Masalimo 96 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 96:1-13

Salimo 96

1Imbirani Yehova nyimbo yatsopano;

Imbirani Yehova dziko lonse lapansi.

2Imbirani Yehova, tamandani dzina lake;

lalikirani chipulumutso chake tsiku ndi tsiku.

3Lengezani ulemerero wake pakati pa mayiko,

ntchito zake zodabwitsa pakati pa mitundu yonse ya anthu.

4Pakuti wamkulu ndi Yehova ndipo ndi woyenera kwambiri kumutamanda;

ayenera kuopedwa kupambana milungu yonse.

5Pakuti milungu yonse ya anthu a mitundu ina ndi mafano,

koma Yehova analenga mayiko akumwamba.

6Ulemu ndi ufumu zili pamaso pake,

mphamvu ndi ulemerero zili mʼmalo ake opatulika.

7Perekani kwa Yehova, inu mabanja a anthu a mitundu ina,

perekani kwa Yehova ulemerero ndi mphamvu.

8Perekani kwa Yehova ulemerero woyenera dzina lake;

bweretsani chopereka ndipo mulowe mʼmabwalo ake.

9Lambirani Yehova mu ulemerero wa chiyero chake;

njenjemerani pamaso pake, dziko lonse lapansi.

10Nenani pakati pa mitundu ya anthu, “Yehova akulamulira.”

Dziko lonse lakhazikika molimba, silingasunthidwe;

Iye adzaweruza mitundu ya anthu molungama.

11Mayiko akumwamba asangalale, dziko lapansi likondwere;

nyanja ikokome, ndi zonse zili mʼmenemo;

12minda ikondwere pamodzi ndi chilichonse chili mʼmenemo.

Pamenepo mitengo yonse ya mʼnkhalango idzayimba ndi chimwemwe;

13idzayimba pamaso pa Yehova,

pakuti Iye akubwera kudzaweruza dziko lapansi;

adzaweruza dziko lonse mwachilungamo

ndi mitundu ya anthu onse mʼchoonadi.

Nueva Versión Internacional

Salmo 96:1-13

Salmo 96

96:1-131Cr 16:23-33

1¡Canten al Señor un cántico nuevo!

¡Canten al Señor, habitantes de toda la tierra!

2¡Canten al Señor, alaben su nombre!

¡Proclamen día tras día su salvación!

3Anuncien su gloria entre las naciones,

sus maravillas a todos los pueblos.

4¡Grande es el Señor y digno de alabanza,

más temible que todos los dioses!

5Todos los dioses de las naciones son ídolos,

pero el Señor ha hecho los cielos.

6El esplendor y la majestad son sus heraldos;

hay poder y belleza en su santuario.

7¡Tributen al Señor, pueblos todos!

¡Tributen al Señor la gloria y el poder!

8¡Tributen al Señor la gloria que merece su nombre!

¡Traigan sus ofrendas y entren en sus atrios!

9¡Póstrense ante el Señor en la hermosura de su santidad!

¡Tiemble delante de él toda la tierra!

10Digan las naciones:

«¡El Señor reina!».

Ha establecido el mundo con firmeza;

jamás será removido.

Él juzga a los pueblos con equidad.

11¡Alégrense los cielos, regocíjese la tierra!

¡Brame el mar y todo lo que él contiene!

12¡Canten alegres los campos y todo lo que hay en ellos!

¡Que canten alegres todos los árboles del bosque!

13¡Canten delante del Señor porque ya viene!

¡Ya viene a juzgar la tierra!

Y juzgará al mundo con justicia

y a los pueblos con fidelidad.