Mateyu 14 – CCL & CARS

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mateyu 14:1-36

Kuphedwa kwa Yohane Mʼbatizi

1Pa nthawi imeneyo Mfumu Herode anamva za mbiri ya Yesu. 2Ndipo iye anati kwa antchito ake, “Uyu ndi Yohane Mʼbatizi; iye wauka kwa akufa! Ichi ndi chifukwa chake mphamvu zodabwitsa zikugwira ntchito mwa iye.”

3Pakuti Herode anamugwira Yohane ndi kumumanga ndipo anamuyika mʼndende chifukwa cha Herodia mkazi wa mʼbale wake Filipo. 4Chifukwa Yohane anakhala akunena kwa iye kuti, “Sichololedwa kwa inu kutenga mkaziyo.” 5Herode anafuna kupha Yohane koma iye anaopa anthu chifukwa anamuyesa iye mneneri.

6Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwa Herode, mwana wamkazi wa Herodia anavina pamaso pa anthu ndipo anasangalatsa kwambiri. 7Kotero Herode analonjeza ndi lumbiro kumupatsa chilichonse chimene mwanayo angamupemphe. 8Ndipo atamupangira amayi ake anati, “Mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.” 9Mfumuyo inamva chisoni koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo amene anali pa phwando lake analamulira kuti chofuna chake chipatsidwe; 10ndipo anakadula mutu wa Yohane mʼndende. 11Mutu wake anawubweretsa mʼmbale ndi kumupatsa mtsikanayo amene anawutengera kwa amayi ake. 12Ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo wake ndi kukawuyika mʼmanda. Pomwepo iwo anapita kukamuwuza Yesu.

Yesu Adyetsa Anthu 5,000

13Yesu atamva zimene zinachitika, anachoka pa bwato mwachinsinsi kupita kumalo a yekha. Magulu a anthu atamva izi anamutsatira Iye poyenda pansi kuchokera ku mizinda. 14Yesu atafika ku mtunda, ndi kuona gulu lalikulu la anthu, Iye anamva nawo chifundo ndipo anachiritsa odwala awo.

15Kutayamba mdima, ophunzira anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kutchire ndipo kwayamba kale kuda. Awuzeni anthu azipita kuti afike ku midzi ndi kukadzigulira zakudya.”

16Yesu anawayankha kuti, “Sikofunika kuti azipita. Inuyo muwapatse kanthu kuti adye.”

17Iwo anayankha kuti, “Tili ndi malofu asanu okha a buledi ndi nsomba ziwiri.”

18Koma Iye anati, “Bweretsani kwa Ine.” 19Analamula anthu kuti akhale pansi pa udzu ndipo anatenga buledi musanu ndi nsomba ziwiri nayangʼana kumwamba, nayamika nagawa bulediyo. Kenaka anapereka bulediyo kwa ophunzira ake ndipo ophunzirawo anagawira anthu. 20Onse anadya nakhuta ndipo ophunzira anatola zotsalira ndi kudzaza madengu khumi ndi awiri. 21Chiwerengero cha amene anadya kupatulako amayi ndi ana chinali pafupifupi amuna 5,000.

Yesu Ayenda pa Nyanja

22Nthawi yomweyo anawawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita kutsidya lina pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita kwawo. 23Atatha kuwawuza kuti azipita kwawo, Iye anakwera ku phiri yekha kukapemphera. Pamene kumada anali kumeneko yekha. 24Pamenepo nʼkuti bwato litapita patali pangʼono kuchokera ku mtunda ndipo linavutika ndi mafunde chifukwa mphepo inkawomba mokumana nalo.

25Pa ora lachinayi usiku, Yesu anabwera kwa iwo akuyendabe pa nyanja. 26Ophunzira atamuona akuyenda pa nyanja, anaopa nati, “Ndi mzukwa!” Ndipo analira chifukwa cha mantha.

27Koma Yesu nthawi yomweyo anawawuza kuti, “Limbani mtima! Ndine, musaope.”

28Petro anayankha nati, “Ambuye ngati ndinu, mundiwuze ndibwere kuli inuko pa madzipo.”

29Iye anati, “Bwera.”

Pamenepo Petro anatuluka mʼbwato ndipo anayenda pa madzi kupita kwa Yesu. 30Koma ataona mphepo, iye anachita mantha ndipo anayamba kumira, nafuwula nati, “Ambuye ndipulumutseni!”

31Ndipo mofulumira Yesu anatambasula dzanja lake namugwira iye, nati, “Iwe wachikhulupiriro chochepa, bwanji unakayika?”

32Ndipo atalowa mʼbwato mphepo inaleka. 33Pamenepo amene anali mʼbwato anamulambira Iye, nati, “Zoonadi, Inu ndinu Mwana wa Mulungu.”

