Masalimo 73 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 73:1-28

BUKU LACHITATU

Masalimo 73–89

Salimo 73

Salimo la Asafu.

1Mulungu ndi wabwino ndithu kwa Israeli,

kwa iwo amene ndi oyera mtima.

2Koma kunena za ine, mapazi anga anali pafupi kuterereka;

ndinatsala pangʼono kugwa.

3Pakuti ndinkachitira nsanje odzitamandira,

pamene ndinaona mtendere wa anthu oyipa.

4Iwo alibe zosautsa;

matupi awo ndi athanzi ndi amphamvu.

5Saona mavuto monga anthu ena;

sazunzika ngati anthu ena onse.

6Nʼchifukwa chake kunyada kuli monga mkanda wa mʼkhosi mwawo;

amadziveka chiwawa.

7Mʼmitima yawo yokhota mumachokera zolakwa;

zoyipa zochokera mʼmaganizo awo sizidziwa malire.

8Iwowo amanyogodola ndi kumayankhula zoyipa;

mwa kudzikuza kwawo amaopseza ena nʼkumati, “Tikuponderezani.”

9Pakamwa pawo pamayankhula monyoza Mulungu kumwamba

ndipo lilime lawo limayenda pa dziko lapansi.

10Nʼchifukwa chake anthu awo amapita kwa iwowo

ndi kumwa madzi mochuluka.

11Iwo amati, “Kodi Mulungu angadziwe bwanji?

Kodi Wammwambamwamba angadziwe kalikonse?”

12Umu ndi mmene oyipa alili;

nthawi zonse ali pabwino ndipo chuma chawo chimachulukirachulukira.

13Ndithudi ine ndawusunga pachabe mtima wanga woyera;

pachabe ndasamba mʼmanja mwanga mwa kusalakwa kwanga.

14Tsiku lonse ndapeza mavuto;

ndakhala ndi kulangidwa mmawa uliwonse.

15Ndikanati, “Ndidzayankhula motere,”

ndikanachita chosakhulupirika kwa ana anu.

16Pamene ndinayesa kuti ndimvetse zonsezi,

zinandisautsa kwambiri

17kufikira nditalowa mʼmalo opatulika a Mulungu;

pamenepo ndinamvetsa mathero awo.

18Zoonadi Inu munawayika pa malo woterera;

Mumawagwetsa pansi kuti awonongeke.

19Mwamsangamsanga iwo amawonongedwa,

amasesedwa kwathunthu ndi mantha!

20Monga loto pamene wina adzuka,

kotero pamene Inu muuka, Inu Ambuye,

mudzawanyoza ngati maloto chabe.

21Pamene mtima wanga unasautsidwa

ndi kuwawidwa mu mzimu mwanga,

22ndinali wopusa ndi wosadziwa;

ndinali chirombo chopanda nzeru pamaso panu.

23Komabe ineyo ndili ndi Inu nthawi zonse;

mumandigwira dzanja langa lamanja.

24Inu mumanditsogolera ndi malangizo anu

ndipo pambuyo pake mudzanditenga ku ulemerero.

25Kodi kumwamba ndili ndi yani kupatula Inu?

Ndipo dziko lapansi lilibe chilichonse chimene ndimachilakalaka koposa Inuyo.

26Thupi ndi mtima wanga zitha kufowoka,

koma Mulungu ndiye mphamvu ya mtima wanga

ndi cholandira changa kwamuyaya.

27Iwo amene ali kutali ndi Inu adzawonongeka;

Inu mumawononga onse osakhulupirika pamaso panu.

28Koma kunena za Ine ndi kwabwino kukhala pafupi ndi Mulungu.

Ndatsimikiza kuti Ambuye Yehova ndiwo pothawirapo panga

ndipo ndidzalalika ntchito zanu zonse.

Nueva Versión Internacional

Salmo 73:1-28

Libro III

Salmos 73–89

Salmo 73

Salmo de Asaf.

1En verdad, ¡cuán bueno es Dios con Israel,

con los de corazón puro!

2Yo estuve a punto de caer;

poco me faltó para que resbalara.

3Sentí envidia de los arrogantes,

al ver la prosperidad de esos malvados.

4Ellos no tienen ningún problema;

su cuerpo está fuerte y saludable.73:4 no … saludable. Alt. no tienen lucha alguna ante su muerte; su cuerpo está saludable.

5Libres están de los afanes de la gente;

no les afectan los infortunios humanos.

6Por eso lucen su orgullo como un collar

y hacen gala de su violencia.

7Están que revientan de malicia

y hasta se les ven sus malas intenciones.

8Ellos se burlan, hablan con maldad,

y arrogantes oprimen y amenazan.

9Con la boca increpan al cielo

y su lengua se pasea por la tierra.

10Por eso la gente acude a ellos

y bebe sus palabras como agua.

11Hasta dicen: «¿Cómo puede Dios saberlo?

¿Acaso el Altísimo tiene entendimiento?».

12Así son los malvados;

sin afanarse, aumentan sus riquezas.

13En verdad, ¿de qué me sirve mantener mi corazón limpio

y mis manos lavadas en la inocencia,

14si todo el día me golpean

y de mañana me castigan?

15Si hubiera dicho: «Voy a hablar como ellos»,

habría traicionado al linaje de tus hijos.

16Cuando traté de comprender todo esto,

me resultó una carga insoportable,

17hasta que entré en el santuario de Dios;

allí comprendí el fin que les espera:

18En verdad, los has puesto en terreno resbaladizo

y los empujas a su propia destrucción.

19¡En un instante serán destruidos,

totalmente consumidos por el terror!

20Como quien despierta de un sueño,

así, Señor, cuando tú te levantes,

los despreciarás como una ilusión.

21Se me afligía el corazón

y se me amargaba el ánimo

22por mi necedad e ignorancia.

¡Me porté contigo como una bestia!

23Pero yo siempre estoy contigo,

pues tú me sostienes de la mano derecha.

24Me guías con tu consejo

y más tarde me acogerás en gloria.

25¿A quién tengo en el cielo sino a ti?

Si estoy contigo, ya nada quiero en la tierra.

26Podrán desfallecer mi cuerpo y mi corazón,

pero Dios es la roca de mi corazón;

él es mi herencia eterna.

27Perecerán los que se alejen de ti;

tú destruyes a los que te son infieles.

28Para mí el bien es estar cerca de Dios.

He hecho del Señor Soberano mi refugio

para contar todas sus obras.