Masalimo 91 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 91:1-16

Salimo 91

1Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba

adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.

2Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,

Mulungu wanga amene ndimadalira.”

3Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje

ndi ku mliri woopsa;

4Adzakuphimba ndi nthenga zake,

ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;

kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.

5Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,

kapena muvi wowuluka masana,

6kapena mliri umene umayenda mu mdima,

kapena zowononga za pa nthawi ya masana.

7Anthu 1,000 atha kufa pambali pako,

anthu 10,000 kudzanja lako lamanja,

koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.

8Udzapenya ndi maso ako

ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.

9Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;

wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.

10Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,

zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.

11Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,

kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;

12ndipo adzakunyamula ndi manja awo,

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.

13Udzapondaponda mkango ndi njoka,

udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.

14“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;

ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.

15Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;

ndidzakhala naye pa mavuto,

ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.

16Ndidzamupatsa moyo wautali

ndi kumupulumutsa.”

Nueva Versión Internacional

Salmo 91:1-16

Salmo 91

1El que habita al abrigo del Altísimo

descansará a la sombra del Todopoderoso.

2Yo digo al Señor: «Tú eres mi refugio,

mi fortaleza, el Dios en quien confío».

3Solo él puede librarte

de las trampas del cazador

y de mortíferas plagas,

4pues te cubrirá con sus plumas

y bajo sus alas hallarás refugio.

Su verdad será tu escudo y tu baluarte.

5No temerás el terror de la noche

ni la flecha que vuela de día

6ni la plaga que acecha en las sombras

ni la peste que destruye a mediodía.

7Podrán caer a tu lado mil

y diez mil a tu derecha,

pero a ti no te afectará.

8No tendrás más que abrir bien los ojos

para ver a los impíos recibir su merecido.

9Ya que has puesto al Señor por tu91:9 tu. Lit. mi. refugio,

al Altísimo por tu protección,

10ningún mal habrá de sobrevenirte,

ningún desastre llegará a tu hogar.

11Porque él ordenará que sus ángeles

te protejan en todos tus caminos.

12Con sus propias manos te sostendrán

para que no tropieces con piedra alguna.

13Aplastarás al león y a la víbora;

hollarás al cachorro de león y a la serpiente.

14«Yo lo libraré, porque él me ama;

lo protegeré, porque conoce mi nombre.

15Él me invocará y yo le responderé;

estaré con él en momentos de angustia,

lo libraré y lo llenaré de honores.

16Lo colmaré con muchos años de vida

y le haré gozar de mi salvación».