Masalimo 95 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 95:1-11

Salimo 95

1Bwerani, tiyeni timuyimbire Yehova mwachimwemwe,

tiyeni tifuwule kwa Thanthwe la chipulumutso chathu

2Tiyeni tibwere pamaso pake ndi chiyamiko

ndipo mupembedzeni Iyeyo ndi zida zoyimbira ndi nyimbo.

3Pakuti Yehova ndi Mulungu wamkulu,

mfumu yayikulu pamwamba pa milungu yonse.

4Mʼmanja mwake muli maziko ozama a dziko lapansi,

ndipo msonga za mapiri ndi zake.

5Nyanja ndi yake, pakuti anayilenga ndi Iye,

ndipo manja ake anawumba mtunda wowuma.

6Bwerani, tiyeni tiwerame pomulambira,

tiyeni tigwade pamaso pa Yehova Mlengi wathu;

7pakuti Iye ndiye Mulungu wathu

ndipo ife ndife anthu a pabusa pake,

ndi nkhosa za mʼdzanja lake.

Lero ngati inu mumva mawu ake,

8musawumitse mitima yanu monga momwe munachitira pa Meriba,

monga munachitira tsiku lija pa Masa mʼchipululu.

9Kumene makolo anu anandiyesa ndi kundiputa,

ngakhale anaona zimene Ine ndinazichita.

10Kwa zaka makumi anayi ndinali wokwiya ndi mʼbado umenewo;

ndipo ndinati, “Iwo ndi anthu amene mitima yawo imasochera

ndipo sanadziwe njira zanga.”

11Choncho ndili chikwiyire, ndinalumbira kuti,

“Iwowa sadzalowa ku malo anga a mpumulo.”

New International Version

Psalms 95:1-11

Psalm 95

1Come, let us sing for joy to the Lord;

let us shout aloud to the Rock of our salvation.

2Let us come before him with thanksgiving

and extol him with music and song.

3For the Lord is the great God,

the great King above all gods.

4In his hand are the depths of the earth,

and the mountain peaks belong to him.

5The sea is his, for he made it,

and his hands formed the dry land.

6Come, let us bow down in worship,

let us kneel before the Lord our Maker;

7for he is our God

and we are the people of his pasture,

the flock under his care.

Today, if only you would hear his voice,

8“Do not harden your hearts as you did at Meribah,95:8 Meribah means quarreling.

as you did that day at Massah95:8 Massah means testing. in the wilderness,

9where your ancestors tested me;

they tried me, though they had seen what I did.

10For forty years I was angry with that generation;

I said, ‘They are a people whose hearts go astray,

and they have not known my ways.’

11So I declared on oath in my anger,

‘They shall never enter my rest.’ ”