34Atawoloka, anafika ku Genesareti. 35Anthu akumeneko atamuzindikira Yesu, iwo anatumiza mawu kwa onse ozungulira deralo. Anthu anabwera ndi odwala awo onse kwa Iye. 36Ndipo anamupempha alole kuti akhudze mphonje ya mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachiritsidwa.

Священное Писание

Матай 14:1-36

Царь Ирод убивает пророка Яхию

(Мк. 6:14-29; Лк. 9:7-9)

1В то время об Исе услышал и правитель Ирод14:1 Это Ирод Антипа, сын Ирода Великого от самарянки Малфаки. Он правил Галилеей и Переей с 4 г. до н. э. по 39 г. н. э.. 2Он говорил своим приближённым:

– Это пророк Яхия. Он воскрес из мёртвых, и поэтому в Нём такая чудодейственная сила.

3В своё время Ирод арестовал Яхию, связал его и бросил в темницу из-за Иродиады, жены своего брата Филиппа14:3 Это Ирод Филипп I, сын Ирода Великого от Мариамны., 4потому что Яхия говорил ему: «Нельзя тебе жить с ней»14:4 Женитьба Ирода на жене брата была нарушением Закона Всевышнего (см. Лев. 18:16; 20:21).. 5Ирод хотел убить Яхию, но боялся народа, так как все считали его пророком. 6И вот когда Ирод праздновал свой день рождения, дочь Иродиады танцевала перед гостями и так понравилась Ироду, 7что он поклялся дать ей всё, чего бы она ни попросила. 8Наученная своей матерью девушка сказала:

– Подай мне сюда на блюде голову пророка Яхии.

9Царь опечалился, но так как он поклялся перед возлежавшими за столом гостями, то велел исполнить её желание. 10По его приказу Яхии отрубили в темнице голову, 11принесли её на блюде и отдали девушке, а та отнесла её матери. 12Ученики Яхии, забрав тело, похоронили его, а затем пошли и рассказали обо всём Исе.

Насыщение более пяти тысяч человек

(Мк. 6:32-44; Лк. 9:10-17; Ин. 6:1-13)

13Услышав о судьбе Яхии, Иса переправился на лодке в пустынное место, чтобы побыть одному. Но люди из окрестных городов узнали, куда Он отправился, и пошли туда пешком. 14Когда Иса сошёл на берег и увидел большую толпу, Он сжалился над людьми и исцелил больных, которые были среди них. 15Наступил вечер. Ученики Исы подошли к Нему и сказали:

– Место здесь пустынное, и уже поздно, отпусти людей, чтобы они успели дойти до ближайших посёлков и купить себе еды.

16Иса ответил:

– Им не нужно уходить отсюда. Вы дайте им есть.

17– Но у нас только пять лепёшек и две рыбы, – ответили ученики.

18– Принесите всё это ко Мне, – сказал Иса.

19Он велел народу расположиться на траве, взял эти пять лепёшек и две рыбы и, подняв глаза к небу, благословил пищу. Затем Он стал разламывать лепёшки и давать их Своим ученикам, а те – народу. 20Все ели и насытились, а когда собрали оставшиеся куски, то их набралось двенадцать полных корзин. 21Всего же ело пять тысяч мужчин, не считая женщин и детей.

Хождение Исы Масиха по воде

(Мк. 6:45-51; Ин. 6:16-21)

22Сразу после этого Иса велел ученикам сесть в лодку и переправиться на другую сторону озера, а Сам Он оставался, пока не отпустил народ. 23А когда народ разошёлся, Иса поднялся на гору помолиться. Наступил вечер, и Иса оставался на горе один. 24Тем временем лодка была уже далеко от берега. Её били волны, так как дул встречный ветер. 25Уже перед рассветом Иса пошёл к ученикам, ступая по озеру. 26Но ученики, увидев Его идущим по воде, очень испугались.

– Это призрак! – закричали они от страха.

27Но Иса сразу же заговорил с ними:

– Успокойтесь, это Я, не бойтесь.

28– Повелитель, если это Ты, – сказал тогда Петир, – то разреши мне прийти к Тебе по воде.

29– Иди, – сказал Иса.

Петир вышел из лодки и пошёл по воде к Исе. 30Но увидев, как сильно дует ветер, он испугался и, начав тонуть, закричал:

– Повелитель, спаси меня!

31Иса тотчас протянул руку и поддержал его.

– Маловерный, – сказал Он, – зачем же ты стал сомневаться?

32Когда они вошли в лодку, ветер утих. 33Все, кто был в лодке, поклонились Исе.

– Ты действительно (вечный) Сын Всевышнего, – сказали они.

Исцеление больных в Генисарете

(Мк. 6:53-56)

34Переправившись на другую сторону озера, они сошли на берег в Генисарете. 35Местные жители узнали Ису и разнесли весть о Его приходе по всей округе. К Исе принесли всех больных 36и просили Его, чтобы Он позволил им прикоснуться лишь к кисточке на краю Его одежды14:36 См. сноску на 9:20.. И все, кто прикасался, выздоравливали.