Mateyu 6 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 6:1-34

Zopereka Zachifundo

1“Samalani kuti musachite ntchito zanu zolungama pamaso pa anthu kuti akuoneni. Popeza ngati mutero simudzalandira mphotho yochokera kwa Atate anu akumwamba.

2“Pamene mupereka zachifundo, musachite modzionetsera monga amachita achiphamaso mʼmasunagoge ndi pa misewu kuti atamidwe ndi anthu. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwowo alandiriratu mphotho yawo yonse. 3Koma pamene mupereka zachifundo, dzanja lanu lamanzere lisadziwe chimene dzanja lanu lamanja likuchita, 4kotero kuti kupereka kwanu kukhale mwachinsinsi. Ndipo Atate anu amene amaona zochitika mwachinsinsi, adzakupatsani mphotho.

Za Kupemphera

5“Pamene mupemphera, musakhale ngati achiphamaso, chifukwa iwo amakonda kupemphera choyimirira mʼmasunagoge ndi pa mphambano za mʼmisewu kuti anthu awaone. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse. 6Koma pamene mupemphera, lowani mʼchipinda chanu chamʼkati, ndi kutseka chitseko ndipo mupemphere kwa Atate anu amene saoneka. Ndipo Atate anu, amene amaona zochitika mseri, adzakupatsani mphotho. 7Ndipo pamene mukupemphera, musamabwerezabwereza monga akunja, pakuti iwo amaganiza kuti adzamveka chifukwa chochulutsa mawu. 8Musakhale ngati iwo chifukwa Atate anu amadziwa zimene musowa musanapemphe.

9“Chifukwa chake pempherani motere:

“ ‘Atate athu akumwamba,

dzina lanu lilemekezedwe,

10Ufumu wanu ubwere,

chifuniro chanu chichitike

pansi pano monga kumwamba.

11Mutipatse chakudya chathu chalero.

12Mutikhululukire mangawa athu,

monga ifenso tawakhululukira amangawa athu.

13Ndipo musatitengere kokatiyesa;

koma mutipulumutse kwa woyipayo.’

14Ngati inu mukhululukira anthu pamene akuchimwirani, Atate anu akumwamba adzakukhululukirani. 15Koma ngati inu simukhululukira anthu zolakwa zawo, Atate anunso sadzakukhululukirani machimo anu.

Kusala Kudya

16“Pamene mukusala kudya, musaonetse nkhope yachisoni monga achita achiphamaso, pakuti iwo amasintha nkhope zawo kuonetsa anthu kuti akusala kudya. Zoonadi, Ine ndikuwuzani kuti iwo alandiriratu mphotho yawo yonse. 17Koma pamene ukusala kudya, samba mʼmaso nudzole mafuta kumutu, 18kuti usaonekere kwa anthu kuti ukusala kudya koma kwa Atate ako ali mseri; ndipo Atate ako amene amaona za mseri adzakupatsa mphotho.

Za Chuma cha Kumwamba

19“Musadziwunjikire chuma pa dziko lapansi, pamene njenjete ndi dzimbiri zimawononga ndi pamene mbala zimathyola ndi kuba. 20Koma mudziwunjikire chuma kumwamba kumene njenjete ndi dzimbiri siziwononga ndipo mbala sizithyola ndi kuba. 21Pakuti kumene kuli chuma chako, mtima wako udzakhala komweko.

Diso Nyale ya Thupi

22“Diso ndi nyale ya thupi. Ngati maso ako ali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mʼkuwala. 23Koma ngati maso ako sali bwino, thupi lako lonse lidzakhala mu mdima. Koma ngati kuwala kuli mwa iwe ndi mdima, ndiye kuti mdimawo ndi waukulu bwanji!

24“Palibe munthu angathe kukhala kapolo wa ambuye awiri. Pakuti pena adzamuda mmodzi ndi kukonda winayo kapena adzagwira ntchito mokhulupirika kwa mmodzi, nadzanyoza winayo. Simungathe kukhala kapolo wa Mulungu ndi wa chuma pa nthawi imodzi.

Musade Nkhawa

25“Nʼchifukwa chake ndikuwuzani kuti musadere nkhawa za moyo wanu kuti mudzadya chiyani kapena mudzamwa chiyani; kapenanso za thupi lanu kuti mudzavala chiyani. Kodi moyo suposa chakudya? Kodi thupi siliposa zovala? 26Onani mbalame zamlengalenga sizifesa kapena kukolola kapena kusunga mʼnkhokwe komabe Atate anu akumwamba amazidyetsa. Kodi inu simuziposa kwambiri? 27Kodi ndani wa inu podandaula angathe kuwonjeza ora limodzi pa moyo wake?

28“Ndipo bwanji inu mudera nkhawa za zovala? Onani makulidwe a maluwa akutchire. Sagwira ntchito kapena kuwomba nsalu. 29Ndikukuwuzani kuti angakhale Solomoni mu ulemerero wake sanavale mofanana ndi limodzi la maluwa amenewa. 30Ngati umu ndi mmene Mulungu avekera udzu wa kutchire umene ulipo lero ndipo mawa uponyedwa ku moto, kodi sadzakuvekani koposa? Aa! Inu a chikhulupiriro chochepa! 31Chifukwa chake musadere nkhawa ndi kuti, ‘Tidzadya chiyani?’ kapena ‘Tidzamwa chiyani?’ kapena ‘Tidzavala chiyani?’ 32Pakuti anthu akunja amazifuna zinthu zonsezi ndipo Atate anu akumwamba adziwa kuti musowa zimenezi. 33Koma muyambe mwafuna ufumu wake ndi chilungamo chake ndipo zinthu zonsezi zidzapatsidwa kwa inu. 34Chifukwa chake musadere nkhawa ndi za mawa, popeza tsiku lililonse lili ndi zovuta zake zokwanira.

