Mateyu 19 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 19:1-30

Za Kuthetsa Ukwati

1Yesu atatsiriza kunena zinthu zimenezi, anachoka ku Galileya ndi kupita ku chigawo cha Yudeya mbali ina ya mtsinje wa Yorodani. 2Magulu akulu a anthu anamutsatira Iye, ndipo iwo anachiritsidwa pomwepo.

3Afarisi ena anabwera kwa Iye kudzamuyesa. Anamufunsa Iye nati, “Kodi ndikololedwa kuti mwamuna amuleke mkazi wake pa chifukwa china chilichonse?”

4Iye anayankha kuti, “Kodi simunawerenge kuti pachiyambi Mulungu analenga iwo, ‘mwamuna ndi mkazi?’ 5Ndipo anati, ‘Pa chifukwa ichi mwamuna adzasiya abambo ake ndi amayi ake nakaphatikana ndi mkazi wake, ndipo awiriwo adzakhala thupi limodzi.’ 6Motero salinso awiri ayi koma mmodzi. Nʼchifukwa chake chimene Mulungu wachimanga pamodzi munthu wina asachilekanitse.”

7Ndipo iwo anamufunsa nati, “Nanga nʼchifukwa chiyani Mose analamula kuti mwamuna azipatsa mkazi wake kalata ya chisudzulo ndi kumuchotsa?”

8Yesu anayankha kuti, “Mose anakulolezani kuti muzisudzula akazi anu chifukwa cha kuwuma mitima kwanu. Koma sizinali chotere kuyambira pachiyambi. 9Ine ndikuwuzani kuti aliyense amene asudzula mkazi wake, osati chifukwa cha chiwerewere nakakwatira mkazi wina, achita chigololo.”

10Ophunzira ake anati kwa Iye, “Ngati umu ndi mmene zilili pa mwamuna ndi mkazi, kuli bwino kusakwatira.”

11Yesu anayankha kuti, “Si aliyense amene angavomere chiphunzitso ichi, koma kwa okhawo amene achimvetsetsa. 12Pakuti ena ndi akuti sangakwatire chifukwa anabadwa motero, ena ali motero chifukwa chofulidwa ndi anthu ndipo ena anawukana ukwati chifukwa cha ufumu wakumwamba. Iye amene angalandire ichi alandire.”

Yesu Adalitsa Ana

13Pamenepo anabwera nawo ana kwa Yesu kuti awasanjike manja ndi kuwapempherera. Koma ophunzira ake anadzudzula amene anabweretsa anawo.

14Yesu anati, “Lolani ana abwere kwa Ine, ndipo musawaletse pakuti ufumu wakumwamba ndi wa iwo onga anawa.” 15Atasanjika manja ake pa anawo, anachokapo.

Mnyamata Wolemera ndi Ufumu wa Mulungu

16Taonani mnyamata wina anabwera kwa Yesu namufunsa kuti, “Aphunzitsi, ndi chinthu chiti chabwino chimene ndiyenera kuchita kuti ndipeze moyo wosatha?”

17Yesu anayankha kuti, “Ukundifunsiranji Ine za chinthu chimene ndi chabwino? Pali mmodzi yekha amene ndi wabwino. Ngati ukufuna kulowa mʼmoyo wosatha mvera malamulo.”

18Mnyamatayo anamufunsa kuti, “Ndi ati?”

Yesu anayankha kuti, “Usaphe, usachite chigololo, usabe, usapereke umboni onama, 19lemekeza abambo ako ndi amayi ako ndipo konda mnansi wako monga iwe mwini.”

20Mnyamatayo anati, “Zonsezi ndimazisunga, nanga chatsala ndi chiyani?”

21Yesu anayankha kuti, “Ngati ukufuna kukhala wangwiro, pita kagulitse katundu wako ndi kupereka kwa osauka, ndipo udzakhala ndi chuma kumwamba. Ukakachita zimenezi, ukabwere udzanditsate Ine.”

22Mnyamatayo atamva zimenezi, anachoka mokhumudwa, chifukwa anali ndi chuma chambiri.

23Pamenepo Yesu anati kwa ophunzira ake, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti nʼkovuta kuti olemera akalowe mu ufumu wakumwamba. 24Komanso ndikuwuzani kuti, nʼkwapafupi kuti ngamira idzere pa kabowo ka zingano kusiyana ndi kuti wolemera akalowe mu ufumu wa Mulungu.”

25Ophunzira atamva zimenezi, anadabwa kwambiri ndipo anamufunsa kuti, “Nanga angapulumuke ndani?”

26Yesu anawayangʼana iwo nati, “Ndi anthu, izi nʼzosatheka, koma ndi Mulungu zinthu zonse zimatheka.”

