Masalimo 72 – CCL & NIV

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 72:1-20

Salimo 72

Salimo la Solomoni.

1Patsani mwana wa mfumu nzeru zanu zoweruzira mwa chilungamo,

Inu Mulungu mupatseni mwana wa mfumu chilungamo chanu.

2Iye adzaweruza anthu anu mwachilungamo,

anthu anu ozunzika mosakondera.

3Mapiri adzabweretsa chuma kwa anthu anu,

timapiri tidzabweretsa zipatso zachilungamo.

4Iye adzateteza ozunzika pakati pa anthu

ndi kupulumutsa ana a anthu osowa;

adzaphwanya ozunza anzawo.

5Adzakhala ndi moyo pa mibado yonse,

nthawi zonse pamene dzuwa ndi mwezi zikuwala.

6Iye adzakhala kugwa kwa mvula pa minda yolimidwa

ngati mivumbi yothirira dziko lapansi.

7Mʼmasiku a munthu wolungama adzakhazikika;

chuma chidzachuluka mpaka mwezi utaleka kuwala.

8Iye adzalamulira kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja ina

ndiponso kuchokera ku mtsinje mpaka ku malekezero a dziko lapansi.

9Mafuko a mʼchipululu adzawerama pamaso pake

ndipo adani ake adzanyambita fumbi.

10Mafumu a ku Tarisisi ndi a ku zilumba zakutali

adzabweretsa mitulo kwa iye,

mafumu a ku Seba ndi Seba

adzapereka mphatso kwa iyeyo.

11Mafumu onse adzamuweramira

ndipo mitundu yonse idzamutumikira.

12Pakuti iye adzawombola wosowa amene akulira,

wozunzika amene alibe wina womuthandiza.

13Iye adzachitira chifundo anthu ofowoka ndi anthu osowa

ndi kupulumutsa osowa ku imfa.

14Iye adzalanditsa iwo ku mazunzo ndi chiwawa

pakuti magazi awo ndi amtengo wapatali pamaso pake.

15Iye akhale ndi moyo wautali;

golide ochokera ku Seba apatsidwe kwa iye.

Anthu amupempherere nthawi zonse

ndi kumudalitsa tsiku lonse.

16Mulole kuti tirigu achuluke mʼdziko lonse;

pamwamba pa mapiri pakhale tirigu.

Zipatso zake zichuluke ngati za ku Lebanoni;

zichuluke ngati udzu wakuthengo

17Dzina lake likhazikike kwamuyaya,

lipitirire kukhala monga momwe limakhalira dzuwa.

Mitundu yonse idzadalitsika kudzera mwa iye

ndipo iwo adzamutcha iye wodala.

18Matamando akhale kwa Yehova Mulungu, Mulungu wa Israeli

amene Iye yekha amachita ntchito zodabwitsa.

19Matamando akhale ku dzina lake laulemerero kwamuyaya

dziko lonse lapansi lidzaze ndi ulemerero wake.

Ameni ndi Ameni.

20Uku ndiko kumaliza kwa mapemphero a Davide mwana wa Yese.

New International Version

Psalms 72:1-20

Psalm 72

Of Solomon.

1Endow the king with your justice, O God,

the royal son with your righteousness.

2May he judge your people in righteousness,

your afflicted ones with justice.

3May the mountains bring prosperity to the people,

the hills the fruit of righteousness.

4May he defend the afflicted among the people

and save the children of the needy;

may he crush the oppressor.

5May he endure72:5 Septuagint; Hebrew You will be feared as long as the sun,

as long as the moon, through all generations.

6May he be like rain falling on a mown field,

like showers watering the earth.

7In his days may the righteous flourish

and prosperity abound till the moon is no more.

8May he rule from sea to sea

and from the River72:8 That is, the Euphrates to the ends of the earth.

9May the desert tribes bow before him

and his enemies lick the dust.

10May the kings of Tarshish and of distant shores

bring tribute to him.

May the kings of Sheba and Seba

present him gifts.

11May all kings bow down to him

and all nations serve him.

12For he will deliver the needy who cry out,

the afflicted who have no one to help.

13He will take pity on the weak and the needy

and save the needy from death.

14He will rescue them from oppression and violence,

for precious is their blood in his sight.

15Long may he live!

May gold from Sheba be given him.

May people ever pray for him

and bless him all day long.

16May grain abound throughout the land;

on the tops of the hills may it sway.

May the crops flourish like Lebanon

and thrive72:16 Probable reading of the original Hebrew text; Masoretic Text Lebanon, / from the city like the grass of the field.

17May his name endure forever;

may it continue as long as the sun.

Then all nations will be blessed through him,72:17 Or will use his name in blessings (see Gen. 48:20)

and they will call him blessed.

18Praise be to the Lord God, the God of Israel,

who alone does marvelous deeds.

19Praise be to his glorious name forever;

may the whole earth be filled with his glory.

Amen and Amen.

20This concludes the prayers of David son of Jesse.