, за кого нам эта беда.

Они бросили жребий, и жребий пал на Иону.

8Тогда они спросили его:

– Скажи нам, кто виновник этой беды? Каково твое ремесло? Откуда ты держишь путь? Из какой ты страны? Из какого народа?

9Он ответил:

– Я еврей и поклоняюсь Господу, Богу небес, Который создал море и сушу.

10Они очень перепугались и спросили:

– Что же ты наделал?

(Они знали, что он бежит от Господа: он уже рассказал им об этом.)

11А море бушевало все сильнее и сильнее, и тогда они спросили его:

– Что нам сделать с тобой, чтобы море утихло перед нами?

12– Возьмите меня и бросьте в море, – ответил он, – и оно утихнет перед вами. Я знаю, что этот страшный шторм обрушился на вас из-за меня.

13Однако они принялись грести изо всех сил, чтобы пристать к берегу, но им это не удавалось, потому что море бушевало еще сильнее. 14Тогда они стали призывать Господа:

– Господи, не дай нам погибнуть за жизнь этого человека. Не взыскивай с нас за убийство невинного, ведь Ты, Господь, делаешь то, что угодно Тебе.

15Потом они взяли Иону, бросили его за борт, и бушевавшее море утихло. 16Моряки ужасно испугались Господа, принесли Господу жертву и дали обеты.