Mateyu 5 – CCL & SZ-PL

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 5:1-48

Chiphunzitso cha pa Phiri

1Iye ataona anthu ambiri, anakwera pa phiri nakhala pansi. Ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye, 2ndipo anayamba kuwaphunzitsa kuti,

3“Odala ndi amene ali osauka mu mzimu,

chifukwa ufumu wakumwamba ndi wawo.

4Odala ndi amene ali achisoni,

chifukwa adzatonthozedwa.

5Odala ndi amene ali ofatsa,

chifukwa adzalandira dziko lapansi.

6Odala ndi amene akumva njala ndi ludzu la chilungamo,

chifukwa adzakhutitsidwa.

7Odala ndi amene ali ndi chifundo,

chifukwa adzawachitira chifundo.

8Odala ndi amene ali oyera mtima,

chifukwa adzaona Mulungu.

9Ndi odala amene amabweretsa mtendere,

chifukwa adzatchedwa ana a Mulungu.

10Odala ndi amene akuzunzidwa chifukwa cha chilungamo,

pakuti ufumu wakumwamba ndi wawo.”

11“Inu ndinu odala anthu akamakunyozani, kukuzunzani, kukunenerani zoyipa zilizonse ndi kukunamizirani chifukwa cha Ine. 12Sangalalani, kondwerani chifukwa mphotho yanu ndi yayikulu kumwamba, chifukwa moterenso ndi mmene anazunzira aneneri inu musanabadwe.

Mchere ndi Kuwunika

13“Inu ndinu mchere wa dziko lapansi. Koma ngati mcherewo usukuluka, adzawukometsanso ndi chiyani? Ulibenso ntchito koma kungowutaya kunja, anthu nawuponda.

14“Inu ndinu kuwunika kwa dziko lapansi. Mzinda wa pa phiri sungathe kubisika. 15Anthu sayatsa nyale ndikuyivundikira ndi mbiya, mʼmalo mwake amayika poonekera ndipo imawunikira onse mʼnyumbamo. 16Momwemonso kuwunika kwanu kuwale pamaso pa anthu kuti aone ntchito zanu zabwino ndi kulemekeza Atate anu akumwamba.

Kukwaniritsa Malamulo

17“Musaganize kuti ndinadza kudzathetsa malamulo kapena zonena za aneneri; sindinabwere kudzathetsa koma kukwaniritsa. 18Ine ndikukuwuzani zoonadi kuti, kufikira kutha kwa thambo ndi dziko lapansi, chilichonse chimene chinalembedwa mʼmalamulo, ngakhale kalemba kakangʼonongʼono, chidzakwaniritsidwa. 19Chifukwa chake aliyense amene aphwanya limodzi la malamulowa ngakhale lalingʼonongʼono ndi kuphunzitsa ena kuti achite chimodzimodzi, adzakhala wotsirizira mu ufumu wakumwamba, koma aliyense amene achita ndi kuphunzitsa malamulo awa adzakhala wamkulu mu ufumu wakumwamba. 20Chifukwa chake ndikuwuzani kuti ngati chilungamo chanu sichiposa cha Afarisi ndi aphunzitsi amalamulo, zoonadi, simudzalowa mu ufumu wakumwamba.

Zokhudza Kupha

21“Munamva kuti kunanenedwa kwa anthu kale kuti, ‘Usaphe ndipo kuti aliyense amene apha munthu adzaweruzidwa.’ 22Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense wokwiyira mʼbale wake adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene wonena mʼbale wake kuti, ‘Ndiwe wopanda phindu,’ adzapezeka wolakwa ku bwalo la milandu lalikulu. Ndipo aliyense amene anganene mnzake ‘wopandapake’ adzatengeredwa ku bwalo la milandu. Ndiponso aliyense amene angamunene mnzake kuti, ‘Chitsiru iwe,’ adzaponyedwa ku gehena.

23“Nʼchifukwa chake, pamene ukupereka chopereka chako pa guwa lansembe ndipo nthawi yomweyo ukumbukira kuti mʼbale wako ali nawe chifukwa, 24usiye choperekacho pa guwa lansembepo, choyamba pita kayanjane ndi mʼbale wako; ukatero bwera kudzapereka chopereka chakocho.

25“Fulumira kuyanjana ndi mnzako amene unamulakwira nthawi ya milandu isanafike chifukwa angakupereke kwa oweruza amene angakupereke kwa mlonda ndipo mlondayo angakutsekere mʼndende. 26Zoonadi, Ine ndikukuwuza kuti sudzatuluka mʼndende mpaka utalipira zonse.

Zokhudza Chigololo

27“Munamva kuti kunanenedwa kuti, ‘Usachite chigololo.’ 28Koma Ine ndikuwuzani kuti aliyense woyangʼana mkazi momusirira wachita naye kale chigololo mu mtima mwake. 29Ngati diso lako lakumanja likuchimwitsa, ulichotse ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena. 30Ndipo ngati dzanja lako lamanja likuchimwitsa, ulidule ndi kulitaya. Pakuti nʼkwabwino kwa iwe kutaya chiwalo chimodzi cha thupi lako, kusiyana ndi kuti thupi lonse liponyedwe mʼgehena.

