Mateyu 10 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 10:1-42

Yesu Atuma Ophunzira Ake

1Yesu anayitana ophunzira ake khumi ndi awiri ndipo anawapatsa ulamuliro otulutsa mizimu yoyipa ndi kuchiritsa nthenda iliyonse ndi zofowoka zilizonse.

2Mayina a atumwi khumi ndi awiriwo ndi awa: woyamba, Simoni (wotchedwa Petro) ndi mʼbale wake Andreya; Yakobo mwana wa Zebedayo ndi mʼbale wake Yohane, 3Filipo ndi Bartumeyu, Tomasi ndi Mateyu wolandira msonkho, Yakobo mwana wa Alufeyo ndi Tadeyo; 4Simoni Mzerote ndi Yudasi Isikarioti, amene anamupereka Iye.

5Yesu anatuma khumi ndi awiriwo ndi kuwalamula kuti, “Musapite kwa anthu a mitundu ina kapena kulowa mʼmudzi uliwonse wa Asamariya. 6Koma pitani kwa nkhosa zotayika za banja la Israeli. 7Pamene mukupita, muzikalalikira uthenga uwu: ‘Ufumu wakumwamba wayandikira.’ 8Chiritsani odwala, ukitsani akufa, chiritsani akhate, tulutsani ziwanda. Munalandira kwaulere, perekani kwaulere.

9“Musatenge ndalama zagolide kapena zasiliva kapena zakopala mʼzikwama mwanu; 10musatenge thumba la paulendo, kapena malaya awiri kapena nsapato kapena ndodo; pakuti wantchito ayenera kulandira chakudya chake. 11Mukalowa mu mzinda ndi mʼmudzi uliwonse, funafunani munthu woyenera ndipo mukhale mʼnyumba mwake kufikira mutachoka. 12Pamene mulowa mʼnyumba mupereke moni. 13Mtendere wanu ukhale pa a mʼnyumbayo ngati ndi oyenera. Koma ngati siwoyenera, mtendere wanu ubwerere kwa inu. 14Ngati wina aliyense sakakulandirani kapena sakamvera mawu anu, musase fumbi la kumapazi anu pamene mutuluka mʼnyumbayo kapena mu mzindawo. 15Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti pa tsiku lachiweruziro, mlandu wa Sodomu ndi Gomora udzachepa kusiyana ndi wa mzindawo.

16“Taonani ndikukutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu. Chifukwa chake khalani ochenjera ngati njoka ndi woona mtima ngati nkhunda. 17Chenjerani ndi anthu pakuti adzakuperekani ku mabwalo amilandu nadzakukwapulani mʼmasunagoge mwawo. 18Chifukwa cha Ine, mudzaperekedwa kwa olamulira ndi kwa mafumu kuti mukhale mboni kwa iwo ndi kwa a mitundu ina. 19Koma pamene akumangani, inu musadandaule kuti mukanena bwanji kapena mukanena chiyani. Mudzapatsidwa pa nthawi imeneyo zoti munene, 20pakuti sindinu mudzanena, koma Mzimu Woyera wa Atate anu, adzayankhula mwa inu.

21“Mʼbale adzapereka mʼbale kuti aphedwe ndi abambo mwana wawo: ndipo ana adzawukira makolo awo ndi kuwapereka kuti aphedwe. 22Anthu onse adzada inu chifukwa cha Ine, koma iye amene apirira mpaka kumapeto, adzapulumuka. 23Pamene akuzunzani pamalo ena thawirani kwina. Pakuti ndikuwuzani zoonadi kuti simudzamaliza mizinda yonse ya Israeli Mwana wa Munthu asanabwere.

24“Wophunzira saposa mphunzitsi wake ndipo wantchito saposa bwana wake. 25Nʼkoyenera kuti wophunzira akhale ngati mphunzitsi wake, ndi wantchito akhale ngati bwana wake. Ngati mwini banja atchedwa Belezebabu, koposa kotani a mʼnyumba mwake!

