Masalimo 60 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 60:1-12

Salimo 60

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Kakombo wa Pangano.” Mikitamu ya Davide yophunzitsira. Pamene anamenyana ndi Mesopotamiya ndi Aramu-Zoba, ndi pamene Yowabu anabwerera ndi kukantha Aedomu 12,000 mʼChigwa cha Mchere.

1Inu Mulungu mwatikanatu ife, ndipo mwatiwonongera otiteteza.

Inu mwatikwiyira, tsopano tibwezeretseni mwakale!

2Inu mwagwedeza dziko ndipo mwalingʼamba,

konzani mingʼalu yake pakuti ikugwedezeka kwambiri.

3Inu mwaonetsa anthu anu nthawi za mavuto;

inu mwatipatsa vinyo amene watichititsa kudzandira.

4Koma kwa iwo amene amaopa Inu, Inu mwakweza mbendera

kuti tisonkhanireko pothawa uta.

5Tipulumutseni ndi kutithandiza ndi dzanja lanu lamanja,

kuti iwo amene mumawakonda apulumutsidwe.

6Mulungu wayankhula kuchokera ku malo ake opatulika:

“Mwakupambana ndidzagawa Sekemu

ndipo ndidzayeza malire a chigwa cha Sukoti.

7Giliyadi ndi wanga, Manase ndi wanganso;

Efereimu ndi chipewa changa chodzitetezera,

Yuda ndi ndodo yanga yaufumu

8Mowabu ndi mbale yanga yosambira,

pa Edomu ndidzaponyapo nsapato yanga,

pa Filisitiya ndidzafuwula mwakupambana.”

9Adzandifikitse ndani ku mzinda wotetezedwa?

Ndani adzanditsogolera ku Edomu?

10Kodi si Inu Mulungu, Inu amene mwatikana ife

ndipo simutuluka pamodzi ndi magulu athu ankhondo.

11Tipatseni chithandizo kuti tilimbane ndi mdani wathu,

pakuti thandizo lochokera kwa munthu ndi lopanda phindu.

12Chifukwa cha Mulungu, ife tidzapeza chipambano

ndipo tidzapondaponda adani athu.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 60:1-12

Salmo 60

60:5-12Sal 108:6-13

Al director musical. Sígase la tonada de «El lirio del pacto». Mictam didáctico de David, cuando luchó contra los arameos del noroeste de Mesopotamia y de Siria central, y cuando Joab volvió y abatió a doce mil edomitas en el valle de la Sal.

1Oh Dios, tú nos has rechazado

y has abierto brecha en nuestras filas;

te has enojado con nosotros:

¡restáuranos ahora!

2Has sacudido la tierra,

la has resquebrajado;

repara sus grietas,

porque se desmorona.

3Has sometido a tu pueblo a duras pruebas;

nos diste a beber un vino embriagador.

4Da60:4 Da (lectura probable); Diste (TM). a tus fieles la señal de retirada,

para que puedan escapar de los arqueros. Selah

5Líbranos con tu diestra, respóndenos

para que tu pueblo amado quede a salvo.

6Dios ha dicho en su santuario:

«Triunfante repartiré a Siquén,

y dividiré el valle de Sucot.

7Mío es Galaad, mío es Manasés;

Efraín es mi yelmo y Judá mi cetro.

8En Moab me lavo las manos,

sobre Edom arrojo mi sandalia;

sobre Filistea lanzo gritos de triunfo».

9¿Quién me llevará a la ciudad fortificada?

¿Quién me mostrará el camino a Edom?

10¿No eres tú, oh Dios, quien nos ha rechazado?

¡Ya no sales, oh Dios, con nuestros ejércitos!

11Bríndanos tu ayuda contra el enemigo,

pues de nada sirve la ayuda humana.

12Con Dios obtendremos la victoria;

¡él pisoteará a nuestros enemigos!