Masalimo 59 – CCL & NRT

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 59:1-17

Salimo 59

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide. Pamene Sauli anatumiza anthu kuti akalondere nyumba ya Davide ndi cholinga choti amuphe.

1Landitseni kwa adani anga, Inu Mulungu;

munditeteze kwa anthu amene auka kutsutsana nane.

2Landitseni kwa anthu ochita zoyipa

ndipo mundipulumutse kwa anthu okhetsa magazi.

3Onani momwe iwo akundibisalira!

Anthu owopsa agwirizana zolimbana nane;

osati chifukwa cha mlandu kapena tchimo langa, Inu Yehova.

4Ine sindinachite cholakwa, koma iwo ndi okonzeka kundithira nkhondo.

Dzukani kuti mundithandize; penyani mavuto anga!

5Inu Yehova Mulungu Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,

dzidzutseni nokha kuti mulange anthu a mitundu ina yonse;

musaonetse chifundo chanu kwa anthu oyipa achinyengowa.

6Iwo amabweranso madzulo

akuchita phokoso ngati agalu

ndi kumangoyendayenda mu mzinda.

7Onani zomwe amalavula mʼkamwa mwawo;

iwo amalavula malupanga kuchokera pa milomo yawo,

ndipo amanena kuti, “Ndani angatimve?”

8Koma Inu Yehova, mumawaseka,

mumayinyoza mitundu yonseyo.

9Inu mphamvu yanga, ine ndiyangʼana kwa inu;

Inu Mulungu, ndinu linga langa. 10Mulungu wanga wachikondi.

Mulungu adzapita patsogolo panga

ndipo adzandilola kunyada pa iwo amene amandinyoza.

11Koma musawaphe, Inu Ambuye chishango chathu,

kuopa kuti anthu anga angayiwale.

Mwa mphamvu zanu,

lolani kuti azingoyendayenda ndipo muwatsitse.

12Chifukwa cha machimo a pakamwa pawo

chifukwa cha mawu a milomo yawo,

iwo akodwe mʼkunyada kwawo.

Chifukwa cha matemberero ndi mabodza amene ayankhula

13muwawononge mu ukali (wanu)

muwawononge mpaka atheretu.

Pamenepo zidzadziwika ku malekezero a dziko lapansi

kuti Mulungu amalamulira Yakobo.

14Iwo amabweranso madzulo,

akuchita phokoso ngati agalu

ndi kumangoyenda mu mzinda.

15Iwo amayendayenda kufuna chakudya

ndipo amawuwa ngati sanakhute.

16Koma ine ndidzayimba za mphamvu yanu,

mmawa ndidzayimba zachikondi chanu;

pakuti ndinu linga langa,

pothawirapo panga mʼnthawi ya mavuto.

17Inu mphamvu yanga, ndiyimba matamando kwa inu;

Inu Mulungu, ndinu linga langa, Mulungu wanga wachikondi.

New Russian Translation

Псалтирь 59:1-14

Псалом 59

(Пс. 107:7-14)

1Дирижеру хора. На мотив «Лилия свидетельства». Мольба Давида. Для наставления. 2Написано когда Давид воевал с Арам-Нахараимом59:2 То есть с арамеями, населявшими северо-западное Междуречье. и с Арам-Цовой59:2 То есть с арамеями, населявшими центральный Арам., и когда Иоав, вернувшись, сразил двенадцать тысяч эдомитян в Соляной долине59:2 См. 2 Цар. 8–10 главы; 1 Пар. 18–19 главы..

3Ты отверг нас, Боже, и сокрушил;

Ты был в гневе – вернись к нам снова!

4Ты заставил землю дрожать и расколол ее;

исцели ее раны – она содрогается.

5Ты послал Своему народу безотрадные времена.

Ты напоил нас вином, от которого нас шатает.

6Но для тех, кто Тебя боится,

поднял Ты знамя,

чтобы они, собравшись к нему,

стали для лука недосягаемы59:6 Или: «собрались к нему ради истины».. Пауза

7Сохрани нас правой рукой Своей и ответь нам59:7 Или: «мне».,

чтобы возлюбленные Тобой спаслись.

8Бог обещал в Своем святилище:

«Я разделю, торжествуя, Шехем

и долину Суккот размерю59:8 Шехем здесь представляет всю территорию на западе от реки Иордана, а долина Суккот – на востоке..

9Мой – Галаад и Мой – Манассия,

Ефрем – Мой шлем,

Иуда – Мой скипетр59:9 Галаад – земля на востоке Иордана. Роду Манассии принадлежала часть этой земли. Роду Ефрема принадлежала земля западнее Иордана, представляющая собой северное царство Израиля. Роду Иуды принадлежала южная часть этой земли западнее Иордана..

10Моав – Моя умывальная чаша,

на Эдом Я брошу Мою сандалию59:10 В древние времена существовал обычай, символизирующий заключение сделки о земельном участке. При этом продавец давал свою сандалию покупателю. Возможно, об этом обычае и упомянуто в этом стихе.,

над землей филистимлян

торжествующе воскликну».

11Кто приведет меня в укрепленный город?

Кто доведет меня до Эдома?

12Не Ты ли, Боже, Который нас отринул,

и не выходишь с войсками нашими?

13Окажи нам помощь в борьбе с врагом,

потому что людская помощь бесполезна.

14С Богом мы одержим победу;

Он низвергнет наших врагов.