Salimo 82
Salimo la Asafu.
1Mulungu akutsogolera msonkhano waukulu;
Iye akuweruza pakati pa “milungu.”
2“Mudzateteza osalungama mpaka liti,
ndi kukondera anthu oyipa?
3Tetezani anthu ofowoka ndi amasiye;
mukhazikitse ufulu wa anthu osauka ndi ozunzika.
4Landitsani anthu ofowoka ndi osowa;
apulumutseni mʼdzanja la anthu oyipa.
5“Iwo sadziwa kanthu, sazindikira kalikonse.
Amayendayenda mu mdima;
maziko onse a dziko lapansi agwedezeka.
6“Ndinati, ‘Inu ndinu Mulungu,
nonsenu ndinu ana a Wammwambamwamba.’
7Koma mudzafa ngati anthu wamba;
mudzagwa ngati wolamula wina aliyense.”
8Dzukani Inu Mulungu, weruzani dziko lapansi,
pakuti mayiko onse ndi cholowa chanu.
Псалам 82
Псалам Асафов.
1Бог је стао у Божијем збору,
па сад суди међу боговима:
2„Докле ћете судити нечасно
и држати страну злотворима? Села
3Заступајте право убогога и сиротога,
оправдајте сиромаха и невољника.
4Спасавајте слабог и тлаченог,
избавите их из руке зликоваца.
5Али нису знали, нису разумели;
у тами су посртали
и темеље земљи задрмали.
6Ја рекох: ’Богови сте,
сви сте деца Свевишњега!’
7Ипак ћете помрети ко људи,
пропашћете ко и главар сваки.“
8Устани, Боже, и суди земљи,
јер сви су народи наследство твоје!