Mateyu 9 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 9:1-38

Munthu Wakufa Ziwalo wa ku Kaperenawo

1Yesu analowa mʼbwato nawoloka, ndipo anabwera ku mudzi wa kwawo. 2Amuna ena anabwera ndi munthu wakufa ziwalo kwa Iye atamugoneka pa mphasa. Yesu ataona chikhulupiriro chawo anati kwa wakufa ziwaloyo, “Limba mtima mwana wanga, machimo ako akhululukidwa.”

3Pamenepo aphunzitsi ena amalamulo anaganiza mu mtima mwawo kuti, “Munthu uyu akuchitira Mulungu mwano.”

4Ndipo podziwa maganizo awo Yesu anati, “Bwanji mukuganiza zoyipa mʼmitima mwanu? 5Chapafupi ndi chiti kunena kuti, ‘Machimo ako akhululukidwa’ kapena kunena kuti, ‘Imirira ndipo yenda?’ 6Tsono kuti mudziwe kuti Mwana wa Munthu ali ndi ulamuliro pa dziko wokhululuka machimo, pamenepo anati kwa wakufa ziwaloyo, ‘Imirira, tenga mphasa yako kazipita kwanu.’ ” 7Ndipo munthuyo anayimirira napita kwawo. 8Gulu la anthu litaona izi, linadzazidwa ndi mantha ndipo linalemekeza Mulungu amene anapereka ulamuliro kwa anthu.

Kuyitanidwa kwa Mateyu

9Ndipo Yesu atachoka kumeneko, anaona munthu wina dzina lake Mateyu, atakhala mʼnyumba ya msonkho. Anati kwa iye, “Nditsate Ine.” Ndipo iye ananyamuka namutsata.

10Ndipo pamene Iye ankadya mʼnyumba, onani, amisonkho ndi ochimwa ambiri anabwera nakhala pansi pamodzi ndi Yesu ndi ophunzira ake. 11Ndipo Afarisi poona izi, anati kwa ophunzira ake, “Nʼchifukwa chiyani Aphunzitsi anu akudya pamodzi ndi amisonkho ndi ochimwa?”

12Yesu atamva, anati, “Munthu wamoyo safuna singʼanga ayi, koma wodwala. 13Koma pitani kaphunzireni tanthauzo la mawu awa: ‘Ndimafuna chifundo osati nsembe ayi.’ Pakuti sindinabwere kudzayitana olungama koma ochimwa.”

Za Kusala Kudya

14Ndipo ophunzira a Yohane anabwera namufunsa Iye kuti, “Bwanji ife ndi Afarisi timasala kudya koma ophunzira anu sasala kudya?”

15Yesu anayankha kuti, “Kodi oyitanidwa ku ukwati angamalire bwanji pamene mkwati ali naye pamodzi? Nthawi idzafika pamene mkwatiyo adzachotsedwa ndi pamene adzasala kudya.”

16Ndipo palibe munthu amasokerera chigamba chatsopano pa chovala chakale chifukwa chigambacho chidzachoka ndipo chibowocho chidzakula kuposa kale. 17Kapena sathira vinyo watsopano mʼmatumba akale; akatero, matumba akalewo adzaphulika ndipo vinyoyo adzatayika, matumbawo adzawonongeka; satero ayi. Amathira vinyo watsopano mʼmatumba atsopanonso ndipo zonse zimasungika.

Za Mwana Wamkazi wa Yairo ndi Mayi Wokhudza Chovala cha Yesu

18Pamene ankanena zimenezi, mkulu wa sunagoge anabwera namugwadira Iye nati, “Mwana wanga wamkazi wamwalira posachedwapa koma tiyeni mukasanjike dzanja lanu pa iye ndipo adzakhala ndi moyo.” 19Yesu ndi ophunzira ake ananyamuka napita naye pamodzi.

20Panali mayi wina amene ankadwala nthenda yotaya magazi kwa zaka khumi ndi ziwiri ndipo anadza mʼmbuyo mwake nakhudza mkanjo wake. 21Iyeyo anati mwa iye yekha, “Nditangokhudza kasonga ka mkanjo wake, ine ndidzachiritsidwa.”

22Ndipo Yesu anatembenuka namuona mayiyo nati, “Limbani mtima mayi iwe, chikhulupiriro chako chakuchiritsa.” Nthawi yomweyo mayiyo anachiritsidwa.