Słowo Życia

Mateusza 6:1-34

Pomoc potrzebującym

1Uważajcie, by nie być dobrymi tylko na pokaz. Jeśli tak będziecie postępować, nie otrzymacie nagrody od waszego Ojca w niebie. 2Gdy obdarowujesz biednego, nie rozgłaszaj tego, jak to czynią obłudnicy w synagogach i na ulicach, by zyskać poklask u ludzi. Zapewniam was: oni teraz odbierają za to nagrodę. 3Wspierając potrzebującego, czyń to dyskretnie. Niech twoja lewa ręka nie wie, co robi prawa, 4aby twoja pomoc pozostała w ukryciu. A Ojciec twój, który wszystko widzi, nagrodzi cię.

Modlitwa

5Gdy się modlicie, nie zachowujcie się jak obłudnicy. Oni uwielbiają to robić w synagogach i na rogach ulic—na pokaz. Zapewniam was: już teraz odbierają za to nagrodę. 6Ty zaś zamknij się w swoim pokoju i módl się do Ojca, który wszystko widzi—On cię nagrodzi.

7Nie róbcie z modlitwy paplaniny—jak poganie, którzy sądzą, że wysłuchanie ich próśb zależy od ilości wypowiedzianych słów. 8Nie bądźcie do nich podobni! Wasz Ojciec doskonale zna wasze potrzeby, zanim jeszcze Go o coś poprosicie! 9Zwracajcie się do Boga tak:

Nasz Ojcze w niebie,

niech Twoje święte imię będzie uwielbione!

10Niech nadejdzie Twoje królestwo.

Niech Twoja wola wypełnia się

na ziemi tak, jak w niebie.

11Zapewnij nam codzienny pokarm.

12Przebacz nam nasze grzechy,

tak jak my przebaczamy tym,

którzy zawinili wobec nas.

13Nie pozwól, byśmy ulegli pokusie

i wybaw nas od złego.

14Jeśli bowiem wybaczycie innym ich zło, to i wam wybaczy wasz Ojciec w niebie. 15Lecz jeśli nie wybaczycie, i On wam nie wybaczy.

Post

16Gdy powstrzymujecie się od posiłków, nie róbcie tego na pokaz—jak obłudnicy, którzy starają się wyglądać ponuro i mizernie. Zapewniam was: oni już teraz odbierają za to nagrodę. 17Gdy więc pościsz, zadbaj o włosy i umyj twarz, 18by pokazać swój post Ojcu, a nie ludziom. On wszystko widzi i nagrodzi cię.

Skarby w niebie

19Nie gromadźcie bogactw tu, na ziemi, gdzie mogą ulec zniszczeniu lub zostać skradzione przez złodziei. 20Gromadźcie je w niebie—tam nic ich nie zniszczy i nikt się nie włamie, by je ukraść. 21Gdzie jest wasz skarb, tam będzie wasze serce.

22Oko jest dla ciała jak lampa. Jeśli jest zdrowe, światło napełnia całe ciało. 23Jeśli jednak jest chore, całe ciało jest pogrążone w ciemnościach. Jeżeli więc twoje światło jest ciemnością, to jest to ciemność nieprzenikniona.

24Nie da się lojalnie służyć dwóm panom. Albo jednego nienawidzisz, a drugiego kochasz, albo na odwrót—drugiego szanujesz, a pierwszego lekceważysz. Nie możecie równocześnie żyć dla Boga i dla pieniędzy!

Nie martwcie się

25Dlatego radzę wam: Nie martwcie się o swoje życie—o to, co będziecie jeść i pić, ani o ciało—w co się ubierzecie. Czy życie ogranicza się tylko do jedzenia, a ciało—tylko do ubrania? 26Spójrzcie na ptaki: Nie sieją ziarna, nie magazynują zapasów, a wasz Ojciec w niebie żywi je! Czy wy nie jesteście ważniejsi od ptaków? 27Czy ktokolwiek, poprzez zamartwianie się, potrafi przedłużyć swoje życie choćby o jedną chwilę? 28Dlaczego martwicie się o ubranie? Uczcie się od polnych kwiatów: Nie pracują i nie troszczą się o swój ubiór. 29A zapewniam was, że nawet król Salomon, w całym swym przepychu, nie był tak pięknie ubrany jak one. 30Jeśli więc Bóg tak wspaniale ubiera polne kwiaty, które dzisiaj kwitną, a jutro więdną i idą na spalenie, to czy tym bardziej nie zatroszczy się o was, nieufni?! 31Nie martwcie się więc i nie powtarzajcie: Co będziemy jeść i pić? W co się ubierzemy? 32O te sprawy zabiegają poganie. Wasz Ojciec w niebie dobrze wie, że tego potrzebujecie. 33W pierwszej kolejności zabiegajcie o Jego królestwo i prawość, a wtedy Bóg zatroszczy się o pozostałe rzeczy. 34Nie martwcie się więc o to, co będzie jutro, bo dzień jutrzejszy zatroszczy się o siebie. Dziś macie już wystarczająco wiele zmartwień.