Mateyu 20 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 20:1-34

Fanizo la Aganyu Mʼmunda wa Mphesa

1“Ufumu wakumwamba uli ngati mwini munda amene anapita mmawa kukalemba anthu aganyu kuti akagwire ntchito mʼmunda wake wa mpesa. 2Anagwirizana kuwalipira dinari monga malipiro a tsiku limodzi ndipo anawatumiza mʼmunda wake wamphesa.

3“Nthawi 9 koloko mmawa, anatulukanso naona ena atayimirira pa msika akungokhala. 4Anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa, ndipo ndidzakulipirani malipiro oyenera.’ 5Ndipo anapita.

“Anatulukanso nthawi ya 12 koloko masana, ndi nthawi ya 3 koloko masananso nachita chimodzimodzi. 6Nthawi ya 5 koloko madzulo anatulukanso ndipo anapeza enanso atangoyimirira. Anawafunsa kuti, ‘Chifukwa chiyani mukungoyimirira pano tsiku lonse osagwira ntchito?’

7“Iwo anayankha kuti, ‘Chifukwa palibe munthu amene watilemba ganyu.’

“Iye anawawuza kuti, ‘Inunso pitani mukagwire ntchito mʼmunda wanga wa mpesa.’

8“Ndipo pofika madzulo, mwini munda wamphesa anayitana kapitawo wake nati, ‘Itana antchito ndipo uwapatse malipiro awo, kuyambira omalizira aja mpaka oyamba.’

9“Antchito amene anawalemba ganyu pa 5 koloko masana anafika ndipo aliyense analandira dinari. 10Ndipo atabwera kwa amene analembedwa poyamba anayembekezera kuti alandira zambiri. Koma aliyense wa iwo analandira dinari. 11Atalandira, anayamba kuderera kwa mwini mundayo. 12Iwo anati, ‘Anthu amene munawalemba pomalizira agwira ntchito ora limodzi, ndipo mwawafananitsa ndi ife amene tathyoka nayo ntchito ndi kutentha kwa dzuwa tsiku lonse.’

13“Koma iye anamuyankha mmodzi wa iwo nati, ‘Bwenzi, ine sikuti sindinachite chilungamo. Kodi sunavomereze kuti ugwira ntchito ndi kulandira dinari? 14Tenga malipiro ako pita. Ndikufuna kumupatsa munthu amene ndinamulemba pomaliza mofanana ndi mmene ndakupatsira iwe. 15Kodi ndilibe ufulu wochita zimene ndikufuna ndi ndalama zanga? Kapena ukuyipidwa chifukwa ndine wopereka mowolowamanja?’

16“Momwemo omalizira adzakhala oyamba ndipo oyamba adzakhala omalizira.”

Yesu Anenanso za Imfa Yake

17Tsopano pamene Yesu ankapita ku Yerusalemu, anatengera pambali ophunzira ake khumi ndi awiriwo nati kwa iwo, 18“Tikupita ku Yerusalemu, ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kwa akulu a ansembe ndi aphunzitsi amalamulo. Iwo adzamuweruza kuti aphedwe, 19ndipo adzamupereka kwa anthu a mitundu ina kuti amunyoze ndi kumukwapula ndi kumupachika. Pa tsiku lachitatu adzaukitsidwa!”

Pempho la Mkazi wa Zebedayo

20Amayi a ana a Zebedayo anabwera ndi ana ake kwa Yesu, nagwada pansi namupempha Iye.

21Yesu anawafunsa kuti, “Mukufuna chiyani?”

Amayiwo anati, “Lolani kuti ana anga awiriwa adzakhale mmodzi ku dzanja lanu lamanja ndi wina ku dzanja lanu lamazere mu ufumu wanu.”

22Yesu anawawuza kuti, “Simukudziwa chimene mukupempha. Kodi mungathe kumwera chikho chimene ndidzamwera Ine?”

Iwo anayankha nati, “Inde tingathe.”

23Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi mudzamwera chikho changa, koma kuti mudzakhale ku dzanja langa lamanja kapena lamazere si kwa Ine kupereka. Malo awa ndi a iwo amene anakonzeredweratu ndi Atate anga.”

24Ophunzira khumi aja, anawapsera mtima abale awiriwo. 25Yesu anawayitana onse pamodzi nati, “Mukudziwa kuti olamulira a mitundu ina ali ndi mphamvu pa iwo, ndipo akuluakulu awo amawalamulira. 26Siziyenera kutero ndi inu. Mʼmalo mwake, aliyense amene akufuna kukhala wamkulu pakati panu akhale wotumikira wanu. 27Ndipo aliyense amene akufuna kukhala woyamba akhale kapolo wanu. 28Momwenso Mwana wa Munthu sanabwere kudzatumikiridwa, koma kudzatumikira, ndi kupereka moyo wake kukhala dipo la anthu ambiri.”

