Mateyu 7 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 7:1-29

Za Kuweruza Ena

1“Musaweruze ena, kuti inunso mungadzaweruzidwe. 2Pakuti momwe inu muweruzira ena, inunso mudzaweruzidwa chimodzimodzi, muyeso umene muyesera ena inunso mudzayesedwa ndi womwewo.

3“Chifukwa chiyani iwe uyangʼana kachitsotso ka mʼdiso la mʼbale wako koma susamalira chimtengo chili mʼdiso mwako? 4Kodi unganene bwanji kwa mʼbale wako kuti, ‘Ndikuchotse kachitsotso mʼdiso mwako,’ pamene nthawi zonse chimtengo uli nacho mʼdiso mwako? 5Wachiphamaso iwe! Yamba wachotsa chimtengo chili mʼdiso mwako ndipo pamenepo udzatha kuona bwino ndi kuchotsa kachitsotso kali mʼdiso mwa mʼbale wako.

6“Musapatse agalu zinthu zopatulika; kapena musaponyere nkhumba ngale zanu. Pakuti ngati mutero, zidzaziponda ndipo pomwepo zidzakutembenukirani ndi kukudulani nthulinthuli.

Pemphani, Funafunani, Gogodani

7“Pemphani ndipo mudzapatsidwa; funafunani ndipo mudzapeza; gogodani ndipo adzakutsekulirani. 8Pakuti wopempha aliyense amalandira; ndi wofuna amapeza; ndipo iye amene agogoda, adzamutsekulira.

9“Ndani mwa inu, mwana wake akamupempha buledi amamupatsa mwala? 10Kapena ngati mwana apempha nsomba, kodi amamupatsa njoka? 11Tsono ngati inu woyipitsitsa mumadziwa kupatsa ana anu mphatso zabwino, nanga Atate anu akumwamba sadzapereka mphatso zabwino kwa iwo amene amupempha? 12Nʼchifukwa chake zinthu zilizonse mukafuna kuti anthu akuchitireni, yambani ndinu kuwachitira, pakuti izi ndi zimene malamulo ndi aneneri amaphunzitsa.

Zipata Ziwiri ndi Njira Ziwiri

13“Lowani pa chipata chopapatiza. Pakuti chipata cholowera kuchiwonongeko nʼchachikulu ndipo msewu wake ndi waukulunso. Ndipo anthu ambiri amalowera pamenepo. 14Koma chipata ndi chopapatiza ndi msewu ndi waungʼono umene utsogolera anthu ku moyo wosatha ndipo ndi owerengeka okha amene ayipeza njirayo.

Aneneri Owona ndi Onyenga

15“Chenjerani nawo aneneri onyenga. Amabwera kwa inu atavala zikopa zankhosa, koma mʼkati mwawo ali mimbulu yolusa. 16Mudzawazindikira iwo ndi zipatso zawo. Kodi anthu amathyola mpesa pa mtengo wa minga, kapena nkhuyu pa nthula? 17Chimodzimodzinso mtengo wabwino umabala chipatso chabwino, koma mtengo woyipa umabala chipatso choyipa. 18Mtengo wabwino sungabale chipatso choyipa, ndi mtengo woyipa sungabale chipatso chabwino. 19Mtengo uliwonse umene subala chipatso chabwino umadulidwa ndi kuponyedwa pa moto. 20Momwemonso, ndi zipatso zawo iwo mudzawazindikira.

Ophunzira Owona ndi Onyenga

21“Si munthu aliyense amene amanena kwa Ine, ‘Ambuye, Ambuye,’ adzalowe mu ufumu wakumwamba, koma ndi yekhayo amene amachita chifuniro cha Atate anga amene ali kumwamba. 22Ambiri adzati kwa Ine pa tsikulo, ‘Ambuye, Ambuye, kodi sitinkanenera mʼdzina lanu ndi mʼdzina lanunso tinkatulutsa ziwanda ndi kuchita zodabwitsa zambiri?’ 23Pamenepo ndidzawawuza momveka bwino kuti, ‘Sindinakudziweni inu. Chokani kwa Ine, inu ochita zoyipa!’