Zokhudza Kusudzula Mkazi

31“Ananena kuti, ‘Aliyense wosudzula mkazi wake ayenera amupatse kalata ya chisudzulo.’ 32Koma Ine ndikukuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake pa chifukwa china chilichonse osati chifukwa cha chiwerewere, akumuchititsa mkaziyo chigololo ndipo aliyense wokwatira mkaziyo, akuchitanso chigololo.

Malonjezo

33“Munamvanso kuti kunanenedwa kwa anthu akale kuti, ‘Musaphwanye lonjezo; koma sungani malonjezo anu amene mwachita kwa Yehova.’ 34Koma ndikuwuzani kuti musalumbire ndi pangʼono pomwe kutchula kumwamba chifukwa kuli mpando waufumu wa Mulungu. 35Kapena kutchula dziko lapansi, chifukwa ndi chopondapo mapazi ake; kapena kutchula Yerusalemu, chifukwa ndi mzinda wa mfumu yayikulu. 36Ndipo musalumbire ndi mutu wanu chifukwa simungathe kuyeretsa ngakhale kudetsa tsitsi limodzi. 37Koma ‘Inde’ wanu akhaledi ‘Inde’ kapena ‘Ayi’ wanu akhaledi ‘Ayi,’ chilichonse choposera apa, chichokera kwa woyipayo.

Za Kubwezera Choyipa

38“Munamva kuti, ‘Diso kulipira diso ndi dzino kulipira dzino.’ 39Koma ndikuwuzani kuti musamukanize munthu woyipa, akakumenya patsaya mupatseni tsaya linalo. 40Ndipo ngati wina afuna kukuzenga mlandu kuti akulande malaya ako, umupatsenso mkanjo wako. 41Ngati wina akukakamiza kuti uyende naye mtunda umodzi, iwe uyende naye mitunda iwiri. 42Wina akakupempha kanthu umupatse, ndipo wofuna kubwereka usamukanize.

Kukonda Adani

43“Munamva kuti, ‘Konda mnansi wako ndi kudana ndi mdani wako.’ 44Koma Ine ndikuwuzani kuti, ‘Kondani adani anu ndi kuwapempherera okuzunzani 45kuti mukhale ana a Atate anu akumwamba, amene awalitsa dzuwa lake pa oyipa ndi pa abwino, nagwetsa mvula pa olungama ndi pa osalungama.’ 46Ngati mukonda amene akukondani inu, mudzapeza mphotho yanji? Kodi ngakhale amisonkho sachita chimodzimodzi? 47Ndipo ngati inu mupatsa moni abale anu okhaokha mukuchita chiyani choposa ena? Kodi ngakhale akunja sachita chimodzimodzi? 48Nʼchifukwa chake, inu khalani angwiro monga Atate anu akumwamba ali wangwiro.”

Słowo Życia

Mateusza 5:1-48

Szczęśliwi

1Pewnego dnia Jezus, widząc gromadzące się wokół Niego tłumy, wszedł na wzgórze i usiadł. 2Uczniowie otoczyli Go, a On zaczął nauczać:

3—Szczęśliwi ubodzy w duchu,

bo do nich należy królestwo niebieskie.

4Szczęśliwi smutni,

bo zostaną pocieszeni.

5Szczęśliwi cisi,

bo odziedziczą całą ziemię.

6Szczęśliwi ci, którzy pragną sprawiedliwości,

bo zostaną nasyceni.

7Szczęśliwi ci, którzy okazują innym miłość,

bo sami zostaną obdarzeni miłością.

8Szczęśliwi ci, którzy mają czyste serce,

bo zobaczą samego Boga.

9Szczęśliwi ci, którzy wprowadzają pokój,

bo zostaną nazwani dziećmi Boga.

10Szczęśliwi prześladowani za prawość,

bo do nich należy królestwo niebieskie.

11Macie ogromne szczęście,

gdy ludzie was znieważają, prześladują

i oczerniają z mojego powodu.

12Cieszcie się i skaczcie z radości,

bo w niebie czeka was wielka nagroda.

Właśnie tak prześladowano kiedyś proroków Boga!

Sól i światło

13Jesteście solą tej ziemi! Lecz jeśli sól utraci swój smak, staje się bezwartościowa. Dlatego wyrzuca się ją na ścieżkę, gdzie zostaje podeptana przez ludzi. 14Jesteście światłem dla świata! Nie można ukryć miasta położonego na wzgórzu. 15Nie zapala się też lampy, aby ją zaraz zasłonić, ale stawia się ją na podwyższeniu, aby świeciła wszystkim, którzy są w domu. 16Wasze światło niech również świeci wszystkim ludziom, aby widzieli wasze dobre postępowanie i oddawali chwałę waszemu Ojcu w niebie.

