Masalimo 62 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 62:1-12

Salimo 62

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Kutsata mayimbidwe a Yedutuni. Salimo la Davide.

1Moyo wanga umapeza mpumulo mwa Mulungu yekha;

chipulumutso changa chimachokera kwa Iye.

2Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iye ndi linga langa, choncho sindidzagwedezeka.

3Kodi nonsenu mudzalimbana naye munthu mpaka liti?

Kodi mudzamugwetsa pansi ngati khoma losalimba,

ngati mpanda wogwedezeka?

4Iwo akufunitsitsa kumugwetsa

kuti achoke pa malo ake apamwamba.

Iwo amakondweretsedwa ndi mabodza.

Ndi pakamwa pawo amadalitsa

koma mʼmitima yawo amatemberera.

5Peza mpumulo mwa Mulungu yekhayo iwe moyo wanga;

chiyembekezo changa chichokera mwa Iye.

6Iye yekhayo ndiye thanthwe langa ndi chipulumutso changa;

Iyeyo ndi linga langa; sindidzagwedezeka.

7Chipulumutso changa ndi ulemu wanga zimachokera kwa Mulungu:

Iye ndiye thanthwe langa lamphamvu; Mulungu ndiye pothawira panga.

8Dalirani Iye nthawi zonse, inu anthu;

khuthulani mitima yanu kwa Iye,

pakuti Mulungu ndiye pothawirapo pathu.

Sela

9Anthu wamba ndi mpweya chabe;

anthu apamwamba ndi bodza chabe;

ngati atayezedwa pa sikelo iwo ndi chabe;

iwowo pamodzi ndi mpweya ndi chabe

10Musadalire kulanda mwachinyengo

kapena katundu wobedwa;

ngakhale chuma chanu chichuluke,

musayike mtima wanu pa icho.

11Mulungu wayankhula kamodzi,

ine ndamvapo zinthu ziwiri;

choyamba nʼchakuti Inu Mulungu ndinu wamphamvu,

12komanso Inu Ambuye, chikondi chanu nʼchosasinthika.

Chachiwiri nʼchakuti mumamuchitira munthu

molingana ndi ntchito zake.

Nueva Versión Internacional

Salmo 62:1-12

Salmo 62Sal 62 En el texto hebreo 62:1-12 se numera 62:2-13.

Al director musical. Para Jedutún. Salmo de David.

1Solo en Dios halla descanso mi alma;

de él viene mi salvación.

2Solo él es mi roca y mi salvación;

él es mi refugio,

¡jamás caeré!

3¿Hasta cuándo atacarán todos ustedes

a un hombre para derribarlo,

como si fuera un muro inclinado

o una cerca a punto de derrumbarse?

4Solo quieren derribarlo

de su lugar de honor.

Se complacen en la mentira:

bendicen con la boca,

pero maldicen con el corazón. Selah

5Solo en Dios halla descanso mi alma;

de él viene mi esperanza.

6Solo él es mi roca y mi salvación;

él es mi refugio,

¡no caeré!

7Dios es mi salvación y mi gloria;

es la roca que me fortalece;

mi refugio está en Dios.

8Oh, pueblo, confía en él siempre,

derrama ante él tu corazón,

pues Dios es nuestro refugio. Selah

9Una quimera es la gente de humilde cuna,

y una mentira la gente de alta alcurnia;

si se les pusiera juntos en la balanza,

pesarían menos que un soplo.

10No confíen en la extorsión

ni se hagan ilusiones con sus rapiñas;

y aunque se multipliquen sus riquezas,

no pongan el corazón en ellas.

11Una cosa ha dicho Dios

y dos veces lo he escuchado:

Que tú, oh Dios, eres poderoso;

12que tú, Señor, eres todo amor;

que tú pagarás a cada uno

según lo que merezcan sus obras.