Masalimo 90 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 90:1-17

BUKU LACHINAYI

Masalimo 90–106

Salimo 90

Pemphero la Mose munthu wa Mulungu.

1Ambuye, mwakhala muli malo athu okhalamo

pa mibado yonse.

2Mapiri asanabadwe,

musanalenge nʼkomwe dziko lapansi ndi dziko lonse,

kuyambira muyaya mpaka muyaya Inu ndinu Mulungu.

3Inu mumabwezera anthu ku fumbi,

mumati, “Bwerera ku fumbi iwe mwana wa munthu.”

4Pakuti zaka 1,000 pamaso panu

zili ngati tsiku limene lapita

kapena ngati kamphindi ka usiku.

5Inu mumasesa anthu mʼtulo ta imfa,

iwo ali ngati udzu watsopano wa mmawa,

6ngakhale kuti mmawa umaphuka watsopano,

pofika madzulo wauma ndi kufota.

7Ife tathedwa ndi mkwiyo wanu;

ndipo taopsezedwa ndi kuyipidwa kwanu.

8Mwayika mphulupulu zathu pamaso panu,

machimo athu obisika poonekera pamaso panu.

9Masiku athu onse amatha ali pansi pa ukali wanu;

timatsiriza zaka zathu ndi kubuwula.

10Kuchuluka kwa masiku athu ndi 70,

kapena 80 ngati tili ndi mphamvu;

komabe zaka zonsezi ndi za mavuto ndi nkhawa,

zimatha mofulumira ndipo ife timawulukira kutali.

11Kodi ndani amadziwa mphamvu ya mkwiyo wanu?

Pakuti ukali wanu ndi waukulu ngati ulemu umene uyenera Inu.

12Tiphunzitseni kuwerenga masiku athu molondola,

kuti tikhale ndi mtima wanzeru.

13Lezani mtima Inu Yehova! Kodi mudzatikwiyira mpaka liti?

Achitireni chifundo atumiki anu.

14Mutikhutitse mmawa ndi chikondi chanu chosatha,

kuti tiyimbe ndi chimwemwe ndi kukhala okondwa masiku athu onse.

15Tisangalatseni masiku ambiri monga masiku amene mwatisautsa,

kwa zaka zambiri monga momwe tinaonera mavuto.

16Ntchito zanu zionetsedwe kwa atumiki anu,

kukongola kwanu kwa ana awo.

17Kukoma mtima kwa Ambuye Mulungu wathu kukhale pa ife;

tikhazikitsireni ntchito ya manja athu;

inde, khazikitsani ntchito ya manja athu.

Hoffnung für Alle

Psalm 90:1-17

Viertes Buch

(Psalm 90–106)

Ist denn alles vergeblich?

1Ein Gebet von Mose, dem Mann Gottes.

Herr, solange es Menschen gibt, bist du unsere Zuflucht!

2Ja, bevor die Berge geboren wurden,

noch bevor Erde und Weltall unter Wehen entstanden,

warst du, o Gott, schon da. Du bist ohne Anfang und Ende.

3Du lässt den Menschen wieder zu Staub werden.

»Kehr zurück!«, sprichst du zu ihm.

4Tausend Jahre sind für dich wie ein einziger Tag,

der doch im Flug vergangen ist,

kurz wie ein paar Stunden Schlaf.

5Du reißt die Menschen hinweg,

sie verschwinden so schnell wie ein Traum nach dem Erwachen.

Sie vergehen wie das Gras:

6Morgens sprießt es und blüht auf,

doch schon am Abend welkt und verdorrt es im heißen Wüstenwind.

7Ja, durch deinen Zorn vergehen wir,

schnell ist es mit uns zu Ende!

8Unsere Schuld liegt offen vor dir,

auch unsere geheimsten Verfehlungen bringst du ans Licht.

9Dein Zorn lässt unser Leben verrinnen –

schnell wie ein kurzer Seufzer ist es vorbei!

10Unser Leben dauert siebzig, vielleicht sogar achtzig Jahre.

Doch alles, worauf wir stolz sind,

ist nur Mühe, viel Lärm um nichts!

Wie schnell eilen die Jahre vorüber!

Wie rasch schwinden wir dahin!

11Doch wer kann begreifen, wie gewaltig dein Zorn ist?

Wer fürchtet sich schon davor?

12Mach uns bewusst, wie kurz das Leben ist,

damit wir unsere Tage weise nutzen!

13Herr, wende dich uns wieder zu!

Wie lange soll dein Zorn noch dauern?

Hab Erbarmen mit uns, wir sind doch deine Diener!

14Schenke uns deine Liebe jeden Morgen neu!

Dann können wir singen und uns freuen, solange wir leben!

15So viele Jahre litten wir unter Not und Bedrückung;

lass uns nun ebenso viele Jahre Freude erleben!

16Zeige uns, wie machtvoll du eingreifst;

auch unsere Kinder sollen deine mächtigen Taten sehen!

17Herr, unser Gott! Zeige uns deine Güte!

Lass unsere Mühe nicht vergeblich sein!

Ja, lass unsere Arbeit Früchte tragen!