Womanga Nyumba Wanzeru ndi Wopusa

24“Nʼchifukwa chake aliyense amene amva mawu anga ndi kuwachita akufanana ndi munthu wanzeru amene anamanga nyumba yake pa thanthwe. 25Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo; koma sinagwe, chifukwa maziko ake anali pa thanthwe. 26Koma aliyense amene amva mawu angawa ndi kusawachita ali ngati munthu wopusa amene anamanga nyumba yake pa mchenga. 27Mvula inagwa, mitsinje inadzaza, ndi mphepo zinawomba pa nyumbayo, ndipo inagwa ndipo kugwa kwake kunali kwakukulu.”

28Yesu atamaliza kunena zonsezi, magulu a anthu anadabwa ndi chiphunzitso chake, 29chifukwa anaphunzitsa ngati amene anali ndi ulamuliro osati ngati aphunzitsi amalamulo.

Священное Писание

Матай 7:1-29

Об осуждении других

(Лк. 6:37-38, 41-42)

1– Не судите, чтобы и вас не судили. 2Так же, как вы судите других, будут судить и вас, и какой мерой вы мерите, такой будет отмерено и вам. 3Что ты смотришь на сучок в глазу своего брата, когда в своём собственном не замечаешь бревна? 4Как ты можешь говорить своему брату: «Дай я выну сучок из твоего глаза», когда в твоём собственном глазу бревно? 5Лицемер, вынь сначала бревно из собственного глаза, а потом ты увидишь, как вынуть сучок из глаза своего брата. 6Того, что свято, не давайте псам, а не то они, обернувшись, растерзают вас. И не разбрасывайте своих драгоценностей перед свиньями, не то они растопчут их.

О настойчивости

(Лк. 11:9-13; 6:31)

7– Просите – и вам дадут, ищите – и найдёте, стучите – и вам откроют. 8Потому что каждый, кто просит, получает, и кто ищет, находит, и тому, кто стучит, откроют. 9Есть ли среди вас такой человек, который даст своему сыну камень, когда тот просит хлеба? 10И кто даст сыну змею, когда тот попросит рыбы? 11Если вы, будучи злы, умеете давать своим детям благие дары, то тем более Небесный Отец даст благое тем, кто просит у Него! 12Поэтому во всём поступайте с людьми так, как хотите, чтобы они поступали с вами. В этом суть всего, что написано в Таурате и в Книге Пророков.

О пути на небеса

(Лк. 13:24)

13– Входите через узкие ворота. Путь, ведущий к погибели, широк, ворота просторны, и многие идут по этому пути. 14Но тесны ворота и узок путь, ведущие к жизни, и лишь немногие находят их.

О хороших и плохих плодах

(Лк. 6:43-44)

15– Берегитесь лжепророков. Они приходят к вам в овечьих шкурах, внутри же они – хищные волки. 16Их вы узнаете по их плодам. Собирают ли с терновника виноград или с чертополоха инжир? 17Здоровое дерево приносит хороший плод, а больное дерево и плод приносит негодный. 18На здоровом дереве не бывает плохих плодов, и на больном дереве не бывает хороших. 19Каждое дерево, не приносящее хороших плодов, срубают и бросают в огонь. 20Итак, вы узнаете их по плодам.

21Не всякий, кто говорит Мне: «Повелитель, Повелитель», войдёт в Небесное Царство, но лишь тот, кто исполняет волю Моего Небесного Отца. 22Многие будут говорить Мне в тот день: «Повелитель, Повелитель, да разве мы не пророчествовали от Твоего имени, разве не изгоняли Твоим именем демонов и не совершали многих чудес?» 23Но Я отвечу им: «Я никогда не знал вас, прочь от Меня, беззаконники!»7:23 См. Заб. 6:9.

Притча о мудром и глупом строителях

(Лк. 6:47-49)

24– Того, кто слушает эти Мои слова и исполняет их, можно сравнить с мудрым человеком, построившим свой дом на камне. 25Пошёл дождь, разлились реки, подули ветры и обрушились на этот дом, но он устоял, потому что был построен на камне. 26А всякого, кто слушает Мои слова, но не исполняет их, можно сравнить с глупцом, построившим свой дом на песке. 27Пошёл дождь, разлились реки, подули ветры и обрушились на этот дом; и он рухнул, и падение его было ужасным.

28Когда Иса закончил говорить, народ изумлялся Его учению, 29потому что Он учил их как имеющий власть, а не как их учители Таурата.