23Yesu atalowa mʼnyumba ya mkulu wa sunagoge ndi kuona oyimba zitoliro ndi gulu la anthu ochita phokoso, 24anati, “Tulukani, mtsikanayu sanafe koma ali mtulo.” Koma anamuseka Iye. 25Atangowatulutsa anthuwo, analowa mʼnyumba ndipo anagwira dzanja la mtsikanayo ndipo anauka. 26Mbiriyi inamveka mʼdera lonse.

Yesu Achiritsa Osaona ndi Osayankhula

27Yesu atapitirira ulendo wake, amuna awiri osaona anamutsatira Iye, akufuwula kuti, “Tichitireni chifundo, Mwana wa Davide!”

28Atalowa mʼnyumba, amuna awiri osaonawo anabwera kwa Iye ndipo anawafunsa kuti, “Kodi mukhulupirira kuti ndikhoza kukuchiritsani?”

Iwo anayankha kuti, “Inde Ambuye.”

29Pomwepo anakhudza maso awo nati, “Zichitike kwa inu monga mwachikhulupiriro chanu.” 30Ndipo anayamba kuona. Yesu anawachenjeza kwambiri nati, “Onani, wina aliyense asadziwe za zimenezi.” 31Koma iwo anatuluka mʼnyumbamo nafalitsa za Iye mʼchigawo chonse.

32Pamene iwo ankatuluka kunja, anthu anabwera kwa Iye ndi munthu wogwidwa ndi mzimu wosayankhula. 33Ndipo atatulutsa mzimuwo, munthuyo anayankhula. Gulu la anthuwo linadabwa ndipo linati, “Zinthu zotere sizinaonekepo mu Israeli.”

34Koma Afarisi anati, “Akutulutsa mizimu yoyipa ndi mphamvu ya mkulu wa ziwanda.”

Antchito ndi Ochepa

35Yesu anayendayenda mʼmizinda yonse ndi mʼmidzi, kuphunzitsa mʼmasunagoge awo, nalalikira Uthenga Wabwino wa ufumu ndi kuchiritsa nthenda zawo zonse ndi zofowoka za mʼmatupi mwawo. 36Ataona maguluwo, anagwidwa ndi chisoni chifukwa anali ozunzika ndi osowa chithandizo ngati nkhosa zopanda mʼbusa. 37Pamenepo anati kwa ophunzira ake, “Zokolola ndi zambiri koma antchito ndi ochepa. 38Nʼchifukwa chake, pemphani Ambuye mwini zokolola kuti atumize antchito ku munda wake.”

Słowo Życia

Mateusza 9:1-38

Jezus uzdrawia sparaliżowanego

1Jezus wsiadł więc do łodzi i odpłynął do swojego miasta, Kafarnaum. 2Tam kilku mężczyzn przyniosło do Niego na noszach sparaliżowanego. Widząc ich wiarę, Jezus rzekł do chorego:

—Bądź dobrej myśli, synu. Odpuszczam ci grzechy!

3„To jawne bluźnierstwo!”—z oburzeniem pomyślało sobie kilku przywódców religijnych. 4Jezus, znając ich myśli, zapytał:

—Dlaczego was to oburza? 5Co jest łatwiej powiedzieć: „Odpuszczam ci grzechy” czy: „Wstań i chodź!”? 6Udowodnię wam, że Ja, Syn Człowieczy, mogę odpuszczać grzechy.

I zwrócił się do sparaliżowanego:

—Jesteś uzdrowiony! Zabierz swoje nosze i idź do domu!

7A chory wstał i odszedł do domu. 8Po zebranych przeszedł dreszcz lęku. I wielbili Boga za to, że dał taką moc człowiekowi!

Powołanie Mateusza

9Odchodząc stamtąd, Jezus zobaczył niejakiego Mateusza, poborcę podatkowego, który właśnie tam pracował.

—Chodź ze Mną—zwrócił się do niego.

A on natychmiast wstał i poszedł z Jezusem. 10Później, gdy Jezus i Jego uczniowie byli u niego w domu, zebrało się wokół stołu wielu nieuczciwych poborców podatkowych i innych ludzi, uważanych za grzeszników. 11Widząc to, faryzeusze mówili do uczniów:

—Dlaczego wasz nauczyciel zadaje się z takimi ludźmi?