26“Chifukwa chake musaope iwo. Pakuti palibe chinthu chobisika chimene sichidzavundukulidwa, ndi chobisika chimene sichidzadziwika. 27Chimene ndikuwuzani Ine mu mdima, muchiyankhule poyera; chimene akunongʼonezani mʼkhutu, muchilalikire muli pa denga. 28Musamaope amene amapha thupi koma sangathe kuchotsa moyo. Koma muziopa Iye amene akhoza kupha mzimu ndi kuwononga thupi mu gehena. 29Kodi suja amagulitsa mbalame ziwiri ndi ndalama imodzi? Koma palibe imodzi ya izo imene idzagwa pansi wopanda chifuniro cha Atate anu. 30Ndipo ngakhale tsitsi la mʼmutu mwanu linawerengedwa kale. 31Potero musaope; inu ndinu a mtengo woposa mbalame zambiri.

32“Aliyense amene avomereza Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzavomereza pamaso pa Atate anga akumwamba. 33Koma iye amene andikana Ine pamaso pa anthu, Inenso ndidzamukana pamaso pa Atate anga akumwamba.

34“Musaganize kuti Ine ndabweretsa mtendere pa dziko lapansi. Sindinabwere kudzapereka mtendere koma lupanga. 35Pakuti Ine ndabwera kudzalekanitsa

“ ‘Munthu ndi abambo ake,

mwana wamkazi ndi amayi ake,

mtengwa kulekanitsidwa ndi apongozi ake,

36adani a munthu adzakhala a mʼbanja mwake momwe.’

37“Aliyense amene akonda abambo kapena amayi ake koposa Ine sayenera kukhala wanga; aliyense amene akonda mwana wake wamwamuna kapena wamkazi koposa Ine sayenera kukhala wanga. 38Aliyense amene satenga mtanda wake ndi kunditsata Ine sayenera kukhala wanga. 39Aliyense amene asunga moyo wake adzawutaya koma aliyense amene ataya moyo chifukwa cha Ine adzawupeza.

40“Iye amene alandira inu alandira Ine, ndipo amene alandira Ine alandiranso amene anandituma Ine. 41Aliyense amene alandira mneneri chifukwa chakuti ndi mneneri alandira mphotho ya mneneri, ndipo aliyense amene alandira munthu wolungama chifukwa chakuti ndi munthu wolungama, adzalandira mphotho ya wolungama. 42Ngati aliyense apereka madzi ozizira a mʼchikho kwa mmodzi wa angʼonoangʼono awa chifukwa cha kuti ndi ophunzira anga, ndikuwuzani zoona, ndithudi sadzataya mphotho yake.”

Słowo Życia

Mateusza 10:1-42

Jezus posyła Dwunastu

1Pewnego dnia Jezus przywołał dwunastu uczniów i dał im władzę uwalniania ludzi od złych duchów i uzdrawiania wszelkich chorób i dolegliwości. 2Byli to: Szymon (zwany też Piotrem) i Andrzej—jego brat, Jakub i Jan—synowie Zebedeusza, 3Filip, Bartłomiej, Tomasz, Mateusz (poborca podatkowy), Jakub—syn Alfeusza, Tadeusz, 4Szymon Gorliwy i Judasz z Kariotu—ten, który później wydał Jezusa.

5Tych dwunastu uczniów Jezus posłał, dając im następujące wskazówki:

—Nie chodźcie do pogan ani do miast Samarii. 6Idźcie jedynie do Izraelitów, którzy jak zagubione owce odeszli od Boga. 7Mówcie im: „Nadchodzi królestwo niebieskie!”. 8Uzdrawiajcie chorych, wskrzeszajcie zmarłych, leczcie trędowatych i uwalniajcie od demonów. Róbcie to za darmo, bo za darmo to otrzymaliście! 9Nie bierzcie ze sobą pieniędzy, 10torby z zapasową odzieżą i obuwiem ani laski podróżnej. Ten bowiem, kto pracuje, powinien otrzymać to, co mu się należy. 11Wchodząc do jakiegoś miasta lub wsi, dowiedzcie się, kto tam jest godnym człowiekiem. Pozostańcie u niego aż do opuszczenia tej miejscowości. 12Wchodząc do jego domu, pozdrówcie tych, którzy w nim mieszkają. 13Jeśli to pobożni ludzie, Bóg obdarzy ich pokojem. Jeśli nie—pokój pozostanie z wami. 14Jeśli nie zostaniecie przyjęci i nie będą chcieli was słuchać, odchodząc z tego domu i miasta, strząśnijcie z nóg nawet tamtejszy kurz. 15Zapewniam was: W dniu sądu złym mieszkańcom Sodomy i Gomory lżej będzie niż temu miastu.