Yesu Achiritsa Anthu Awiri Osaona

29Pamene Yesu ndi ophunzira ake ankachoka ku Yeriko, gulu lalikulu la anthu linawatsata. 30Amuna awiri osaona anakhala mʼmbali mwa msewu, ndipo pamene anamva kuti Yesu akudutsa anafuwula kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”

31Gulu la anthulo linawadzudzula iwo ndi kuwawuza kuti akhale chete, koma anafuwulitsabe kuti, “Ambuye, Mwana wa Davide, tichitireni chifundo!”

32Yesu anayima ndi kuwayitana ndipo anawafunsa kuti, “Mukufuna ndikuchitireni chiyani?”

33Anamuyankha nati, “Ambuye, tikufuna tione!”

34Yesu anamva nawo chifundo ndipo anakhudza maso awo. Nthawi yomweyo anaona namutsata Iye.

New Serbian Translation

Матеј 20:1-34

Исус приповеда параболу о једнако плаћеним радницима

1Царство небеско је слично домаћину који је у рану зору отишао да унајми раднике за свој виноград. 2Погодио се са њима да раде за један сребрњак на дан и послао их у свој виноград.

3Око девет сати ујутро је поново отишао и видео друге како стоје на тргу беспослени, 4па и њима рече: ’Идите и ви у виноград, па ћу вам платити што буде право.’ 5Они одоше. Отишао је поново око подне и око три по подне и учинио исто тако. 6Изашавши око пет по подне, нашао је неке друге како стоје на тргу, па их је упитао: ’Зашто стојите овде цели дан беспослени?’

7Они му одговорише: ’Нико нас није унајмио.’ Домаћин и њима рече: ’Идите и ви у мој виноград.’

8Кад је пало вече, господар винограда рече своме управитељу: ’Позови раднике и плати им, почевши од оних који су дошли последњи, па до оних који су дошли први.’

9Кад су дошли они који су радили од пет сати по подне, добили су по један сребрњак. 10Када су дошли они који су први почели да раде, помислили су да ће примити више. Али и они су примили по један сребрњак. 11Примивши своје, почели су да гунђају против домаћина. 12Говорили су: ’Ови који су дошли последњи радили су само један сат, а ти си их изједначио са нама који смо подносили тежину дневног посла и жегу.’

13А господар одговори једном од њих: ’Пријатељу, ја ти не чиним неправду. Ниси ли се погодио са мном за сребрњак? 14Узми своје па иди. А ја хоћу да дам овом последњем као и теби. 15Зар ја немам право да располажем својим новцем како хоћу? Или ти је око завидно зато што сам ја добар?’

16Тако ће последњи бити први, и први – последњи.“

Исус трећи пут предсказује своју смрт и васкрсење

17Док се Исус успињао према Јерусалиму, узео је Дванаесторицу ученика насамо, и путем им рекао: 18„Ево, пењемо се према Јерусалиму и Син Човечији ће бити предан водећим свештеницима и зналцима Светог писма, и они ће га осудити на смрт. 19Затим ће га изручити незнабошцима да му се ругају, и да га избичују и разапну, али ће он трећег дана васкрснути.“

Молба Јаковљеве и Јованове мајке

20Тада му приступи мајка синова Заведејевих са синовима и паде ничице да затражи нешто од њега. 21Исус је упита: „Шта желиш?“ Она му рече: „Одреди да ова моја два сина у твоме Царству седну поред тебе, један здесна, а други слева.“ 22Исус одговори: „Не знате шта тражите. Можете ли пити чашу коју ћу ја испити?“ „Можемо!“ – одговорише му они.

23Исус им узврати: „Чашу ћете испити, али ко ће седети мени здесна и слева, то ја нисам овлаштен да дам. То је за оне којима је то мој Отац наменио.“

24Када су то чула остала десеторица, разљутише се на два брата. 25Исус их онда све дозва и рече им: „Ви знате да владари владају народима и да их њихови великаши држе под влашћу. 26Тако нешто неће бити међу вама! Него, ко хоће међу вама да буде велик, нека вам буде слуга, 27и ко хоће међу вама да буде први, нека вам буде слуга. 28Тако ни Син Човечији није дошао да му служе, него да служи и да свој живот да као откупнину за многе.“

Два јерихонска слепца

29Кад су излазили из Јерихона, пође за њим силан народ. 30Уто, два слепца која су седела крај пута, чувши да Исус пролази, повикаше: „Смилуј се на нас, Господе, Сине Давидов!“

31Народ их је ућуткивао, али они још јаче повикаше: „Смилуј се на нас, Господе, Сине Давидов!“ 32Исус стаде, позва их и рече: „Шта желите да вам учиним?“

33Они му рекоше: „Господе, дај да прогледамо!“ 34Исус се сажали на њих, дотаче њихове очи и они одмах прогледаше. Потом су кренули за њим.