Masalimo 91 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 91:1-16

Salimo 91

1Iye amene amakhala mu mthunzi wa Wammwambamwamba

adzapuma mu mthunzi wa Wamphamvuzonse.

2Ndidzanena za Yehova, “Iye ndiye pothawira panga ndi linga langa,

Mulungu wanga amene ndimadalira.”

3Ndithu, Iye adzakupulumutsa ku msampha wa mlenje

ndi ku mliri woopsa;

4Adzakuphimba ndi nthenga zake,

ndipo udzapeza malo othawira mʼmapikomo;

kukhulupirika kwake kudzakhala chishango chako ndi lihawo.

5Sudzachita mantha ndi zoopsa za usiku,

kapena muvi wowuluka masana,

6kapena mliri umene umayenda mu mdima,

kapena zowononga za pa nthawi ya masana.

7Anthu 1,000 atha kufa pambali pako,

anthu 10,000 kudzanja lako lamanja,

koma zoopsazo sizidzafika pafupi ndi iwe.

8Udzapenya ndi maso ako

ndipo udzaona mmene anthu oyipa amalangidwira.

9Pakuti wasankha Wammwambamwamba kukhala malo ako okhalamo;

wavomera Yehova kukhala kothawira kwako.

10Choncho palibe choyipa chimene chidzakugwera,

zoopsa sizidzafika pafupi ndi tenti yako.

11Pakuti adzalamulira angelo ake za iwe,

kuti akutchinjirize mosamala pa njira zako zonse;

12ndipo adzakunyamula ndi manja awo,

kuti phazi lako lisagunde pa mwala.

13Udzapondaponda mkango ndi njoka,

udzapondereza mkango wamphamvu ndiponso chinjoka.

14“Chifukwa iye amandikonda,” akutero Yehova, “Ndidzamulanditsa;

ndidzamuteteza pakuti wavomereza dzina langa.

15Adzandiyitana, ndipo ndidzamuyankha;

ndidzakhala naye pa mavuto,

ndidzamupulumutsa ndi kumulemekeza.

16Ndidzamupatsa moyo wautali

ndi kumupulumutsa.”

Hoffnung für Alle

Psalm 91:1-16

Unter Gottes Schutz

1Wer unter dem Schutz des Höchsten wohnt,

der kann bei ihm, dem Allmächtigen, Ruhe finden.

2Auch ich sage zum Herrn:

»Du schenkst mir Zuflucht wie eine sichere Burg!

Mein Gott, dir gehört mein ganzes Vertrauen!«

3Er bewahrt dich vor versteckten Gefahren

und hält jede tödliche Krankheit von dir fern.

4Wie ein Vogel seine Flügel über die Jungen ausbreitet,

so wird er auch dich stets behüten und dir nahe sein.

Seine Treue umgibt dich wie ein starker Schild.

5Du brauchst keine Angst zu haben vor den Gefahren der Nacht

oder den heimtückischen Angriffen bei Tag.

6Selbst wenn die Pest im Dunkeln zuschlägt

und am hellen Tag das Fieber wütet,

musst du dich doch nicht fürchten.

7Wenn tausend neben dir tot umfallen,

ja, wenn zehntausend um dich herum sterben –

dich selbst trifft es nicht!

8Mit eigenen Augen wirst du sehen,

wie Gott es denen heimzahlt, die ihn missachten.

9Du aber darfst sagen: »Beim Herrn bin ich geborgen!«

Ja, bei Gott, dem Höchsten, hast du Heimat gefunden.

10Darum wird dir nichts Böses zustoßen,

kein Unglück wird dein Haus erreichen.

11Denn Gott wird dir seine Engel schicken,

um dich zu beschützen, wohin du auch gehst.

12Sie werden dich auf Händen tragen,

und du wirst dich nicht einmal an einem Stein stoßen!

13Löwen werden dir nichts anhaben,

auf Schlangen trittst du ohne Gefahr.

14Gott sagt: »Er liebt mich von ganzem Herzen,

darum will ich ihn retten.

Ich werde ihn schützen, weil er mich kennt und ehrt.

15Wenn er zu mir ruft, erhöre ich ihn.

Wenn er keinen Ausweg mehr weiß, bin ich bei ihm.

Ich will ihn befreien und zu Ehren bringen.

16Ich lasse ihn meine Rettung erfahren

und gebe ihm ein langes und erfülltes Leben!«