12Jezus usłyszał to i odpowiedział:

—To chorzy potrzebują lekarza, a nie zdrowi! 13Idźcie i zastanówcie się nad słowami Pisma: „Pragnę waszej miłości, a nie ofiar”. Nie przyszedłem wzywać do opamiętania się tych, którzy uważają się za dobrych, ale właśnie grzeszników.

Pytanie o post

14Pewnego razu przyszli do Jezusa uczniowie Jana Chrzciciela i zapytali Go:

—My i faryzeusze, stosując się do religijnych zaleceń, często powstrzymujemy się od posiłków. Dlaczego Twoi uczniowie tego nie czynią?

15—Przecież goście na weselu, będąc z panem młodym, nie mogą się smucić!—odrzekł Jezus. —Ale nadejdzie czas, gdy zabiorą im pana młodego. Wtedy będą pościć. 16Nikt nie używa nowego materiału do łatania starego ubrania, bo nowa łata się kurczy i jeszcze bardziej rozdziera ubranie. 17Nie wlewa się też świeżego wina do starych, stwardniałych bukłaków. Mogłyby przecież popękać, a wtedy i wino by się rozlało, i bukłaki zniszczyły. Świeże wino wlewa się do nowych, miękkich bukłaków. W ten sposób i jedno, i drugie się zachowuje.

Jezus wskrzesza i uzdrawia

18Gdy jeszcze o tym mówił, podszedł do Niego przełożony miejscowej synagogi. Pokłonił się i powiedział:

—Przed chwilą zmarła moja córeczka. Ale jeśli przyjdziesz i dotkniesz jej, ożyje.

19Jezus wstał i wraz z uczniami poszedł za przełożonym. 20Tymczasem pewna kobieta, od dwunastu lat cierpiąca na krwotok, podeszła do Niego od tyłu i dotknęła Jego ubrania. 21Pomyślała bowiem: „Jeśli tylko dotknę Jego płaszcza, zostanę uzdrowiona”. 22Jezus odwrócił się, dostrzegł ją i rzekł:

—Bądź dobrej myśli, córko! Uwierzyłaś, więc zostałaś uzdrowiona!

I w tej samej chwili kobieta odzyskała zdrowie.

23Gdy przybył do domu przełożonego synagogi, zobaczył żałobników i lamentujący tłum.

24—Odejdźcie stąd—powiedział. —Dziewczynka nie umarła, tylko śpi.

Ale oni śmiali się z Niego. 25W końcu jednak wyproszono tłum. Jezus wszedł do środka, wziął dziewczynkę za rękę, a ona natychmiast wstała! 26Wieść o tym obiegła całą okolicę.

Jezus uzdrawia niewidomych

27Jezus właśnie stamtąd odchodził, gdy zjawili się dwaj niewidomi, którzy wołali za Nim:

—Potomku króla Dawida, zmiłuj się nad nami!

28Szli tak za Nim aż do domu, gdzie się zatrzymał. Wtedy podeszli bliżej, a On ich zapytał:

—Wierzycie, że mogę to zrobić?

—Tak, Panie!—odpowiedzieli.

29—Niech będzie tak, jak wierzycie—powiedział Jezus i dotknął ich oczu.

30I nagle przejrzeli! Wówczas On surowo im nakazał:

—Nikomu o tym nie mówcie.

31Ale oni odeszli i zaraz wszędzie o tym opowiedzieli.

Jezus uzdrawia niemowę

32W tym właśnie czasie przyprowadzono do Jezusa kolejnego człowieka—niemowę zniewolonego przez demona. 33Po wypędzeniu demona, człowiek ten zaczął mówić. A tłumy nie mogły wyjść z podziwu:

—Coś takiego nigdy się nie zdarzyło w całym Izraelu!

34—Wypędza demony, bo władca demonów Mu w tym pomaga—twierdzili natomiast faryzeusze.

Niewielu pracowników

35A Jezus odwiedzał wszystkie okoliczne miasta i wioski. Nauczał w synagogach, głosił dobrą nowinę o królestwie i uzdrawiał z każdej choroby i słabości. 36Gdy patrzył na otaczające Go tłumy, ogarniała Go litość. Ludzie byli bowiem udręczeni i zagubieni jak owce bez pasterza.

37—Żniwo jest wielkie—mówił uczniom—a tak mało pracujących! 38Proście więc gospodarza, aby posłał więcej pracowników na żniwa.