Masalimo 61 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 61:1-8

Salimo 61

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Loyimbidwa ndi zipangizo za zingwe.

1Imvani kulira kwanga, Inu Mulungu;

mvetserani pemphero langa.

2Kuchokera ku malekezero a dziko lapansi ine ndimayitana Inu

ndimayitana pomwe mtima wanga ukufowoka;

tsogolereni ku thanthwe lalitali kuposa ineyo.

3Pakuti Inu mwakhala pothawirapo panga,

nsanja yolimba polimbana ndi adani anga.

4Ine ndikulakalaka kukhala mʼtenti yanu kwamuyaya

ndi kupeza chitetezo mu mthunzi wa mapiko anu.

5Pakuti Inu Mulungu mwamva malumbiro anga;

mwandipatsa cholowa cha iwo amene amaopa dzina lanu.

6Wonjezerani masiku a moyo wa mfumu,

zaka zake kwa mibado yochuluka.

7Iye akhale pa mpando waufumu pamaso pa Mulungu kwamuyaya;

ikani chikondi chanu ndi kukhulupirika kwanu kuti zimuteteze.

8Kotero ndidzayimba matamando kwamuyaya pa dzina lanu

ndi kukwaniritsa malumbiro anga tsiku ndi tsiku.

Hoffnung für Alle

Psalm 61:1-9

Gott, wo du wohnst, will auch ich sein

1Von David, mit Instrumenten zu begleiten.

2Höre, Gott, meinen Hilfeschrei

und achte auf mein Gebet!

3Aus weiter Ferne61,3 Wörtlich: Vom Ende der Erde. rufe ich zu dir,

denn ich bin am Ende meiner Kraft.

Ich selbst kann mich nicht mehr in Sicherheit bringen,

darum hilf du mir und rette mich!61,3 Wörtlich: Bring mich auf den Felsen, der mir zu hoch ist.

4Zu dir kann ich jederzeit fliehen;

du bist seit jeher meine Festung, die kein Feind bezwingen kann.

5Wo du wohnst,61,5 Wörtlich: In deinem Zelt. möchte auch ich für immer bleiben –

dort, in deinem Heiligtum.

Bei dir suche ich Zuflucht

wie ein Küken unter den Flügeln seiner Mutter.

6Gott, du kennst die Versprechen, die ich dir gegeben habe.

Du beschenkst jeden reich, der deinen Namen achtet und ehrt.

Auch mir gibst du meinen Anteil.

7Gib dem König ein langes Leben,

er soll über viele Generationen regieren!

8Lass ihn für immer in deiner Nähe bleiben,

beschütze ihn durch deine Güte und Treue!

9Dann will ich dich allezeit besingen und deinen Namen preisen.

Tag für Tag werde ich erfüllen, was ich dir versprochen habe.