Masalimo 57 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 57:1-11

Salimo 57

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Ndakatulo ya Davide, pamene anathawa Sauli kupita ku phanga.

1Mundichitire chifundo, Inu Mulungu mundichitire chifundo,

pakuti mwa Inu moyo wanga umathawiramo.

Ndidzathawira mu mthunzi wa mapiko anu

mpaka chiwonongeko chitapita.

2Ine ndikufuwulira kwa Mulungu Wammwambamwamba,

kwa Mulungu amene amakwaniritsa cholinga chake pa ine.

3Mulungu amanditumizira kuchokera kumwamba ndi kundipulumutsa,

kudzudzula iwo amene akundithamangitsa kwambiri.

Mulungu amatumiza chikondi chake ndi kukhulupirika kwake.

4Ine ndili pakati pa mikango,

ndagona pakati pa zirombo zolusa;

anthu amene mano awo ndi milomo yawo ndi mivi,

malilime awo ndi malupanga akuthwa.

5Mukwezekedwe Inu Mulungu, kuposa mayiko onse akumwamba;

mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

6Iwo anatchera mapazi anga ukonde

ndipo ndinawerama pansi mosautsidwa.

Anakumba dzenje mʼnjira yanga

koma agweramo okha mʼmenemo.

7Mtima wanga ndi wokhazikika, Inu Mulungu

mtima wanga ndi wokhazikika.

Ndidzayimba nyimbo, nyimbo yake yamatamando.

8Dzuka moyo wanga!

Dzukani zeze ndi pangwe!

Ndidzadzuka mʼbandakucha.

9Ndidzakutamandani Ambuye, pakati pa mitundu ya anthu,

ndidzayimba za Inu pakati pa mayiko.

10Pakuti chikondi chanu nʼchachikulu, kufikira ku mayiko akumwamba;

kukhulupirika kwanu kwafika ku mitambo.

11Mukwezekedwe Inu Mulungu kuposa mayiko akumwamba,

mulole kuti ulemerero wanu ukhale pa dziko lonse lapansi.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 57:1-11

Salmo 57

57:7-11Sal 108:1-5

Al director musical. Sígase la tonada de «No destruyas». Mictam de David, cuando David había huido de Saúl y estaba en una cueva.

1Ten compasión de mí, oh Dios;

ten compasión de mí, que en ti confío.

A la sombra de tus alas me refugiaré,

hasta que haya pasado el peligro.

2Clamo al Dios Altísimo,

al Dios que me brinda su apoyo.

3Desde el cielo me tiende la mano y me salva;

reprende a mis perseguidores. Selah

¡Dios me envía su amor y su verdad!

4Me encuentro en medio de leones,

rodeado de gente rapaz.

Sus dientes son lanzas y flechas;

su lengua, una espada afilada.

5Pero tú, oh Dios, estás sobre los cielos,

¡tu gloria cubre toda la tierra!

6Tendieron una red en mi camino,

y mi ánimo quedó por los suelos.

En mi senda cavaron una fosa,

pero ellos mismos cayeron en ella. Selah

7Firme está, oh Dios, mi corazón;

firme está mi corazón.

Voy a cantarte salmos.

8¡Despierta, alma mía!

¡Despertad, arpa y lira!

¡Haré despertar al nuevo día!

9Te alabaré, Señor, entre los pueblos,

te cantaré salmos entre las naciones.

10Pues tu amor es tan grande que llega a los cielos;

¡tu verdad llega hasta el firmamento!

11¡Tú, oh Dios, estás sobre los cielos;

tu gloria cubre toda la tierra!