Masalimo 83 – CCL & NSP

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 83:1-18

Salimo 83

Nyimbo. Salimo la Asafu.

1Inu Mulungu musakhale chete;

musangoti phee, Mulungu musangoti duu.

2Onani adani anu akuchita chiwawa,

amene amadana nanu autsa mitu yawo.

3Mochenjera iwo akukambirana za chiwembu kutsutsana ndi anthu anu;

Iwo akukonzekera kutsutsana ndi omwe mumawakonda.

4Iwo akunena kuti, “Bwerani” akutero, “Tiyeni tiwononge mtundu wonsewu

kuti dzina la Israeli lisakumbukikenso.”

5Ndi mtima umodzi akukonzekera chiwembu;

Iwo achita mgwirizano kutsutsana nanu:

6Matenti a Edomu ndi Aismaeli,

Mowabu ndi Ahagiri,

7Agebala, Aamoni ndi Aamaleki,

Afilisti, pamodzi ndi anthu a ku Turo.

8Ngakhalenso Aasiriya aphatikizana nawo

kupereka mphamvu kwa ana a Loti.

Sela

9Muwachitire zomwe munachitira Amidiyani,

monga munachitira Sisera ndi Yabini ku mtsinje wa Kisoni.

10Amene anawonongedwa ku Endori

ndi kukhala ngati zinyalala.

11Anthu awo otchuka muwachite zomwe munachita Orebu ndi Zeebu

ana a mafumu muwachite zomwe munachita Zeba ndi Zalimuna,

12amene anati, “Tiyeni tilande dziko

la msipu la Mulungu.”

13Muwasandutse fumbi lowuluka, Inu Mulungu wanga,

ngati mankhusu owuluka ndi mphepo.

14Monga moto umatentha nkhalango,

kapena malawi a moto kuyatsa phiri,

15kotero muwathamangitse ndi mphepo yamkuntho,

ndi kuwachititsa mantha ndi namondwe.

16Muphimbe nkhope zawo ndi manyazi

kuti adzafunefune dzina lanu Yehova.

17Achite manyazi ndi mantha nthawi zonse;

awonongeke mwa manyazi.

18Adziwe kuti Inu amene dzina lanu ndi Yehova,

ndinu nokha Wammwambamwamba pa dziko lonse lapansi.

New Serbian Translation

Псалми 83:1-18

Псалам 83

Песма. Псалам Асафов.

1О, Боже, немој да заћутиш!

Не онеми,

немој да мирујеш, о Боже!

2Гле, ено их буче твоји душмани,

главу дижу они што те мрзе!

3Сплетке кују против твог народа

и заверу праве твоме штићенику.

4Рекли су: „Дођите, дајте да их сатремо као народ,

да се име Израиља више не спомене!“

5Ено, сви су сложни у замисли

да против тебе савез склопе:

6шатори Едома и Исмаила,

Моава и Агарина;

7Гевала, Амона и Амалика,

Филистејци с житељима Тира.

8Још им је и Асирија пришла,

пристала ко војска уз децу Лотову. Села

9Учини им као Мадијану и као Сисери,

као Јавину на потоку Кисону!

10Били су потрвени код Ен-Дора,

претворени у ђубриво за њиву.

11С племићима им поступи као с Оривом и Зивом,

а са кнезовима њиховим као са Зевејем и Салманом.

12Јер они говоре:

„Заузмимо Божије пашњаке!“

13О, мој Боже, претвори их у клупко корова,

у плеву на ветру!

14Ко кад ватра шуму пали

и ко кад пламен горе жари,

15тако их потерај вихором својим,

ужасни их својом олујом.

16Бешчашћем им лице покриј,

па нек вапе за именом твојим, о, Господе!

17Нек се стиде и смету довека!

Нек пропадну срамећи се!

18Па нека се зна – име ти је Господ –

над земљом си целом ти једини Свевишњи!