Wypełnienie Prawa

17Nie myślcie, że przyszedłem znieść Prawo Mojżesza albo pisma proroków. Nie znieść, ale wypełnić! 18Zapewniam was, że prędzej niebo i ziemia przestaną istnieć, niż zmieni się najmniejsza literka w Prawie—zanim wszystko zostanie do końca wypełnione. 19Jeśli więc ktoś usunąłby nawet najmniej ważne przykazanie Prawa i tak nauczał innych, będzie najmniej ważny w królestwie niebieskim. A kto sam wypełnia wszystko i uczy tego innych, będzie wielki w królestwie niebieskim. 20Ostrzegam was więc: jeśli wasza prawość nie będzie większa od prawości faryzeuszy i przywódców religijnych, nie wejdziecie do królestwa niebieskiego.

Zabójstwo

21Słyszeliście, że powiedziano przodkom: „Nie zabijaj”, a kto zabije, pójdzie pod sąd. 22A ja wam mówię: Każdy, kto się na kogoś gniewa, pójdzie pod sąd! A kto nazywa go głupcem, stanie przed Wysoką Radą. A kto nazwałby go idiotą, zasługuje na ogień piekielny. 23Jeśli więc, przynosząc dar na ołtarz w świątyni, przypomniałbyś sobie, że ktoś ci coś zarzuca, 24zostaw swój dar przy ołtarzu i idź się pogodzić z tym człowiekiem. Potem wróć i złóż dar Bogu. 25Póki jest na to czas, staraj się polubownie załatwić sprawę ze swoim oskarżycielem. W przeciwnym bowiem razie sędzia cię skaże i zostaniesz wtrącony do więzienia. 26Zapewniam cię, że nie wyjdziesz stamtąd, aż spłacisz cały dług—co do grosza.

Niewierność małżeńska

27Słyszeliście, że w Prawie Mojżesza powiedziano: „Bądź wierny w małżeństwie”. 28A Ja wam mówię: Kto spogląda na kobietę i pożąda jej, w sercu już się dopuścił niewierności. 29Jeśli więc twoje prawe oko skłania cię do grzechu, wyłup je i odrzuć. Lepiej bowiem, gdy zginie jakaś część twojego ciała, niż byś z całym ciałem miał być wrzucony do piekła. 30I jeśli twoja prawa ręka skłania cię do grzechu, odetnij ją i odrzuć. Lepiej bowiem, gdy zginie jakaś część twojego ciała, niż byś z całym ciałem miał znaleźć się w piekle.

Rozwód

31W Prawie Mojżesza powiedziano też: „Kto chce się rozwieść z żoną, niech jej wręczy dokument rozwodowy”. 32A Ja wam mówię: Kto rozwodzi się z żoną (z wyjątkiem przypadku rozwiązłości seksualnej), naraża ją na grzech niewierności. Kto zaś żeni się z rozwódką, również dopuszcza się grzechu niewierności małżeńskiej.

Przysięga

33Słyszeliście również, że powiedziano przodkom: „Nie przysięgaj fałszywie, lecz dotrzymaj przysięgi danej Panu”. 34A Ja wam mówię: W ogóle nie przysięgajcie: ani na niebo—bo jest tronem Boga; 35ani na ziemię—bo jest Jego podnóżkiem; ani na Jerozolimę—bo jest miastem wielkiego Króla! 36Nawet na własną głowę nie przysięgaj—bo nie możesz jednego włosa uczynić białym lub czarnym. 37Mów prawdę: niech twoje „tak” znaczy „tak”, a „nie” znaczy „nie”. Każde oszustwo pochodzi od szatana.

Oko za oko

38Słyszeliście, że w Prawie Mojżesza powiedziano: „Oko za oko, ząb za ząb”. 39A Ja wam mówię: Nie rewanżujcie się za doznane zło! Jeśli ktoś cię obrazi, uderzając w policzek, nadstaw mu drugi. 40Jeśli ktoś chce się z tobą sądzić o koszulę, daj mu od razu i płaszcz. 41Jeśli ktoś cię zmusza, byś niósł mu bagaż kilometr, nieś mu i dwa. 42Daj temu, kto cię prosi, i nie odwracaj się od tego, kto chce od ciebie coś pożyczyć.

Miłość do wrogów

43Słyszeliście, że powiedziano: „Kochaj przyjaciół, nienawidź wrogów”. 44A Ja wam mówię: Kochajcie waszych wrogów i módlcie się za tych, którzy was prześladują— 45tak postępują dzieci waszego Ojca w niebie. On bowiem sprawia, że słońce wschodzi dla dobrych i dla złych. A deszcz pada dla prawych i dla nieprawych. 46Czy sądzicie, że zasługujecie na nagrodę, bo kochacie tych, którzy was kochają? Czy nawet źli ludzie tak nie postępują? 47Jeśli jesteście mili tylko dla przyjaciół, w czym jesteście lepsi? Czy poganie tak nie postępują? 48Bądźcie więc doskonali, tak jak wasz Ojciec w niebie.