Masalimo 56 – CCL & CST

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Masalimo 56:1-13

Salimo 56

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Potsata mayimbidwe a “Njiwa pa Mtengo wa Thundu wa Kutali.” Mikitamu ya Davide, pamene Afilisti anamugwira ku Gati.

1Mundichitire chifundo Inu Mulungu, pakuti anthu akundithamangitsa kwambiri;

tsiku lonse akundithira nkhondo.

2Ondinyoza akundithamangitsa tsiku lonse,

ambiri akumenyana nane monyada.

3Ndikachita mantha

ndimadalira Inu.

4Mwa Mulungu, amene mawu ake ine ndimatamanda,

mwa Mulungu ine ndimadaliramo; sindidzachita mantha.

Kodi munthu amene amafa angandichite chiyani?

5Tsiku lonse amatembenuza mawu anga;

nthawi zonse amakonza zondivulaza.

6Iwo amakambirana, amandibisalira,

amayangʼanitsitsa mayendedwe anga

ndipo amakhala ndi chidwi chofuna kuchotsa moyo wanga.

7Musalole konse kuti athawe;

mu mkwiyo wanu Mulungu mugwetse mitundu ya anthu.

8Mulembe za kulira kwanga,

mulembe chiwerengero cha misozi yanga mʼbuku lanu.

Kodi zimenezi sizinalembedwe mʼbuku lanulo?

9Adani anga adzabwerera mʼmbuyo

pamene ndidzalirira kwa Inu.

Pamenepo ndidzadziwa kuti Mulungu ali ku mbali yanga.

10Mwa Mulungu amene mawu ake ndimawatamanda,

mwa Yehova amene mawu ake ndimawatamanda,

11mwa Mulungu ine ndimadalira ndipo sindidzachita mantha.

Kodi munthu angandichite chiyani?

12Ndiyenera kuchita zomwe ndinalumbira kwa Mulungu;

ndidzapereka nsembe zanga zachiyamiko kwa inu.

13Pakuti mwawombola moyo wanga ku imfa

ndi mapazi anga kuti ndingagwe,

kuti ndiyende pamaso pa Mulungu

mʼkuwala kwa moyo.

Nueva Versión Internacional (Castilian)

Salmo 56:1-13

Salmo 56

Al director musical. Sígase la tonada de «La tórtola en los robles lejanos». Mictam de David, cuando los filisteos lo apresaron en Gat.

1Ten compasión de mí, oh Dios,

pues hay gente que me persigue.

Todo el día me atacan mis opresores,

2todo el día me persiguen mis adversarios;

son muchos los arrogantes que me atacan.

3Cuando siento miedo,

pongo en ti mi confianza.

4Confío en Dios y alabo su palabra;

confío en Dios y no siento miedo.

¿Qué puede hacerme un simple mortal?

5Todo el día tuercen mis palabras;

siempre están pensando hacerme mal.

6Conspiran, se mantienen al acecho;

ansiosos por quitarme la vida,

vigilan todo lo que hago.

7¡En tu enojo, Dios mío, humilla a esos pueblos!

¡De ningún modo los dejes escapar!

8Toma en cuenta mis lamentos;

registra mi llanto en tu libro.56:8 registra mi llanto en tu libro. Lit. pon mis lágrimas en tu frasco.

¿Acaso no lo tienes anotado?

9Cuando yo te pida ayuda,

huirán mis enemigos.

Una cosa sé: ¡Dios está de mi parte!

10Confío en Dios y alabo su palabra;

confío en el Señor y alabo su palabra;

11confío en Dios y no siento miedo.

¿Qué puede hacerme un simple mortal?

12He hecho votos delante de ti, oh Dios,

y te presentaré mis ofrendas de gratitud.

13Tú, oh Dios, me has librado de tropiezos,

me has librado de la muerte,

para que siempre, en tu presencia,

camine en la luz de la vida.