Masalimo 71 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 71:1-24

Salimo 71

1Mwa Inu Yehova ine ndathawiramo;

musalole kuti ndichititsidwe manyazi.

2Mundilanditse ndi kundipulumutsa mwa chilungamo chanu,

mutchere khutu lanu ndi kundipulumutsa.

3Mukhale thanthwe langa lothawirapo,

kumene ine nditha kupita nthawi zonse;

lamulani kuti ndipulumuke,

pakuti Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa.

4Landitseni Inu Mulungu wanga, kuchoka mʼdzanja la oyipa,

kuchoka mʼdzanja la oyipa ndi anthu ankhanza.

5Pakuti Inu mwakhala chiyembekezo changa, Inu Ambuye Wamphamvuzonse,

chilimbikitso changa kuyambira ndili mwana.

6Kuyambira pamene ndinabadwa, ndakhala ndikudalira Inu;

Inu munanditulutsa mʼmimba mwa amayi anga,

ndipo ndidzakupembedzani nthawi zonse.

7Ine ndakhala chinthu chodabwitsa kwa anthu ambiri

koma Inu ndinu wonditchinjiriza wamphamvu.

8Pakamwa panga padzaza ndi matamando anu,

kulengeza ulemerero wanu tsiku lonse.

9Musanditaye pamene ndakalamba;

musandisiye pamene mphamvu zanga zatha.

10Pakuti adani anga ayankhula motsutsana nane;

iwo amene amadikira kuti andiphe amapangana pamodzi.

11Iwo amati, “Mulungu wamusiya;

mutsatireni ndi kumugwira,

pakuti palibe amene adzamupulumutse.”

12Musakhale kutali ndi ine Inu Mulungu,

bwerani msanga, Inu Mulungu wanga; thandizeni.

13Ondineneza anga awonongeke mwa manyazi,

iwo amene akufuna kundipweteka

avale chitonzo ndi manyazi.

14Koma ine ndidzakhala ndi chiyembekezo mwa Inu nthawi zonse,

ndidzakutamandani mowirikizawirikiza.

15Pakamwa panga padzafotokoza za chilungamo chanu,

za chipulumutso chanu tsiku lonse,

ngakhale sindikudziwa muyeso wake.

16Ndidzabwera ndi kulengeza za machitidwe amphamvu zanu Inu Ambuye Wamphamvuzonse.

Ndidzalengeza chilungamo chanu, chanu chokha.

17Kuyambira ubwana wanga, Inu Mulungu mwakhala mukundiphunzitsa,

ndipo mpaka lero ine ndikulengeza za ntchito zanu zodabwitsa

18Ngakhale pamene ndakalamba ndipo imvi zili mbuu

musanditaye Inu Mulungu,

mpaka nditalengeza mphamvu zanu

kwa mibado yonse yakutsogolo.

19Mphamvu zanu ndi kulungama kwanu zimafika mpaka kumwambamwamba.

Ndani wofanana nanu Inu Mulungu,

amene mwachita zazikulu?

20Ngakhale mwandionetsa mavuto

ambiri owawa,

mudzabwezeretsanso moyo wanga;

kuchokera kunsi kwa dziko lapansi,

mudzandiukitsanso.

21Inu mudzachulukitsa ulemu wanga

ndi kunditonthozanso.

22Ndidzakutamandani ndi zeze

chifukwa cha kukhulupirika kwanu Mulungu,

ndidzayimba matamando kwa Inu ndi pangwe,

Inu Woyera wa Israeli.

23Milomo yanga idzafuwula ndi chimwemwe

pamene ndidzayimba matamando kwa Inu

amene mwandiwombola.

24Lilime langa lidzafotokoza za ntchito zanu zachilungamo

tsiku lonse,

pakuti iwo amene amafuna kundipweteka

achititsidwa manyazi ndi kusokonezedwa.

New International Version

Psalms 71:1-24

Psalm 71

1In you, Lord, I have taken refuge;

let me never be put to shame.

2In your righteousness, rescue me and deliver me;

turn your ear to me and save me.

3Be my rock of refuge,

to which I can always go;

give the command to save me,

for you are my rock and my fortress.

4Deliver me, my God, from the hand of the wicked,

from the grasp of those who are evil and cruel.

5For you have been my hope, Sovereign Lord,

my confidence since my youth.

6From birth I have relied on you;

you brought me forth from my mother’s womb.

I will ever praise you.

7I have become a sign to many;

you are my strong refuge.

8My mouth is filled with your praise,

declaring your splendor all day long.

9Do not cast me away when I am old;

do not forsake me when my strength is gone.

10For my enemies speak against me;

those who wait to kill me conspire together.

11They say, “God has forsaken him;

pursue him and seize him,

for no one will rescue him.”

12Do not be far from me, my God;

come quickly, God, to help me.

13May my accusers perish in shame;

may those who want to harm me

be covered with scorn and disgrace.

14As for me, I will always have hope;

I will praise you more and more.

15My mouth will tell of your righteous deeds,

of your saving acts all day long—

though I know not how to relate them all.

16I will come and proclaim your mighty acts, Sovereign Lord;

I will proclaim your righteous deeds, yours alone.

17Since my youth, God, you have taught me,

and to this day I declare your marvelous deeds.

18Even when I am old and gray,

do not forsake me, my God,

till I declare your power to the next generation,

your mighty acts to all who are to come.

19Your righteousness, God, reaches to the heavens,

you who have done great things.

Who is like you, God?

20Though you have made me see troubles,

many and bitter,

you will restore my life again;

from the depths of the earth

you will again bring me up.

21You will increase my honor

and comfort me once more.

22I will praise you with the harp

for your faithfulness, my God;

I will sing praise to you with the lyre,

Holy One of Israel.

23My lips will shout for joy

when I sing praise to you—

I whom you have delivered.

24My tongue will tell of your righteous acts

all day long,

for those who wanted to harm me

have been put to shame and confusion.