Masalimo 58 – CCL & NVI

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 58:1-11

Salimo 58

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide.

1Kodi inu olamulira mumayankhuladi molungama?

Kodi mumaweruza mwachilungamo pakati pa anthu?

2Ayi, mʼmitima mwanu mumakonzekera zosalungama,

ndipo manja anu amatulutsa zachiwawa pa dziko lapansi.

3Ngakhale kuchokera tsiku lawo lobadwa oyipa amasochera;

kuchokera mʼmimba ya amayi awo, iwo ndi otayika ndipo amayankhula mabodza.

4Ululu wawo uli ngati ululu wa njoka,

ngati uja wa mphiri imene yatseka mʼmakutu mwake.

5Imene simva liwu la munthu wamatsenga,

ngakhale akhale wa luso lotani munthu wamatsengayo.

6Gululani mano mʼkamwa mwawo, Inu Mulungu,

Yehova khadzulani mano a mikango!

7Mulole kuti asowe ngati madzi oyenda

pamene iwo akoka uta mulole kuti mivi yawo ikhale yosathwa.

8Akhale ngati nkhono imene imasungunuka pamene ikuyenda;

ngati mwana wakufa asanabadwe, iwo asaone dzuwa.

9Miphika yanu isanagwire moto waminga ya mkandankhuku,

kaya iyo ndi yobiriwira kapena yowuma, oyipa adzachotsedwa.

10Olungama adzasangalala poona kubwezera chilango,

pamene adzasambitsa mapazi awo mʼmagazi a anthu oyipa.

11Ndipo anthu adzanena kuti,

“Zoonadi, olungama amalandirabe mphotho;

zoonadi kuli Mulungu amene amaweruza dziko lapansi.”

Nueva Versión Internacional

Salmo 58:1-11

Salmo 58Sal 58 En el texto hebreo 58:1-11 se numera 58:2-12.

Al director musical. Sígase la tonada de «No destruyas». Mictam de David.

1¿Acaso ustedes, gobernantes, proclaman la justicia

y juzgan con rectitud a los seres humanos?

2¡No! Ustedes a plena conciencia cometen injusticias,

y la violencia de sus manos se esparce en el país.

3Los malvados se descarrían desde que nacen;

desde el vientre materno se desvían los mentirosos.

4Su veneno es como el de las serpientes,

como el de una cobra que cierra su oído

5para no escuchar la música de los encantadores,

del diestro en hechizos.

6Rómpeles, oh Dios, los dientes;

¡arráncales, Señor, los colmillos a esos leones!

7Que desaparezcan, como el agua que se derrama;

que se rompan sus flechas al tensar el arco.

8Que se disuelvan, como babosa rastrera;

que no vean la luz del sol, cual si fueran abortivos.

9Que sin darse cuenta, ardan como espinos;

que el vendaval los arrastre, estén verdes o secos.

10Se alegrará el justo al ver la venganza,

al empapar sus pies en la sangre del malvado.

11Dirá entonces la gente:

«Ciertamente los justos son recompensados;

ciertamente hay un Dios que juzga en la tierra».