27Petro anamuyankha Iye kuti, “Ife tinasiya zonse ndi kukutsatirani Inu! Nanga tsono ife tidzalandira chiyani?”

28Yesu anawawuza kuti, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti pa nthawi yokonzanso zinthu zonse, pamene Mwana wa Munthu adzakhala pa mpando wake waufumu mu ulemerero wake kumwamba, inu amene mwanditsata Ine mudzakhalanso pa mipando khumi ndi iwiri yaufumu, kuweruza mafuko khumi ndi awiri a Israeli. 29Ndipo aliyense amene wasiya nyumba, kapena abale, kapena alongo, kapena bambo kapena mayi kapena mkazi, kapena ana, kapena minda chifukwa cha Ine adzalandira madalitso ochuluka ndi kulandiranso moyo wosatha. 30Koma ambiri amene ali oyambirira adzakhala omalizira, ndipo ambiri amene ndi omalizira adzakhala oyambirira.”

New Serbian Translation

Матеј 19:1-30

Исус долази у сукоб са верским вођама

О разводу

1Када је Исус завршио ове беседе, напустио је Галилеју и дошао у област Јудеје, с друге стране Јордана. 2Пратило га је велико мноштво народа. Он је онда излечио болесне у народу.

3Тада му приступише неки фарисеји с намером да га искушају. Рекоше му: „Да ли је допуштено човеку да се разведе од своје жене из било каквог разлога?“ 4Исус одговори: „Зар нисте читали да је Створитељ у почетку створио мушко и женско?“ 5Уз то је рекао: „Стога ће човек оставити свога оца и своју мајку, те се приљубити уз своју жену, па ће двоје бити једно тело. 6Тако нису више двоје, него једно тело. Дакле, што је Бог саставио, човек да не раставља!“ 7А они му рекоше: „Зашто је онда Мојсије заповедио да муж да својој жени потврду о разводу брака када се од ње разводи?“

8Исус им одговори: „Мојсије вам је због тврдоће вашег срца допустио да се разводите од својих жена. Ипак, у почетку није било овако. 9А ја вам кажем: ко се разведе од своје жене, осим због њеног блуда, и ожени се другом, тај чини прељубу.“ 10Тада му рекоше његови ученици: „Ако тако стоје ствари између мужа и жене, онда је боље не женити се.“ 11Исус им одговори: „Не могу то сви разумети, него само они којима је дано. 12Има, наиме, неспособних за брак, јер су рођени са телесном маном. Има, опет, и таквих који су неспособни за брак, јер су их људи осакатили. А има и таквих који су сами себе лишили брачног живота, због Царства небеског. Ко може да прихвати, нека прихвати.“

Исус благосиља децу

13Тада су му довели децу да би положио руке на њих и помолио се за њих, али су им ученици бранили. 14Исус рече: „Пустите децу и не спречавајте их да долазе к мени, јер таквима припада Царство небеско!“ 15Исус положи руке на њих па оде оданде.

Богати младић

16Уто му приступи неки човек и рече: „Учитељу, какво добро треба да чиним да бих имао вечни живот?“ 17Исус му одговори: „Зашто ме питаш шта је добро? Само је Један добар. Ако хоћеш да уђеш у живот, држи заповести.“

18Човек га упита: „А које?“ Исус му одговори: „Не убиј, не чини прељубе, не кради, не сведочи лажно, 19поштуј свога оца и мајку, и воли ближњега свога као самога себе.“ 20Младић му рече: „Све сам то извршавао. Шта ми још недостаје?“

21Исус му одговори: „Ако хоћеш да будеш савршен, онда иди и продај све што имаш, па раздели то сиромасима и имаћеш благо на небесима. Онда дођи и следи ме.“

22Када је то младић чуо, отишао је жалостан, јер је имао велики иметак.

23Исус рече својим ученицима: „Заиста вам кажем да је богаташу тешко ући у Царство небеско! 24Још вам кажем да је лакше камили да прође кроз иглене уши, него богаташу да уђе у Царство Божије.“

25Када су ученици чули ово, запањише се и рекоше: „Ко се онда може спасти?“

26Исус их погледа па им рече: „За људе је ово немогуће, али је за Бога све могуће.“

27Тада му Петар рече: „Ево, ми смо све оставили и кренули за тобом. Шта ћемо, дакле, добити за то?“

28А Исус им рече: „Заиста вам кажем: долази дан свеопште обнове када ће Син Човечији сести на престо своје славе. Тада ћете ви који ме следите и сами сести на дванаест престола и судити над дванаест племена Израиљевих. 29И свако ко због мене остави куће, или браћу, или сестре, или оца, или мајку, или жену, или децу, или њиве, примиће стоструко и баштиниће вечни живот. 30Али ће многи први бити последњи, и последњи – први.