Masalimo 60 – CCL & HOF

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 60:1-12

Salimo 60

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

1Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.

Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

2Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,

konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.

3Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;

inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

4Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera

kuti tisonkhanireko pothawa uta.

5Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

6Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.

7Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu

8Mowabu ndi mbale yanga yosambira,

pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,

pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

9Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

10Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife

ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.

11Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,

pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.

12Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano

ndipo tidzapondaponda adani athu.

Hoffnung für Alle

Psalm 60:1-14

Besiegt, aber nicht mutlos

1Ein Lied von David zur Belehrung, nach der Melodie: »Die Lilie als Zeugnis«.

2Es stammt aus der Zeit, als David mit den Aramäern von Mesopotamien und mit den Aramäern von Zoba im Krieg lag. Damals fügte Joab auf dem Rückweg den Edomitern im Salztal eine Niederlage zu, bei der 12.000 von ihnen fielen.60,2 Vgl. 2. Samuel 8,1‒14; 1. Chronik 18,3‒13. – Der Psalm wurde wahrscheinlich vor Joabs Sieg über die Edomiter gedichtet.

3Gott, du hast uns aufgegeben:

Unsere Truppen wurden zersprengt und aufgerieben.

Wir haben deinen Zorn zu spüren bekommen,

doch nun richte uns wieder auf!

4Du hast das Land erschüttert und zerrissen;

heile seine Risse, damit es nicht zerbricht!

5Du hast dein Volk hart geschlagen,

wie betrunken torkeln wir umher60,5 Wörtlich: Du hast uns einen Wein zu trinken gegeben, der uns zum Taumeln brachte..

6All denen aber, die Ehrfurcht vor dir haben,

hast du ein Warnzeichen gegeben.

So konnten sie fliehen

und den Pfeilen ihrer Verfolger entkommen.

7Befreie uns – wir sind doch dein geliebtes Volk!

Erhöre uns und komm uns zu Hilfe!

8Gott hat in seinem Heiligtum versprochen:

»Im Triumph will ich meinem Volk die Gegend um Sichem geben;

das Tal von Sukkot will ich ihnen zuteilen.

9Mir gehören die Gebiete von Gilead und Manasse,

Ephraim ist der Helm auf meinem Kopf

und Juda das Zepter in meiner Hand.

10Das Land Moab muss mir dienen, von Edom ergreife ich Besitz.60,10 Wörtlich: Moab ist mein Waschbecken, auf Edom will ich meinen Schuh werfen. – Die Bedeutung dieser Bilder ist unsicher.

Und auch du, Land der Philister, juble mir zu!«

11Mein Gott, ich frage dich nun:

Wer gibt mir Gewalt über die befestigte Stadt?

Wer schenkt mir den Sieg über Edom?

12Außer dir kommt ja niemand in Frage!

Doch gerade du, Gott, hast uns verstoßen.

Gerade du ziehst nicht mehr mit unseren Truppen in den Kampf.

13Rette uns doch vor unseren Feinden!

Denn wer sich auf Menschen verlässt, der ist verlassen!

14Aber mit Gott werden wir große Taten vollbringen;

er wird all unsere Feinde zertreten!