16Posyłam was jak owce między wilki. Bądźcie więc sprytni jak węże, ale nieskazitelni jak gołębie. 17Uważajcie na siebie! Postawią was przed sądami, będą was biczować w synagogach 18oraz oskarżać przed władzami za to, że Mnie naśladujecie. Będzie to dla was okazja do przedstawienia im dobrej nowiny. W ten sposób dotrze ona do wielu narodów. 19Nie martwcie się jednak, co i jak macie mówić. We właściwym czasie otrzymacie stosowne słowa. 20Bo to nie wy będziecie mówić, lecz Duch waszego Ojca będzie mówił przez was! 21Bracia będą wzajemnie się wydawać na śmierć, ojcowie zdradzą własne dzieci, a dzieci—rodziców. 22Wszyscy was znienawidzą za to, że należycie do Mnie. Ale ci, którzy wytrwają do końca i nie zaprą się Mnie, zostaną uratowani! 23Gdy spotka was prześladowanie w jednym mieście, uciekajcie do drugiego! Zapewniam was: Nie zdążycie obejść wszystkich miast Izraela, a Ja, Syn Człowieczy powrócę.

Ostrzeżenia

24Uczeń nie przewyższa nauczyciela, a sługa—swego pana. 25Wystarczy, że będą jak ich nauczyciel lub pan. Skoro Mnie, pana domu, nazwano Belzebubem, władcą demonów, to tym bardziej spotka to domowników. 26Ale nie bójcie się ich! Nie ma bowiem niczego ukrytego, co by ostatecznie nie wyszło na jaw. 27To, co teraz mówię wam pod osłoną nocy, rozpowiadajcie z nastaniem dnia. To, co słyszycie na ucho, rozgłaszajcie publicznie! 28Nie bójcie się tych, którzy uśmiercają ciało, lecz nie mogą zabić duszy! Lękajcie się Boga, który i duszę, i ciało może zatracić w piekle. 29Ile kosztuje para wróbli? Można ją kupić już za kilka drobnych monet. A jednak żaden z nich nie spadnie na ziemię bez wiedzy waszego Ojca w niebie. 30Przecież On wie nawet ile macie włosów na głowie! 31Nie bójcie się więc! Jesteście dla Niego cenniejsi niż całe stado wróbli!

32Jeśli więc jakiś człowiek wyzna przed innymi ludźmi, że należy do Mnie, to i Ja przyznam się do Niego przed moim Ojcem w niebie. 33Lecz jeśli ktoś wyprze się Mnie wobec ludzi, i Ja się go wyprę przed moim Ojcem w niebie.

34Nie myślcie, że przyszedłem przynieść na ziemię pokój! Wręcz przeciwnie—miecz podziału! 35Przyszedłem poróżnić syna z ojcem, córkę—z matką, a synową—z teściową. 36Nawet najbliżsi staną się wrogami! 37Kto kocha ojca lub matkę bardziej niż Mnie, nie jesteś Mnie godny. I kto kocha syna lub córkę bardziej niż Mnie, nie jest Mnie godny. 38Kto nie bierze swojego krzyża i nie idzie ze Mną, nie jest Mnie godny. 39Kto zabiega o swoje życie, utraci je. Lecz ten, kto poświęci życie dla Mnie, odnajdzie je.

40Kto was przyjmuje, Mnie przyjmuje. A kto Mnie przyjmuje, przyjmuje Ojca, który Mnie posłał. 41Kto przyjmuje proroka—dlatego, że jest on prorokiem—otrzyma nagrodę należną prorokowi. Kto przyjmuje prawego człowieka—dlatego, że jest on prawy—otrzyma nagrodę należną prawemu człowiekowi. 42Nawet jeśli ktoś poda kubek wody najmniejszemu z moich uczniów—właśnie dlatego, że jest on moim uczniem—zapewniam was: nie ominie go nagroda!